Kulangidwa Kwa Babuloni
1Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:
2Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see,
muwafuwulire ankhondo;
muwakodole kuti adzalowe pa zipata
za anthu olemekezeka.
3Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga;
ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira
amene amadzikuza ndi chipambano changa.
4Tamvani phokoso ku mapiri,
likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu!
Tamvani phokoso pakati pa maufumu,
ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi!
Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera
kuchita nkhondo.
5Iwo akuchokera ku mayiko akutali,
kuchokera kumalekezero a dziko
Yehova ali ndi zida zake za nkhondo
kuti adzawononge dziko la Babuloni.
6Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira;
lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
7Zimenezi zinafowoketsa manja onse,
mtima wa munthu aliyense udzachokamo.
8Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu,
zowawa ndi masautso zidzawagwera;
adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka.
Adzayangʼanana mwamantha,
nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.
9Taonani, tsiku la Yehova likubwera,
tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo;
kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu
ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.
10Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga
sizidzaonetsa kuwala kwawo.
Dzuwa lidzada potuluka,
ndipo mwezi sudzawala konse.
11Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake,
anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo.
Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza,
ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.
12Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino.
Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.
13Tsono ndidzagwedeza miyamba
ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake.
Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse
pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.
14Ngati mbawala zosakidwa,
ngati nkhosa zopanda wozikusa,
munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo,
aliyense adzathawira ku dziko lake.
15Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa
adzaphedwa momubaya ndi lupanga.
16Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona;
nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.
17Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva
ndipo sasangalatsidwa ndi golide,
kuti amenyane ndi Ababuloni.
18Adzapha anyamata ndi mauta awo;
sadzachitira chifundo ana
ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.
19Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse.
Anthu ake amawunyadira.
Koma Yehova adzawuwononga
ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.
20Anthu sadzakhalamonso
kapena kukhazikikamo pa mibado yonse;
palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake,
palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.
21Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko,
nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe;
mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi,
ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.
22Mu nsanja zake muzidzalira afisi,
mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe.
Nthawi yake yayandikira
ndipo masiku ake ali pafupi kutha.
A Prophecy Against Babylon
1A prophecy against Babylon that Isaiah son of Amoz saw:
2Raise a banner on a bare hilltop,
shout to them;
beckon to them
to enter the gates of the nobles.
3I have commanded those I prepared for battle;
I have summoned my warriors to carry out my wrath—
those who rejoice in my triumph.
4Listen, a noise on the mountains,
like that of a great multitude!
Listen, an uproar among the kingdoms,
like nations massing together!
The Lord Almighty is mustering
an army for war.
5They come from faraway lands,
from the ends of the heavens—
the Lord and the weapons of his wrath—
to destroy the whole country.
6Wail, for the day of the Lord is near;
it will come like destruction from the Almighty.13:6 Hebrew Shaddai
7Because of this, all hands will go limp,
every heart will melt with fear.
8Terror will seize them,
pain and anguish will grip them;
they will writhe like a woman in labor.
They will look aghast at each other,
their faces aflame.
9See, the day of the Lord is coming
—a cruel day, with wrath and fierce anger—
to make the land desolate
and destroy the sinners within it.
10The stars of heaven and their constellations
will not show their light.
The rising sun will be darkened
and the moon will not give its light.
11I will punish the world for its evil,
the wicked for their sins.
I will put an end to the arrogance of the haughty
and will humble the pride of the ruthless.
12I will make people scarcer than pure gold,
more rare than the gold of Ophir.
13Therefore I will make the heavens tremble;
and the earth will shake from its place
at the wrath of the Lord Almighty,
in the day of his burning anger.
14Like a hunted gazelle,
like sheep without a shepherd,
they will all return to their own people,
they will flee to their native land.
15Whoever is captured will be thrust through;
all who are caught will fall by the sword.
16Their infants will be dashed to pieces before their eyes;
their houses will be looted and their wives violated.
17See, I will stir up against them the Medes,
who do not care for silver
and have no delight in gold.
18Their bows will strike down the young men;
they will have no mercy on infants,
nor will they look with compassion on children.
19Babylon, the jewel of kingdoms,
the pride and glory of the Babylonians,13:19 Or Chaldeans
will be overthrown by God
like Sodom and Gomorrah.
20She will never be inhabited
or lived in through all generations;
there no nomads will pitch their tents,
there no shepherds will rest their flocks.
21But desert creatures will lie there,
jackals will fill her houses;
there the owls will dwell,
and there the wild goats will leap about.
22Hyenas will inhabit her strongholds,
jackals her luxurious palaces.
Her time is at hand,
and her days will not be prolonged.