Yesaya 14 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 14:1-32

1Yehova adzachitira chifundo Yakobo;

adzasankhanso Israeli

ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo.

Alendo adzabwera kudzakhala nawo

ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.

2Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli

ku dziko lawo.

Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja

kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova.

Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo.

Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.

3Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani, 4mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti,

Wopsinja uja watha!

Ukali wake uja watha!

5Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa,

Iye waphwanya ndodo ya olamulira.

6Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali

powamenya kosalekeza,

Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali

ndikuwazunza kosalekeza.

7Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere;

ndipo akuyimba mokondwa.

8Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni

ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti,

“Chigwetsedwere chako pansi,

palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”

9Ku manda kwatekeseka

kuti akulandire ukamabwera;

mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri

a dziko lapansi, yadzutsidwa.

Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu

ayimiritsidwa pa mipando yawo.

10Onse adzayankha;

adzanena kwa iwe kuti,

“Iwenso watheratu mphamvu ngati ife;

Iwe wafanana ndi ife.”

11Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda,

pamodzi ndi nyimbo za azeze ako;

mphutsi zayalana pogona pako

ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi.

12Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba,

iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha!

Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi,

Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!

13Mu mtima mwako unkanena kuti,

“Ndidzakwera mpaka kumwamba;

ndidzakhazika mpando wanga waufumu

pamwamba pa nyenyezi za Mulungu;

ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako,

pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.

14Ndidzakwera pamwamba pa mitambo;

ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”

15Koma watsitsidwa mʼmanda

pansi penipeni pa dzenje.

16Anthu akufa adzakupenyetsetsa

nadzamalingalira za iwe nʼkumati,

“Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi

ndi kunjenjemeretsa maufumu,

17munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu,

amene anagwetsa mizinda yake

ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”

18Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu

aliyense mʼmanda akeake.

19Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako,

ngati nthambi yowola ndi yonyansa.

Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa;

amene anabayidwa ndi lupanga,

anatsikira mʼdzenje lamiyala

ngati mtembo woponderezedwa.

20Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu,

chifukwa unawononga dziko lako

ndi kupha anthu ako.

Zidzukulu za anthu oyipa

sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.

21Konzani malo woti muphere ana ake aamuna

chifukwa cha machimo a makolo awo;

kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi

ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.

22Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni.

Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo.

Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,”

akutero Yehova.

23“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu

ndiponso dambo lamatope;

ndidzawusesa ndi tsache lowononga,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

Za Kulangidwa kwa Asiriya

24Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti,

“Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho,

ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.

25Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa;

ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga;

ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga,

ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”

26Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi,

ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.

27Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse?

Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?

Za Kulangidwa kwa Afilisti

28Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:

29Musakondwere inu Afilisti nonse

kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa;

chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri,

ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.

30Osaukitsitsa adzapeza chakudya

ndipo amphawi adzakhala mwamtendere.

Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala,

ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.

31Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda!

Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse!

Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto,

ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.

32Kodi tidzawayankha chiyani

amithenga a ku Filisitiya?

“Yehova wakhazikitsa Ziyoni,

ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”