Yesaya 1 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 1:1-31

1Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.

Anthu Owukira

2Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi!

Pakuti Yehova wanena kuti,

“Ndinabala ana ndi kuwalera,

koma anawo andiwukira Ine.

3Ngʼombe imadziwa mwini wake,

bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake,

koma Israeli sadziwa,

anthu anga samvetsa konse.”

4Haa, mtundu wochimwa,

anthu olemedwa ndi machimo,

obadwa kwa anthu ochita zoyipa,

ana odzipereka ku zoyipa!

Iwo asiya Yehova;

anyoza Woyerayo wa Israeli

ndipo afulatira Iyeyo.

5Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe?

Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira?

Mutu wanu wonse uli ndi mabala,

mtima wanu wonse wafowokeratu.

6Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu

palibe pabwino,

paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda,

mabala ali magazi chuchuchu,

mabala ake ngosatsuka, ngosamanga

ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.

7Dziko lanu lasanduka bwinja,

mizinda yanu yatenthedwa ndi moto;

minda yanu ikukololedwa ndi alendo

inu muli pomwepo,

dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.

8Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha

ngati nsanja mʼmunda wampesa,

ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka,

ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.

9Yehova Wamphamvuzonse akanapanda

kutisiyira opulumuka,

tikanawonongeka ngati Sodomu,

tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.

10Imvani mawu a Yehova,

inu olamulira Sodomu;

mverani lamulo la Mulungu wathu,

inu anthu a ku Gomora!

11Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani

nsembe zanu zochuluka?”

“Zandikola nsembe zanu zopsereza

za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa;

sindikusangalatsidwanso

ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.

12Ndani anakulamulirani kuti

mubwere nazo pamaso panga?

Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?

13Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo!

Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine.

Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa,

kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.

14Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika

ndimadana nazo.

Zasanduka katundu wondilemera;

ndatopa kuzinyamula.

15Mukamatambasula manja anu popemphera,

Ine sindidzakuyangʼanani;

ngakhale muchulukitse mapemphero anu,

sindidzakumverani.

Manja anu ndi odzaza ndi magazi;

16sambani, dziyeretseni.

Chotsani pamaso panu

ntchito zanu zoyipa!

Lekani kuchita zoyipa,

17phunzirani kuchita zabwino!

Funafunani chilungamo,

thandizani oponderezedwa.

Tetezani ana amasiye,

muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”

18Yehova akuti,

“Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu.

Ngakhale machimo anu ali ofiira,

adzayera ngati thonje.

Ngakhale ali ofiira ngati kapezi,

adzayera ngati ubweya wankhosa.

19Ngati muli okonzeka kundimvera

mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;

20koma mukakana ndi kuwukira

mudzaphedwa ndi lupanga.”

Pakuti Yehova wayankhula.

21Taonani momwe mzinda wokhulupirika

wasandukira wadama!

Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama;

mu mzindamo munali chilungamo,

koma tsopano muli anthu opha anzawo!

22Siliva wako wasanduka wachabechabe,

vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.

23Atsogoleri ako ndi owukira,

anthu ogwirizana ndi mbala;

onse amakonda ziphuphu

ndipo amathamangira mphatso.

Iwo sateteza ana amasiye;

ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.

24Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu,

Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti,

“Haa, odana nane ndidzawatha,

ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.

25Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe;

ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa,

monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.

26Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana,

aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja.

Kenaka iweyo udzatchedwa

mzinda wolungama,

mzinda wokhulupirika.”

27Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama,

anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.

28Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi,

ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.

29“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu

imene inkakusangalatsani;

mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda

imene munayipatula.

30Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota,

mudzakhala ngati munda wopanda madzi.

31Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma,

ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali;

motero zonse zidzayakira limodzi,

popanda woti azimitse motowo.”

Nueva Versión Internacional

Isaías 1:1-31

1Visión que recibió Isaías, hijo de Amoz, acerca de Judá y Jerusalén, durante los reinados de Uzías, Jotán, Acaz y Ezequías, reyes de Judá.

Judá, nación rebelde

2¡Oigan, cielos! ¡Escucha, tierra!

Porque el Señor ha hablado:

«Yo crie hijos y los hice crecer,

pero ellos se rebelaron contra mí.

3El buey conoce a su dueño

y el asno el pesebre de su amo;

¡pero Israel no conoce,

mi pueblo no comprende!».

