Yesaya 15 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 15:1-9

Za Kulangidwa kwa Mowabu

1Uthenga wonena za Mowabu:

Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa,

wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.

Mzinda wa Kiri wawonongedwa,

wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.

2Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo,

akupita ku malo awo achipembedzo kukalira;

anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba.

Mutu uliwonse wametedwa mpala,

ndipo ndevu zonse zametedwa.

3Mʼmisewu akuvala ziguduli;

pa madenga ndi mʼmabwalo

aliyense akulira mofuwula,

misozi ili pupupu.

4Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula,

mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi.

Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula,

ndipo ataya mtima.

5Inenso ndikulirira Mowabu;

chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari

ndi Egilati-Selisiya

akupita akulira ku chikweza cha Luhiti,

Akulira mosweka mtima

pa njira yopita ku Horonaimu;

akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.

6Madzi a ku Nimurimu aphwa

ndipo udzu wauma;

zomera zawonongeka

ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.

7Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga,

achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.

8Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu;

kulira kwawo kosweka mtima kukumveka

mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.

9Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi,

komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni,

mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu

ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.

Het Boek

Jesaja 15:1-9

Gods profetie over Moab

1Dit is Gods profetie over Moab.

Uw steden Ar en Kir zullen in één nacht worden verwoest. 2Uw onderdanen in Dibon gaan naar hun tempels om te treuren om het lot van Nebo en Medeba, zij scheren uit rouw hun hoofdhaar en hun baard af. 3In zakken gekleed lopen zij door de straten en vanuit elk huis is het geklaag van de rouwenden te horen. 4De kreten vanuit Chesbon en Eleale worden tot in Jahas vernomen. De moedigste strijders van Moab schreeuwen het uit van angst.

5Met pijn in het hart denk ik aan Moab! Haar inwoners vluchten naar Soar en Eglath-Selisia. Huilend gaan zij langs de weg naar Lubith omhoog en hun geklaag is op de weg naar Horonaïm nog te horen.

6Zelfs de Nimrim-rivier wordt een woestenij. Het gras verdort en de kwetsbare planten verwelken. 7De vertwijfelde vluchtelingen nemen alleen dat mee wat zij van hun bezittingen kunnen dragen en vluchten over de Wilgenbeek. 8In het land Moab, van het ene tot het andere eind, wordt gerouwd en geklaagd. 9Het water van de Dimon is rood gekleurd door bloed, maar Ik zal nog meer rampen over de Dimon laten gaan. Leeuwen zullen jagen op wie ontsnapte of achterbleef.