Yesaya 11 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 11:1-16

Za Ufumu Wamtendere wa Mesiya

1Padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese

ndipo nthambi idzaphukira kuchokera ku mizu yake.

2Mzimu wa Yehova udzakhala pa iye

Mzimu wanzeru ndi wa kumvetsa zinthu,

Mzimu wauphungu ndi wamphamvu,

Mzimu wachidziwitso ndi wakuopa Yehova.

3Ndipo kuopa Yehova ndiye chidzakhale chinthu chomukondweretsa.

Iye sadzaweruza potsata zooneka pamaso,

kapena kugamula mlandu potsata zakumva;

4koma amphawi adzawaweruza mwachilungamo,

adzaweruza mwachilungamo mlandu wa anthu osauka a dziko lapansi.

Iye adzakantha dziko lapansi ndi mawu ake;

atalamula Iyeyu anthu oyipa adzaphedwa.

5Chilungamo chidzakhala ngati lamba wake

ndipo kukhulupirika kudzakhala ngati chomangira mʼchiwuno mwake.

6Mʼmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa,

kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwana wambuzi,

mwana wangʼombe ndi mwana wa mkango adzadyera limodzi

ndipo mwana wamngʼono adzaziweta.

7Ngʼombe yayikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi,

ana awo adzagona pamodzi,

ndipo mkango udzadya udzu ngati ngʼombe.

8Mwana wakhanda adzasewera pa dzenje la mamba,

ndipo mwana wamngʼono adzapisa dzanja lake ku phanga la mphiri osalumidwa.

9Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena chowononga

pa phiri lopatulika la Yehova,

pakuti anthu a dziko lapansi adzadzaza ndi nzeru yotha kudziwa Yehova

monga momwe nyanja imadzazira ndi madzi.

10Tsiku limenelo mfumu yatsopano yochokera pa Muzu wa Yese idzakhala ngati chizindikiro kwa anthu a mitundu yonse. Mitundu ya anthu idzasonkhana kwa Iye, ndipo malo awo okhalapo adzakhala aulemerero. 11Tsiku limenelo Ambuye adzatambasula dzanja lake kachiwiri kuti awombole anthu ake otsalira ku Asiriya, ku Igupto, ku Patirosi, Kusi, ku Elamu, ku Sinana, ku Hamati ndi pa zilumba za nyanja yamchere.

12Adzakwezera mitundu ya anthu mbendera,

ndipo adzasonkhanitsa otayika a ku Israeli;

Iye adzasonkhanitsa anthu obalalika a ku Yuda

kuchokera ku mbali zonse zinayi za dziko lapansi.

13Nsanje ya Efereimu idzatha,

ndipo adani a Yuda adzatha;

Efereimu sadzachitira nsanje Yuda,

ngakhale Yuda sadzamuda Efereimu.

14Yuda ndi Efereimu adzathira nkhondo pa Afilisti mbali ya kumadzulo;

ndipo onsewo pamodzi adzalanda zinthu za anthu a kummawa.

Adzalimbana ndi Edomu ndi Mowabu,

ndipo Aamoni adzawagonjera.

15Yehova adzaphwetsa

mwendo wa nyanja ya Igupto;

adzatambasula dzanja lake ndipo adzawombetsa mphepo yotentha

pa mtsinje wa Yufurate.

Iye adzawugawa mtsinjewo kukhala timitsinje tisanu ndi tiwiri

kuti anthu athe kuwoloka powuma atavala nsapato.

16Padzakhala msewu waukulu woti ayendepo anthu ake otsalira

amene anatsalira ku Asiriya,

monga mmene panali msewu waukulu woyendapo Israeli

pamene amachokera ku Igupto.

Het Boek

Jesaja 11:1-16

Een nieuwe vrucht uit oude wortels

1Maar uit de stronk van Isaï, de omgehakte boom van David, zal een scheut groeien, een nieuwe vrucht bloeit op uit zijn wortels. 2En de Geest van de Here zal op Hem rusten, de Geest van wijsheid en inzicht, van raad en kracht, de Geest van kennis en van ontzag voor de Here. 3Ontzag voor de Here zal zijn lust en leven zijn. Hij zal niet rechtspreken op grond van wat aannemelijk lijkt of op grond van valse getuigenis of van horen zeggen. 4De armen en verdrukten zal Hij verdedigen. Maar Hij treft de aarde met het zwaard van zijn mond en doodt de schuldigen met zijn adem, 5want Hij zal bekleed zijn met rechtvaardigheid en trouw.

6Dan zullen de wolf en het lam bij elkaar liggen en er zal vrede heersen tussen panter en geit. Kalveren en mestvee zullen veilig tussen de leeuwen kunnen lopen en een klein kind zal hen hoeden. 7De koeien zullen tussen beren grazen, jonge beertjes zullen bij kalveren liggen en de leeuwen zullen net als de koeien gras eten. 8Babyʼs zullen veilig tussen giftige slangen kruipen en een klein kind kan rustig zijn hand in een nest met giftige adders steken. 9Op heel mijn heilige berg zal niemand schade aanrichten of iets vernietigen, want zoals het water de zee vult, zal de aarde vol zijn van de kennis van de Here.

10In die beslissende tijd zal een nakomeling van Isaï opstaan als een banier en over de volken regeren. Hun hoop zal op Hem gevestigd zijn, alle volken zullen naar Hem toekomen, want het land waar Hij woont, is een glorieuze plaats. 11In die tijd zal de Here voor de tweede keer een restant van zijn volk terugbrengen naar het land Israël. Zij zullen komen vanuit Assur, Egypte, Pathros, Ethiopië, Elam, Babel, Hamath en uit alle ver afgelegen kustlanden. 12Hij zal een banier voor hen oprichten tussen de volken waarheen ze zijn weggevoerd. Hij zal de verstrooide Israëlieten bijeenbrengen vanuit alle hoeken van de aarde. 13Dan zal er ten slotte een einde komen aan de jaloezie tussen Israël en Juda, zij zullen elkaar niet langer bestrijden. 14Samen zullen zij de volken in het oosten en het westen aanvallen. Zij zullen hun krachten bundelen om hen te vernietigen en zij zullen Edom, Moab en Ammon onderwerpen.

15De Here zal een pad door de Rode Zee droogleggen en zijn hand over de Eufraat bewegen en een machtige wind sturen die haar zal verdelen in zeven afzonderlijke beekjes die gemakkelijk kunnen worden overgestoken. 16Hij zal een gebaande weg vanuit Assur maken voor het restant dat daar is overgebleven, net zoals Hij voor heel Israël deed toen het uit Egypte terugkeerde.