Yesaya 12 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 12:1-6

Nyimbo za Mayamiko

1Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:

“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;

chifukwa ngakhale munandipsera mtima,

mkwiyo wanu wachoka,

ndipo mwanditonthoza.

2Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;

ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.

Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;

Iye wakhala chipulumutso changa.”

3Mudzakondwera popeza Yehova

ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.

4Tsiku limenelo mudzati:

“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;

mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,

ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.

5Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;

zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.

6Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;

pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”

New Serbian Translation

Књига пророка Исаије 12:1-6

Песма захвалности

1У онај дан ти ћеш говорити:

„Хвалим те, Господе,

ти си се на мене разгневио,

али и гнев свој одвратио;

још си ме утешио.

2Ево, Бог је спасење моје,

уздам се и нећу се бојати,

јер је Господ снага моја и песма Господња,

он ми је био на спасење.“

3И радосно ћете црпсти воду

из спасоносних извора.

4Ви ћете говорити у дан онај:

„Захваљујте Господу!

Призивајте име његово!

Обзнањујте народима дела његова!

Помињите како је узвишено дело његово!

5Певајте Господу зато што је сазвао дивоту.

Нека то буде по свој земљи знано.

6Кличите и узвисујте, становници Сиона,

јер је велик међу вама Израиљев Светитељ.“