Nyimbo za Mayamiko
1Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:
“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;
chifukwa ngakhale munandipsera mtima,
mkwiyo wanu wachoka,
ndipo mwanditonthoza.
2Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;
ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
Iye wakhala chipulumutso changa.”
3Mudzakondwera popeza Yehova
ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
4Tsiku limenelo mudzati:
“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;
mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,
ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
5Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;
zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
6Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;
pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”
Песни хвалы
1В тот день ты скажешь:
– О Вечный! Славлю Тебя!
Ты гневался на меня,
но отвратил Свой гнев
и утешил меня.
2Истинно, Всевышний – спасение моё,
буду надеяться на Него и не стану бояться.
Вечный Бог – моя сила и песнь;
Он стал мне спасением.
3Радостно будете черпать воду
из колодцев спасения.
4В тот день ты скажешь:
– Славьте Вечного, имя Его призывайте;
возглашайте в народах Его деяния,
возвещайте, что велико имя Его.
5Пойте Вечному, ведь Он совершил великое;
пусть это откроется всей земле.
6Кричите и пойте от радости, жители Сиона,
потому что велик среди вас святой Бог Исраила!