Yesaya 1 – CCL & AKCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 1:1-31

1Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.

Anthu Owukira

2Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi!

Pakuti Yehova wanena kuti,

“Ndinabala ana ndi kuwalera,

koma anawo andiwukira Ine.

3Ngʼombe imadziwa mwini wake,

bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake,

koma Israeli sadziwa,

anthu anga samvetsa konse.”

4Haa, mtundu wochimwa,

anthu olemedwa ndi machimo,

obadwa kwa anthu ochita zoyipa,

ana odzipereka ku zoyipa!

Iwo asiya Yehova;

anyoza Woyerayo wa Israeli

ndipo afulatira Iyeyo.

5Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe?

Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira?

Mutu wanu wonse uli ndi mabala,

mtima wanu wonse wafowokeratu.

6Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu

palibe pabwino,

paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda,

mabala ali magazi chuchuchu,

mabala ake ngosatsuka, ngosamanga

ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.

7Dziko lanu lasanduka bwinja,

mizinda yanu yatenthedwa ndi moto;

minda yanu ikukololedwa ndi alendo

inu muli pomwepo,

dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.

8Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha

ngati nsanja mʼmunda wampesa,

ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka,

ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.

9Yehova Wamphamvuzonse akanapanda

kutisiyira opulumuka,

tikanawonongeka ngati Sodomu,

tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.

10Imvani mawu a Yehova,

inu olamulira Sodomu;

mverani lamulo la Mulungu wathu,

inu anthu a ku Gomora!

11Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani

nsembe zanu zochuluka?”

“Zandikola nsembe zanu zopsereza

za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa;

sindikusangalatsidwanso

ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.

12Ndani anakulamulirani kuti

mubwere nazo pamaso panga?

Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?

13Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo!

Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine.

Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa,

kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.

14Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika

ndimadana nazo.

Zasanduka katundu wondilemera;

ndatopa kuzinyamula.

15Mukamatambasula manja anu popemphera,

Ine sindidzakuyangʼanani;

ngakhale muchulukitse mapemphero anu,

sindidzakumverani.

Manja anu ndi odzaza ndi magazi;

16sambani, dziyeretseni.

Chotsani pamaso panu

ntchito zanu zoyipa!

Lekani kuchita zoyipa,

17phunzirani kuchita zabwino!

Funafunani chilungamo,

thandizani oponderezedwa.

Tetezani ana amasiye,

muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”

18Yehova akuti,

“Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu.

Ngakhale machimo anu ali ofiira,

adzayera ngati thonje.

Ngakhale ali ofiira ngati kapezi,

adzayera ngati ubweya wankhosa.

19Ngati muli okonzeka kundimvera

mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;

20koma mukakana ndi kuwukira

mudzaphedwa ndi lupanga.”

Pakuti Yehova wayankhula.

21Taonani momwe mzinda wokhulupirika

wasandukira wadama!

Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama;

mu mzindamo munali chilungamo,

koma tsopano muli anthu opha anzawo!

22Siliva wako wasanduka wachabechabe,

vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.

23Atsogoleri ako ndi owukira,

anthu ogwirizana ndi mbala;

onse amakonda ziphuphu

ndipo amathamangira mphatso.

Iwo sateteza ana amasiye;

ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.

24Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu,

Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti,

“Haa, odana nane ndidzawatha,

ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.

25Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe;

ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa,

monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.

26Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana,

aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja.

Kenaka iweyo udzatchedwa

mzinda wolungama,

mzinda wokhulupirika.”

27Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama,

anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.

28Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi,

ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.

29“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu

imene inkakusangalatsani;

mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda

imene munayipatula.

30Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota,

mudzakhala ngati munda wopanda madzi.

31Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma,

ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali;

motero zonse zidzayakira limodzi,

popanda woti azimitse motowo.”

Akuapem Twi Contemporary Bible

Yesaia 1:1-31

1Saa anisoadehu a ɛfa Yuda ne Yerusalem ho no baa Amos babarima Yesaia so wɔ Yuda ahemfo Usia, Yotam, Ahas ne Hesekia mmere so.

Atuatewman

2Ɔsoro, muntie! Asase, yɛ aso!

Na Awurade akasa:

“Matetew mma ama wɔanyinyin,

nanso wɔatew me so atua.

3Nantwi nim ne wura,

afurum nso nim ne wura mmoa adididaka,

nanso Israel nnim,

me nkurɔfo nte ase.”

4Nnome nka, amumɔyɛ man,

ɔman a wɔn afɔdi so,

nnebɔneyɛfo kuw,

mma a porɔwee ahyɛ wɔn ma!

Wɔatwe wɔn ho afi Awurade ho;

wɔapo Israel Kronkronni no,

wɔadan wɔn akyi akyerɛ no.

5Adɛn nti na mopɛ sɛ wɔkɔ so boro mo?

Adɛn nti na moda so tew atua?

Wɔapira mo ti,

na mo koma nso di yaw.

6Efi mo nan ase kosi mo ti so,

ahomeka biara nni mu,

apirakuru ne ahonhon nko ara

akuru a anim deda hɔ

na wɔnhohoro so anaa wɔnkyekyeree

anaa wɔmfaa ngo nsrasraa so ɛ.

