Yesaya 10 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 10:1-34

1Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo,

kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,

2kuwalanda anthu osauka ufulu wawo

ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga,

amalanda zinthu za akazi amasiye

ndi kubera ana amasiye.

3Kodi mudzatani pa tsiku la chilango,

pofika chiwonongeko chochokera kutali?

Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni?

Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?

4Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa

kapena kufa pamodzi ndi ophedwa.

Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere,

mkono wake uli chitambasulire.

Chiweruzo cha Mulungu pa Asiriya

5“Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga,

iye ndiye ndodo ya mkwiyo wanga!

6Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu,

ndidzamutumiza kukalimbana ndi anthu amene amandikwiyitsa Ine,

kukafunkha ndi kulanda chuma,

ndi kuwapondereza pansi ngati matope a mʼmisewu.

7Koma izi si zimene akufuna kukachita,

izi si zimene zili mʼmaganizo mwake;

cholinga chake ndi kukawononga,

kukapulula mitundu yambiri ya anthu.

8Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’

9‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi?

Kodi Hamati sali ngati Aripadi,

nanga Samariya sali ngati Damasiko?

10Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano,

mafumu amene mafano awo ndi aakulu kupambana Yerusalemu ndi Samariya;

11nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake

monga ndinakanthira Samariya pamodzi ndi mafano ake?’ ”

12Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake. 13Pakuti mfumuyo ikuti,

“ ‘Ndachita zimenezi ndi dzanja langa,

ndiponso ndi nzeru zanga, chifukwa ndine wozindikira zinthu.

Ndinachotsa malire a mitundu ya anthu,

ndinafunkha chuma chawo;

ndinagonjetsa mafumu awo monga munthu wamphamvu.

14Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu

ngati momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame,

ngati momwe anthu amatolera mazira osiyidwa,

motero inenso ndinasonkhanitsa mayiko onse;

palibe mbalame imene inakupiza mapiko ake,

kapena kuyasama kukamwa kuti ilire.’ ”

15Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito,

kapena macheka angathe kudzikuza kupambana wowagwiritsa ntchito?

Ndiye kukhala ngati kuti chikwapu chikuzunguza munthu amene wachinyamula,

kapena ngati kuti ndodo ikuopseza amene wayinyamula!

16Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse

adzatumiza matenda owondetsa kwa ankhondo amphamvu;

kunyada kwa mfumuyo kudzapsa

ndi moto wosazima.

17Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto,

Woyera uja wa Israeli adzakhala ngati malawi a moto.

Motowo udzawatentha ndi kuwapsereza

ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi.

18Ankhondo ake adzawonongedwa

ngati nkhalango yayikulu

ndi ngati nthaka yachonde.

19Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri,

yoti ndi mwana yemwe ndi kuyiwerenga.

Aisraeli Otsala

20Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli,

opulumuka a nyumba ya Yakobo,

sadzadaliranso anthu

amene anawakantha,

koma adzadalira Yehova,

Woyerayo wa Israeli.

21Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo

adzabwerera kwa Mulungu Wamphamvu.

22Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja,

otsala okha ndiwo adzabwerere.

Chiwonongeko chalamulidwa,

chidzaonetsa chilungamo chosefukira.

23Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse

monga momwe analamulira.

24Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti,

“Inu anthu anga okhala mu Ziyoni,

musawaope Asiriya,

amene amakukanthani ndi ndodo

nakumenyani ndi zibonga monga mmene Igupto anachitira.

25Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu

ndipo ndidzaonetsa ukali wanga pa iwo mpaka kuwawononga.”

26Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu,

monga momwe anakwapulira Amidiyani ku thanthwe la Orebu;

ndipo adzatukula ndodo yake pa madzi

ndikuwalanga monga analangira Igupto pa nyanja.

27Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu,

goli lawo lidzachoka mʼkhosi mwanu;

golilo lidzathyoka

chifukwa cha kunenepa kwambiri.

28Adani alowa mu Ayati

apyola ku Migironi;

asunga katundu wawo ku Mikimasi.

29Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti,

“Tikagona ku Geba”

Rama akunjenjemera;

Gibeya, mzinda wa Saulo ukuthawa.

30Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu!

Tchera khutu, iwe Laisa!

Iwe Anatoti wosauka!

31Anthu a ku Madimena akuthawa;

anthu a ku Gebimu bisalani.

32Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu;

adzagwedeza mikono yawo,

kuopseza anthu a ku Ziyoni,

pa phiri la Yerusalemu.

33Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse,

adzadula mwamphamvu nthambi za mitengo,

mitengo yodzikweza idzadulidwa,

mitengo yayitali idzagwetsedwa.

34Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira;

Lebanoni adzagwa pamaso pa Wamphamvu.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 10:1-34

1制定不義律例、起草不公法令的人啊,

你們有禍了!

2你們冤枉窮人,

奪去我子民中困苦者的權利,

擄掠寡婦,搶劫孤兒。

3在懲罰的日子,

當災禍從遠方臨到你們頭上時,

你們怎麼辦?

你們能跑到誰那裡去求救呢?

你們能把財物藏在哪裡呢?

4你們將不是被擄就是被殺。

雖然如此,耶和華的怒氣還沒有止息,

祂降罰的手沒有收回。

主要審判亞述

5耶和華說:「亞述王有禍了!

他是我的憤怒之棍,

他手中拿著我發烈怒的杖。

6我要差遣他去攻打一個不虔敬的國家,

一個惹我發怒的民族,

去搶奪、擄掠他們的財物,

像踐踏街上的泥土一樣踐踏他們。

7可是他卻不這樣想,

心裡也不這樣盤算,

他只想毀滅許多國家。

8他說,『我的臣僕都要做藩王!

9迦勒挪豈不是和迦基米施一樣嗎?

哈馬豈不是和亞珥拔一樣嗎?

撒瑪利亞豈不是和大馬士革一樣嗎?

它們不是都被我征服了嗎?

10這些國家都在我的手中,

他們雕刻的偶像不勝過耶路撒冷撒瑪利亞的偶像嗎?

11我怎樣毀滅撒瑪利亞和它的偶像,

也必怎樣毀滅耶路撒冷和它的偶像。』」

12主完成在錫安山和耶路撒冷要做的事後,必懲罰心裡狂妄、眼目高傲的亞述王。

13因為亞述王說:

「我靠自己的力量和智慧成就了此事,

因為我很聰明。

我廢除列國的疆界,

擄掠他們的財物,

像勇士一樣征服他們的君王。

14我奪取列國的財物,

好像探囊取物;

我征服天下,

不過是手到擒來;

無人反抗,無人吭聲。」

15然而,斧頭怎能向舞動它的人自誇呢?

鋸子怎能向用鋸的人炫耀呢?

難道棍子可以揮動舉它的人嗎?

手杖可以舉起它的主人嗎?

16因此,主——萬軍之耶和華必使亞述王強健的士兵疾病纏身,

使火焰吞噬他的榮耀。

17以色列的光必成為火焰,

他們的聖者必成為烈火,

一日之間燒光亞述王的荊棘和蒺藜。

18他茂盛的樹林和肥美的田園必被徹底摧毀,

猶如病人漸漸消亡。

19林中剩下的樹木稀少,

連小孩子也能數清。

以色列的餘民

20到那日,以色列的餘民,就是雅各家的倖存者,將不再倚靠欺壓他們的亞述,他們將真心倚靠耶和華——以色列的聖者, 21重新歸向全能的上帝。 22以色列啊,你的人民雖多如海沙,將只有剩餘的人歸回。充滿公義的毀滅之事已定。 23因為主——萬軍之耶和華必按所定的在整個大地上施行毀滅。

24因此,主——萬軍之耶和華說:「我錫安的子民啊,雖然亞述人像埃及人一樣揮舞著棍棒毒打你們,你們不要懼怕。 25因為很快我就不再向你們發怒,我要向他們發怒,毀滅他們。」 26萬軍之耶和華要鞭打他們,就像在俄立磐石擊殺米甸人,就像祂向海伸杖,使海水淹沒埃及人。 27到那日,祂必除去亞述人加在你們肩頭的重擔和頸上的軛;那軛必因你們肥壯而折斷。

28亞述大軍攻佔了亞葉

穿過米磯崙

把輜重存放在密抹

29他們過了關口,

迦巴宿營。

拉瑪人戰戰兢兢,

掃羅的鄉親基比亞人倉皇逃跑。

30迦琳人啊,高聲喊叫吧!

萊煞人啊,可憐的亞拿突人啊,

留心聽吧!

31瑪得米納人逃跑,

基柄人躲藏。

32那時,亞述王必屯兵挪伯

向著錫安10·32 」希伯來文是「女子」,可能是對錫安的暱稱,下同16·152·262·11的山嶺,

向著耶路撒冷的山丘摩拳擦掌。

33看啊,主——萬軍之耶和華要以大能削去樹枝。

高大的樹必被斬斷,

挺拔的大樹必被砍倒,

34茂密的樹林必被鐵斧砍掉,

黎巴嫩的大樹也要倒在全能的上帝面前。