Yesaya 10 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 10:1-34

1Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo,

kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,

2kuwalanda anthu osauka ufulu wawo

ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga,

amalanda zinthu za akazi amasiye

ndi kubera ana amasiye.

3Kodi mudzatani pa tsiku la chilango,

pofika chiwonongeko chochokera kutali?

Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni?

Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?

4Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa

kapena kufa pamodzi ndi ophedwa.

Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere,

mkono wake uli chitambasulire.

Chiweruzo cha Mulungu pa Asiriya

5“Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga,

iye ndiye ndodo ya mkwiyo wanga!

6Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu,

ndidzamutumiza kukalimbana ndi anthu amene amandikwiyitsa Ine,

kukafunkha ndi kulanda chuma,

ndi kuwapondereza pansi ngati matope a mʼmisewu.

7Koma izi si zimene akufuna kukachita,

izi si zimene zili mʼmaganizo mwake;

cholinga chake ndi kukawononga,

kukapulula mitundu yambiri ya anthu.

8Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’

9‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi?

Kodi Hamati sali ngati Aripadi,

nanga Samariya sali ngati Damasiko?

10Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano,

mafumu amene mafano awo ndi aakulu kupambana Yerusalemu ndi Samariya;

11nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake

monga ndinakanthira Samariya pamodzi ndi mafano ake?’ ”

12Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake. 13Pakuti mfumuyo ikuti,

“ ‘Ndachita zimenezi ndi dzanja langa,

ndiponso ndi nzeru zanga, chifukwa ndine wozindikira zinthu.

Ndinachotsa malire a mitundu ya anthu,

ndinafunkha chuma chawo;

ndinagonjetsa mafumu awo monga munthu wamphamvu.

14Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu

ngati momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame,

ngati momwe anthu amatolera mazira osiyidwa,

motero inenso ndinasonkhanitsa mayiko onse;

palibe mbalame imene inakupiza mapiko ake,

kapena kuyasama kukamwa kuti ilire.’ ”

15Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito,

kapena macheka angathe kudzikuza kupambana wowagwiritsa ntchito?

Ndiye kukhala ngati kuti chikwapu chikuzunguza munthu amene wachinyamula,

kapena ngati kuti ndodo ikuopseza amene wayinyamula!

16Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse

adzatumiza matenda owondetsa kwa ankhondo amphamvu;

kunyada kwa mfumuyo kudzapsa

ndi moto wosazima.

17Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto,

Woyera uja wa Israeli adzakhala ngati malawi a moto.

Motowo udzawatentha ndi kuwapsereza

ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi.

18Ankhondo ake adzawonongedwa

ngati nkhalango yayikulu

ndi ngati nthaka yachonde.

19Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri,

yoti ndi mwana yemwe ndi kuyiwerenga.

Aisraeli Otsala

20Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli,

opulumuka a nyumba ya Yakobo,

sadzadaliranso anthu

amene anawakantha,

koma adzadalira Yehova,

Woyerayo wa Israeli.

21Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo

adzabwerera kwa Mulungu Wamphamvu.

22Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja,

otsala okha ndiwo adzabwerere.

Chiwonongeko chalamulidwa,

chidzaonetsa chilungamo chosefukira.

23Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse

monga momwe analamulira.

24Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti,

“Inu anthu anga okhala mu Ziyoni,

musawaope Asiriya,

amene amakukanthani ndi ndodo

nakumenyani ndi zibonga monga mmene Igupto anachitira.

25Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu

ndipo ndidzaonetsa ukali wanga pa iwo mpaka kuwawononga.”

26Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu,

monga momwe anakwapulira Amidiyani ku thanthwe la Orebu;

ndipo adzatukula ndodo yake pa madzi

ndikuwalanga monga analangira Igupto pa nyanja.

27Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu,

goli lawo lidzachoka mʼkhosi mwanu;

golilo lidzathyoka

chifukwa cha kunenepa kwambiri.

28Adani alowa mu Ayati

apyola ku Migironi;

asunga katundu wawo ku Mikimasi.

29Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti,

“Tikagona ku Geba”

Rama akunjenjemera;

Gibeya, mzinda wa Saulo ukuthawa.

30Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu!

Tchera khutu, iwe Laisa!

Iwe Anatoti wosauka!

31Anthu a ku Madimena akuthawa;

anthu a ku Gebimu bisalani.

32Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu;

adzagwedeza mikono yawo,

kuopseza anthu a ku Ziyoni,

pa phiri la Yerusalemu.

33Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse,

adzadula mwamphamvu nthambi za mitengo,

mitengo yodzikweza idzadulidwa,

mitengo yayitali idzagwetsedwa.

34Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira;

Lebanoni adzagwa pamaso pa Wamphamvu.

