Yesaya 12 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 12:1-6

Nyimbo za Mayamiko

1Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:

“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;

chifukwa ngakhale munandipsera mtima,

mkwiyo wanu wachoka,

ndipo mwanditonthoza.

2Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;

ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.

Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;

Iye wakhala chipulumutso changa.”

3Mudzakondwera popeza Yehova

ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.

4Tsiku limenelo mudzati:

“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;

mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,

ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.

5Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;

zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.

6Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;

pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”

Священное Писание

Исаия 12:1-6

Песни хвалы

1В тот день ты скажешь:

– О Вечный! Славлю Тебя!

Ты гневался на меня,

но отвратил Свой гнев

и утешил меня.

2Истинно, Всевышний – спасение моё,

буду надеяться на Него и не стану бояться.

Вечный Бог – моя сила и песнь;

Он стал мне спасением.

3Радостно будете черпать воду

из колодцев спасения.

4В тот день ты скажешь:

– Славьте Вечного, имя Его призывайте;

возглашайте в народах Его деяния,

возвещайте, что велико имя Его.

5Пойте Вечному, ведь Он совершил великое;

пусть это откроется всей земле.

6Кричите и пойте от радости, жители Сиона,

потому что велик среди вас святой Бог Исраила!