Yesaya 13 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 13:1-22

Kulangidwa Kwa Babuloni

1Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:

2Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see,

muwafuwulire ankhondo;

muwakodole kuti adzalowe pa zipata

za anthu olemekezeka.

3Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga;

ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira

amene amadzikuza ndi chipambano changa.

4Tamvani phokoso ku mapiri,

likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu!

Tamvani phokoso pakati pa maufumu,

ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi!

Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera

kuchita nkhondo.

5Iwo akuchokera ku mayiko akutali,

kuchokera kumalekezero a dziko

Yehova ali ndi zida zake za nkhondo

kuti adzawononge dziko la Babuloni.

6Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira;

lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.

7Zimenezi zinafowoketsa manja onse,

mtima wa munthu aliyense udzachokamo.

8Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu,

zowawa ndi masautso zidzawagwera;

adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka.

Adzayangʼanana mwamantha,

nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.

9Taonani, tsiku la Yehova likubwera,

tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo;

kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu

ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.

10Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga

sizidzaonetsa kuwala kwawo.

Dzuwa lidzada potuluka,

ndipo mwezi sudzawala konse.

11Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake,

anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo.

Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza,

ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.

12Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino.

Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.

13Tsono ndidzagwedeza miyamba

ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake.

Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse

pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.

14Ngati mbawala zosakidwa,

ngati nkhosa zopanda wozikusa,

munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo,

aliyense adzathawira ku dziko lake.

15Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa

adzaphedwa momubaya ndi lupanga.

16Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona;

nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.

17Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva

ndipo sasangalatsidwa ndi golide,

kuti amenyane ndi Ababuloni.

18Adzapha anyamata ndi mauta awo;

sadzachitira chifundo ana

ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.

19Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse.

Anthu ake amawunyadira.

Koma Yehova adzawuwononga

ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.

20Anthu sadzakhalamonso

kapena kukhazikikamo pa mibado yonse;

palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake,

palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.

21Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko,

nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe;

mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi,

ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.

22Mu nsanja zake muzidzalira afisi,

mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe.

Nthawi yake yayandikira

ndipo masiku ake ali pafupi kutha.

New International Version

Isaiah 13:1-22

A Prophecy Against Babylon

1A prophecy against Babylon that Isaiah son of Amoz saw:

2Raise a banner on a bare hilltop,

shout to them;

beckon to them

to enter the gates of the nobles.

3I have commanded those I prepared for battle;

I have summoned my warriors to carry out my wrath—

those who rejoice in my triumph.

4Listen, a noise on the mountains,

like that of a great multitude!

Listen, an uproar among the kingdoms,

like nations massing together!

The Lord Almighty is mustering

an army for war.

5They come from faraway lands,

from the ends of the heavens—

the Lord and the weapons of his wrath—

to destroy the whole country.

6Wail, for the day of the Lord is near;

it will come like destruction from the Almighty.13:6 Hebrew Shaddai

7Because of this, all hands will go limp,

every heart will melt with fear.

8Terror will seize them,

pain and anguish will grip them;

they will writhe like a woman in labor.

They will look aghast at each other,

their faces aflame.

9See, the day of the Lord is coming

—a cruel day, with wrath and fierce anger—

to make the land desolate

and destroy the sinners within it.

10The stars of heaven and their constellations

will not show their light.

The rising sun will be darkened

and the moon will not give its light.

11I will punish the world for its evil,

the wicked for their sins.

I will put an end to the arrogance of the haughty

and will humble the pride of the ruthless.

12I will make people scarcer than pure gold,

more rare than the gold of Ophir.

13Therefore I will make the heavens tremble;

and the earth will shake from its place

at the wrath of the Lord Almighty,

in the day of his burning anger.

14Like a hunted gazelle,

like sheep without a shepherd,

they will all return to their own people,

they will flee to their native land.

15Whoever is captured will be thrust through;

all who are caught will fall by the sword.

16Their infants will be dashed to pieces before their eyes;

their houses will be looted and their wives violated.

17See, I will stir up against them the Medes,

who do not care for silver

and have no delight in gold.

18Their bows will strike down the young men;

they will have no mercy on infants,

nor will they look with compassion on children.

19Babylon, the jewel of kingdoms,

the pride and glory of the Babylonians,13:19 Or Chaldeans

will be overthrown by God

like Sodom and Gomorrah.

20She will never be inhabited

or lived in through all generations;

there no nomads will pitch their tents,

there no shepherds will rest their flocks.

21But desert creatures will lie there,

jackals will fill her houses;

there the owls will dwell,

and there the wild goats will leap about.

22Hyenas will inhabit her strongholds,

jackals her luxurious palaces.

Her time is at hand,

and her days will not be prolonged.