King James Version

Isaiah 10:1-34

1Woe unto them that decree unrighteous decrees, and that write grievousness which they have prescribed;10.1 that write…: or, to the writers that write grievousness 2To turn aside the needy from judgment, and to take away the right from the poor of my people, that widows may be their prey, and that they may rob the fatherless! 3And what will ye do in the day of visitation, and in the desolation which shall come from far? to whom will ye flee for help? and where will ye leave your glory? 4Without me they shall bow down under the prisoners, and they shall fall under the slain. For all this his anger is not turned away, but his hand is stretched out still.

5¶ O Assyrian, the rod of mine anger, and the staff in their hand is mine indignation.10.5 O…: or, Woe to the Assyrian: Heb. Asshur10.5 and: or, though 6I will send him against an hypocritical nation, and against the people of my wrath will I give him a charge, to take the spoil, and to take the prey, and to tread them down like the mire of the streets.10.6 tread…: Heb. lay them a treading 7Howbeit he meaneth not so, neither doth his heart think so; but it is in his heart to destroy and cut off nations not a few. 8For he saith, Are not my princes altogether kings? 9Is not Calno as Carchemish? is not Hamath as Arpad? is not Samaria as Damascus? 10As my hand hath found the kingdoms of the idols, and whose graven images did excel them of Jerusalem and of Samaria; 11Shall I not, as I have done unto Samaria and her idols, so do to Jerusalem and her idols? 12Wherefore it shall come to pass, that when the Lord hath performed his whole work upon mount Zion and on Jerusalem, I will punish the fruit of the stout heart of the king of Assyria, and the glory of his high looks.10.12 punish: Heb. visit upon10.12 stout…: Heb. greatness of the heart 13For he saith, By the strength of my hand I have done it, and by my wisdom; for I am prudent: and I have removed the bounds of the people, and have robbed their treasures, and I have put down the inhabitants like a valiant man:10.13 a valiant…: or, many people 14And my hand hath found as a nest the riches of the people: and as one gathereth eggs that are left, have I gathered all the earth; and there was none that moved the wing, or opened the mouth, or peeped. 15Shall the axe boast itself against him that heweth therewith? or shall the saw magnify itself against him that shaketh it? as if the rod should shake itself against them that lift it up, or as if the staff should lift up itself, as if it were no wood.10.15 the rod…: or, a rod should shake them that lift it up10.15 itself, as if…: or, that which is not wood 16Therefore shall the Lord, the Lord of hosts, send among his fat ones leanness; and under his glory he shall kindle a burning like the burning of a fire. 17And the light of Israel shall be for a fire, and his Holy One for a flame: and it shall burn and devour his thorns and his briers in one day; 18And shall consume the glory of his forest, and of his fruitful field, both soul and body: and they shall be as when a standardbearer fainteth.10.18 both…: Heb. from the soul, and even to the flesh 19And the rest of the trees of his forest shall be few, that a child may write them.10.19 few: Heb. number

20¶ And it shall come to pass in that day, that the remnant of Israel, and such as are escaped of the house of Jacob, shall no more again stay upon him that smote them; but shall stay upon the LORD, the Holy One of Israel, in truth. 21The remnant shall return, even the remnant of Jacob, unto the mighty God. 22For though thy people Israel be as the sand of the sea, yet a remnant of them shall return: the consumption decreed shall overflow with righteousness.10.22 of them: Heb. in, or, among, etc10.22 with: or, in 23For the Lord GOD of hosts shall make a consumption, even determined, in the midst of all the land.

24¶ Therefore thus saith the Lord GOD of hosts, O my people that dwellest in Zion, be not afraid of the Assyrian: he shall smite thee with a rod, and shall lift up his staff against thee, after the manner of Egypt.10.24 and shall…: or, but he shall lift up his staff for 25For yet a very little while, and the indignation shall cease, and mine anger in their destruction. 26And the LORD of hosts shall stir up a scourge for him according to the slaughter of Midian at the rock of Oreb: and as his rod was upon the sea, so shall he lift it up after the manner of Egypt. 27And it shall come to pass in that day, that his burden shall be taken away from off thy shoulder, and his yoke from off thy neck, and the yoke shall be destroyed because of the anointing.10.27 be taken…: Heb. remove 28He is come to Aiath, he is passed to Migron; at Michmash he hath laid up his carriages: 29They are gone over the passage: they have taken up their lodging at Geba; Ramah is afraid; Gibeah of Saul is fled. 30Lift up thy voice, O daughter of Gallim: cause it to be heard unto Laish, O poor Anathoth.10.30 Lift…: Heb. Cry shrill with 31Madmenah is removed; the inhabitants of Gebim gather themselves to flee. 32As yet shall he remain at Nob that day: he shall shake his hand against the mount of the daughter of Zion, the hill of Jerusalem. 33Behold, the Lord, the LORD of hosts, shall lop the bough with terror: and the high ones of stature shall be hewn down, and the haughty shall be humbled. 34And he shall cut down the thickets of the forest with iron, and Lebanon shall fall by a mighty one.10.34 by…: or, mightily