Yesaya 1 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 1:1-31

1Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.

Anthu Owukira

2Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi!

Pakuti Yehova wanena kuti,

“Ndinabala ana ndi kuwalera,

koma anawo andiwukira Ine.

3Ngʼombe imadziwa mwini wake,

bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake,

koma Israeli sadziwa,

anthu anga samvetsa konse.”

4Haa, mtundu wochimwa,

anthu olemedwa ndi machimo,

obadwa kwa anthu ochita zoyipa,

ana odzipereka ku zoyipa!

Iwo asiya Yehova;

anyoza Woyerayo wa Israeli

ndipo afulatira Iyeyo.

5Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe?

Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira?

Mutu wanu wonse uli ndi mabala,

mtima wanu wonse wafowokeratu.

6Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu

palibe pabwino,

paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda,

mabala ali magazi chuchuchu,

mabala ake ngosatsuka, ngosamanga

ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.

7Dziko lanu lasanduka bwinja,

mizinda yanu yatenthedwa ndi moto;

minda yanu ikukololedwa ndi alendo

inu muli pomwepo,

dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.

8Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha

ngati nsanja mʼmunda wampesa,

ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka,

ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.

9Yehova Wamphamvuzonse akanapanda

kutisiyira opulumuka,

tikanawonongeka ngati Sodomu,

tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.

10Imvani mawu a Yehova,

inu olamulira Sodomu;

mverani lamulo la Mulungu wathu,

inu anthu a ku Gomora!

11Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani

nsembe zanu zochuluka?”

“Zandikola nsembe zanu zopsereza

za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa;

sindikusangalatsidwanso

ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.

12Ndani anakulamulirani kuti

mubwere nazo pamaso panga?

Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?

13Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo!

Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine.

Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa,

kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.

14Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika

ndimadana nazo.

Zasanduka katundu wondilemera;

ndatopa kuzinyamula.

15Mukamatambasula manja anu popemphera,

Ine sindidzakuyangʼanani;

ngakhale muchulukitse mapemphero anu,

sindidzakumverani.

Manja anu ndi odzaza ndi magazi;

16sambani, dziyeretseni.

Chotsani pamaso panu

ntchito zanu zoyipa!

Lekani kuchita zoyipa,

17phunzirani kuchita zabwino!

Funafunani chilungamo,

thandizani oponderezedwa.

Tetezani ana amasiye,

muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”

18Yehova akuti,

“Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu.

Ngakhale machimo anu ali ofiira,

adzayera ngati thonje.

Ngakhale ali ofiira ngati kapezi,

adzayera ngati ubweya wankhosa.

19Ngati muli okonzeka kundimvera

mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;

20koma mukakana ndi kuwukira

mudzaphedwa ndi lupanga.”

Pakuti Yehova wayankhula.

21Taonani momwe mzinda wokhulupirika

wasandukira wadama!

Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama;

mu mzindamo munali chilungamo,

koma tsopano muli anthu opha anzawo!

22Siliva wako wasanduka wachabechabe,

vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.

23Atsogoleri ako ndi owukira,

anthu ogwirizana ndi mbala;

onse amakonda ziphuphu

ndipo amathamangira mphatso.

Iwo sateteza ana amasiye;

ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.

24Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu,

Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti,

“Haa, odana nane ndidzawatha,

ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.

25Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe;

ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa,

monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.

26Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana,

aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja.

Kenaka iweyo udzatchedwa

mzinda wolungama,

mzinda wokhulupirika.”

27Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama,

anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.

28Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi,

ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.

29“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu

imene inkakusangalatsani;

mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda

imene munayipatula.

30Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota,

mudzakhala ngati munda wopanda madzi.

31Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma,

ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali;

motero zonse zidzayakira limodzi,

popanda woti azimitse motowo.”

Священное Писание

Исаия 1:1-31

1Видение об Иудее и Иерусалиме, которое Исаия, сын Амоца, видел во времена правления Уззии, Иотама, Ахаза и Езекии, царей Иудеи1:1 Уззия, Иотам, Ахаз и Езекия правили Иудеей в период с 792 по 686 гг. до н. э. Об их правлении см. 4 Цар. 15:1-7, 32–16:20; 18–20; 2 Лет. 26–32..

Грех народа

2Слушайте, небеса! Внимай, земля!

Так говорит Вечный1:2 Вечный – на языке оригинала: «Яхве». Под этим именем Всевышний открылся Мусе и народу Исраила (см. Исх. 3:13-15). См. пояснительный словарь.:

– Я воспитал и вырастил сыновей,

а они восстали против Меня.