7Mo man ada mpan,

wɔde ogya ahyehyew mo nkuropɔn;

ananafo regye mo mfuw

a mo ani tua,

na asɛe sɛnea ɛyɛɛ bere a ahɔho tuu mo gui no.

8Wɔagyaw Ɔbabea Sion

te sɛ bobeturo mu sese

te sɛ akuraa a esi ɛfere afuw mu,

te sɛ kuropɔn a atamfo atwa ho ahyia.

9Sɛ Asafo Awurade

annyaw yɛn asefo a,

anka yɛayɛ sɛ Sodom,

na yɛadan ayɛ sɛ Gomora.

10Muntie Awurade asɛm,

mo Sodom sodifo;

muntie yɛn Nyankopɔn mmara,

mo Gomorafo!

11“Mo afɔrebɔ ahorow bebree no,

dɛn na ɛyɛ ma me?”

Sɛnea Awurade se ni.

“Mewɔ ɔhyew afɔrebɔde ma ɛboro so,

nea ɛyɛ adwennini ne mmoa a wɔadɔ srade;

mʼani nnye

anantwinini, nguantenmma ne mpapo mogya ho.

12Sɛ moba mʼanim a

hena na obisa eyi fi mo hɔ,

sɛ mutiatia me fi yi?

13Munnyae afɔrebɔde a ɛmfra a mode ba no!

Mo aduhuam yɛ me tan.

Ɔsram foforo, homenna ne nhyiamu ahorow,

mo nhyiamu hunu no afono me.

14Mo ɔsram foforo afahyɛ ne mo aponto a moahyehyɛ,

me kra kyi.

Ayɛ adesoa ama me;

masoa abrɛ.

15Sɛ momema mo nsa so bɔ mpae a,

meyi mʼani ato nkyɛn.

Sɛ mobɔ mpae bebree mpo a

merentie.

“Mogya bebree agu mo nsa ho fi.

16“Munnwira mo ho na mo ho ntew.

Munnyi mo nnebɔne mfi mʼani so!

Munnyae bɔneyɛ,

17Monyɛ papa! Monhwehwɛ atɛntrenee.

Monhyɛ wɔn a wɔhyɛ wɔn so nkuran

Munni mma ayisaa,

monka akunafo nsɛm mma wɔn.

18“Afei mommra na yennwen mmɔ mu,”

sɛnea Awurade se ni.

“Sɛ mo bɔne te sɛ ɔkɔben a,

ɛbɛyɛ fitaa sɛ sukyerɛmma;

mpo sɛ ɛyɛ kɔkɔɔ te sɛ mogya a

ɛbɛyɛ fitaa sɛ asaawa mfuturu.

19Sɛ mopene so na moyɛ osetie a,

mubedi asase no so nnepa.

20Na sɛ moampene na motew atua a,

afoa bedi mo nam.”

Awurade na wakasa.

21Hwɛ sɛnea kuropɔn nokwafo no

adan oguamanfo.

Bere bi, na atɛntrenee ahyɛ no ma

na anka trenee te ne mu,

nanso mprempren, awudifo ahyɛ mu ma!

22Wo dwetɛ adan ade a so nni mfaso,

wɔde nsu afra wo nsa papa mu.

23Wo sodifo yɛ atuatewfo,

akorɔmfo yɔnkonom;

wɔn nyinaa pɛ adanmude,

na wɔpere akyɛde ho.

Wonni mma ayisaa;

na akunafo nsɛm nkɔ wɔn anim.

24Enti, Awurade, Asafo Awurade,

nea ɔyɛ Ɔkɛse ma Israel no ka se,

“Aa, menya ahomegye afi mʼatamfo hɔ

na matɔ wɔn so were.

25Mɛma me nsa so, atia mo;

mɛhohoro mo ho fi korakora

na mayi mo ho nkekae nyinaa.

26Mɛma mo atemmufo bio sɛ kan no,

ne mo afotufo sɛnea na ɛte, mfiase no.

Eyi akyi no, wɔbɛfrɛ wo

Kuropɔn Trenee,

Kuropɔn Nokwafo.”

27Wɔde atɛntrenee begye Sion bio,

na wɔn a wonu wɔn ho no, wɔde trenee begye wɔn.

28Nanso atuatewfo ne nnebɔneyɛfo de, wɔbɛdwerɛw wɔn abɔ mu,

na wɔn a wɔpa Awurade akyi bɛyera.

29“Mo ani bewu, esiane odum anyame a

munyaa wɔn mu anigye no;

wobegu mo anim ase, esiane nturo

a mosom abosom wɔ mu no nti.

30Mobɛyɛ sɛ odum a ne nhaban apo,

ne turo a ennya nsu.

31Ɔhoɔdenfo bɛyɛ sɛ ade a ɛhyew ntɛm

nʼadwuma bɛyɛ sɛ ogya a aturuw;

abien no bɛhyew abɔ mu,

a obiara rentumi nnum.”