4¡Ay, nación pecadora,

pueblo cargado de culpa,

generación de malhechores,

hijos corruptos!

¡Han abandonado al Señor!

¡Han despreciado al Santo de Israel!

¡Le han dado la espalda!

5¿Por qué recibir más golpes?

¿Por qué insistir en la rebelión?

Toda su cabeza está herida,

todo su corazón está enfermo.

6Desde la planta del pie hasta la coronilla

no les queda nada sano:

todo en ellos es heridas, moretones

y llagas abiertas,

que no les han sido curadas, ni vendadas,

ni aliviadas con aceite.

7Su país está desolado,

sus ciudades son presa del fuego;

ante sus propios ojos

los extraños devoran sus campos;

su país está desolado, como si hubiera sido destruido por extranjeros.

8La hija Sión ha quedado

como cobertizo en un viñedo,

como choza en un huerto de pepinos,

como ciudad sitiada.

9Si el Señor de los Ejércitos

no nos hubiera dejado un remanente de sobrevivientes,

seríamos ya como Sodoma,

nos pareceríamos a Gomorra.

10¡Oigan la palabra del Señor,

gobernantes de Sodoma!

¡Escuchen la instrucción de nuestro Dios,

pueblo de Gomorra!

11«¿De qué me sirven sus muchos sacrificios?»,

dice el Señor.

«Harto estoy de holocaustos de carneros

y de la grasa de animales engordados;

la sangre de novillos, corderos y machos cabríos

no me complace.

12¿Por qué vienen a presentarse ante mí?

¿Quién les mandó traer animales

para que pisotearan mis atrios?

13No me sigan trayendo vanas ofrendas;

el incienso es para mí una abominación.

Luna nueva, día de reposo, asambleas convocadas;

¡no soporto sus asambleas que me ofenden!

14Yo aborrezco sus lunas nuevas y festividades;

se me han vuelto una carga

que estoy cansado de soportar.

15Cuando levantan sus manos,

yo aparto de ustedes mis ojos;

aunque multipliquen sus oraciones,

no las escucharé.

»¡Tienen las manos llenas de sangre!

16»¡Lávense, límpiense!

¡Aparten de mi vista sus obras malvadas!

¡Dejen de hacer el mal!

17¡Aprendan a hacer el bien!

¡Busquen la justicia y restituyan al oprimido!

¡Aboguen por el huérfano

y defiendan a la viuda!».

18«Vengan, pongamos las cosas en claro»,

dice el Señor.

«Aunque sus pecados sean como escarlata,

quedarán blancos como la nieve.

Aunque sean rojos como la púrpura,

quedarán como la lana.

19¿Están ustedes dispuestos a obedecer?

¡Comerán lo bueno de la tierra!

20¿Se niegan y se rebelan?

¡Serán devorados por la espada!».

El Señor mismo lo ha dicho.

21¡Cómo se ha prostituido la ciudad fiel!

Antes estaba llena de justicia.

La rectitud moraba en ella,

pero ahora solo quedan asesinos.

22Tu plata se ha convertido en escoria;

tu buen vino está mezclado con agua.

23Tus gobernantes son rebeldes,

cómplices de ladrones;

todos aman el soborno

y van detrás de las recompensas.

No abogan por el huérfano

ni se ocupan de la causa de la viuda.

24Por eso, afirma el Señor,

el Señor de los Ejércitos, el Poderoso de Israel:

«Me desquitaré de mis adversarios,

me vengaré de mis enemigos.

25Volveré mi mano contra ti,

limpiaré tus escorias con lejía

y quitaré todas tus impurezas.

26Restauraré a tus líderes como al principio

y a tus consejeros como al comienzo.

Entonces serás llamada

“Ciudad de justicia”,

“Ciudad fiel”».

27Con justicia Sión será redimida

y con rectitud, los que se arrepientan.

28Pero los rebeldes y pecadores a una serán quebrantados

y perecerán los que abandonan al Señor.

29«Se avergonzarán de las encinas

que ustedes tanto aman;

los jardines que eligieron

les serán una afrenta,

30como una encina con hojas marchitas,

como un jardín sin agua.

31El hombre fuerte se convertirá en estopa

y su trabajo, en chispa;

arderán los dos juntos

y no habrá quien los apague».