3Знает вол хозяина своего,

и осёл – своё стойло,

а Исраил не знает,

народ Мой не понимает.

4О грешное племя,

отягчённый грехом народ,

потомство злодеев,

сыновья растления!

Оставили Вечного,

презрели святого Бога Исраила,

повернулись к Нему спиной.

5Зачем вы так упорны в своём отступничестве?

Хотите, чтобы вас били ещё?

Вся голова ваша в ранах,

всё сердце изнурено.

6С головы до пят

нет у вас живого места,

только раны, рубцы

и открытые язвы –

не промытые, не перевязанные,

не смягчённые маслом.

7В запустении ваша страна,

сожжены дотла города.

Чужаки грабят вашу землю у вас на глазах;

в запустении всё, как после разорения чужими.

8Остался Иерусалим1:8 Букв.: «дочь Сиона» – это олицетворение Иерусалима.,

как шатёр в винограднике,

словно шалаш на бахче,

точно город в осаде.

9Если бы Вечный, Повелитель Сил,

не сохранил нам нескольких уцелевших,

то мы уподобились бы Содому,

стали бы как Гоморра1:9 См. Нач. 18:20–19:29..

10Слушайте слово Вечного,

вожди «Содома»;

внимай Закону нашего Бога,

народ «Гоморры»!

11– Что Мне множество ваших жертв? –

говорит Вечный. –

Я пресыщен всесожжениями баранов,

жиром откормленного скота;

крови телят, ягнят и козлят

Я не хочу.

12Когда вы приходите,

чтобы предстать предо Мной,

кто вас об этом просит?

Не топчите Мои дворы;

13не приносите больше бессмысленных даров;

благовония Мне противны.

Ваши Новолуния, субботы, созывы собраний1:13 Праздник Новолуния – исраильтяне, пользовавшиеся лунным календарём, праздновали начало каждого месяца, которое совпадало с новолунием (см. Чис. 28:11-15). Суббота – седьмой день недели у иудеев, день, посвящённый Вечному. В этот день, согласно повелению Вечного, исраильский народ должен был отдыхать и совершать ритуальные приношения (см. Исх. 31:12-17; Чис. 28:9-10). См. также таблицу «Праздники в Исраиле». не терплю –

это праздники с беззаконием.

14Новолуния ваши и праздники

ненавидит душа Моя.

Они стали для Меня бременем,

Я устал его нести.

15Когда вы поднимаете свои руки в молитве,

Я прячу от вас глаза,

и когда умножаете ваши молитвы,

Я не слышу.

Ваши руки полны крови;

16омойтесь, очиститесь.

Удалите свои злодеяния

с глаз Моих долой!

Перестаньте творить зло,

17научитесь делать добро!

Ищите справедливости,

обличайте угнетателя1:17 Или: «поддерживайте угнетённого».,

защищайте сироту,

заступайтесь за вдову.

18Придите же, и вместе рассудим, –

говорит Вечный. –

Пусть грехи ваши как багрянец, –

убелю их, как снег;

пусть красны они, словно пурпур, –

они будут как белая шерсть.

19Если захотите и послушаетесь,

будете есть блага земные,

20но если будете упрямыми и мятежными,

вас поглотит меч, –

так сказали уста Вечного.

21Как же это стала блудницей

некогда верная столица?!

Она была полна правосудия,

обитала в ней правда,

а теперь вот – убийцы!

22Серебро твоё стало окалиной,

вино твоё разбавлено водой.

23Твои правители – изменники

и сообщники воров;

все они любят взятки

и гоняются за подарками.

Не защищают они сироту,

дело вдовы до них не доходит.

24Поэтому Владыка Вечный, Повелитель Сил,

могучий Бог Исраила, возвещает:

– О, как Я избавлюсь от врагов,

отомщу за Себя Своим недругам!

25Руку Мою на тебя обращу;

отчищу окалину твою, точно щёлоком,

отделю от тебя все примеси.

26Я верну тебе судей, как в прежние времена,

твоих советников, как в начале.

И тогда тебя назовут

«Городом правды»,

«Столицей верной».

27Сион будет выкуплен правосудием,

раскаявшиеся жители его – праведностью.

28Но мятежники и грешники будут сокрушены,

и оставившие Вечного погибнут.

29– Вам будет стыдно из-за священных дубов,

под которыми вы желали поклоняться идолам;

вы покраснеете за священные сады,

которые вы избрали вместо Меня.

30Будете как дуб с увядшими листьями,

как сад без воды.

31Сильные станут паклей,

дело их – искрой:

вспыхнут они вместе,

и никто не потушит.