Yeremiya 9 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 9:1-26

1Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi,

ndi maso anga ngati kasupe wa misozi!

Ndikanalira usana ndi usiku

kulirira anthu anga amene aphedwa.

2Ndani adzandipatsa malo

ogona mʼchipululu

kuti ndiwasiye anthu anga

ndi kuwachokera kupita kutali;

pakuti onse ndi achigololo,

ndiponso gulu la anthu onyenga.

3“Amapinda lilime lawo ngati uta.

Mʼdzikomo mwadzaza

ndi mabodza okhaokha

osati zoonadi.

Amapitirirabe kuchita zoyipa;

ndipo sandidziwa Ine.”

Akutero Yehova.

4“Aliyense achenjere ndi abwenzi ake;

asadalire ngakhale abale ake.

Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu.

Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.

5Aliyense amamunamiza mʼbale wake

ndipo palibe amene amayankhula choonadi.

Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza;

amalimbika kuchita machimo.

6Iwe wakhalira mʼchinyengo

ndipo ukukana kundidziwa Ine,”

akutero Yehova.

7Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa.

Kodi ndingachite nawonso

bwanji chifukwa cha machimo awo?

8Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa;

limayankhula zachinyengo.

Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake,

koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.

9Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi?

akutero Yehova.

‘Kodi ndisawulipsire

mtundu wotere wa anthu?’ ”

10Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri

ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu.

Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako,

ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe.

Mbalame zamlengalenga zathawa

ndipo nyama zakuthengo zachokako.

11Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja,

malo okhalamo ankhandwe;

ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda

kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”

12Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”

13Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala. 14Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.” 15Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu. 16Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”

17Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere;

itanani akazi odziwa kulira bwino.”

18Anthu akuti, “Abwere mofulumira

kuti adzatilire

mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi

ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.

19Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti,

‘Aa! Ife tawonongeka!

Tachita manyazi kwambiri!

Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu

chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’ ”

20Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova;

tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova.

Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni;

aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.

21Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu

ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa;

yapha ana athu mʼmisewu,

ndi achinyamata athu mʼmabwalo.

22Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti,

“ ‘Mitembo ya anthu

idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda,

ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola,

popanda munthu woyitola.’ ”

23Yehova akuti,

“Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake,

kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake,

kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,

24koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi:

kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa,

kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo,

chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi.

Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,”

akutero Yehova.

25“Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe. 26Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 9:1-26

1真希望我的頭是水泉,

眼是淚泉,

好為我被殺的同胞晝夜哭泣;

2真希望我在曠野有棲身之處,

以便遠離我的同胞,

因為他們是一群不忠不貞之徒。

3耶和華說:

「他們鼓舌如簧,射出謊言,

遍地充滿詭詐,毫無誠實;

他們行惡不斷,

不認我是上帝。

4你們要提防鄰居,

不要信賴弟兄,

因為弟兄詭計多端,

鄰居滿口是非。

5他們彼此欺騙,不說真話;

他們說謊成性,

不知疲倦地肆意犯罪;

6他們充滿詭詐,

不認我是上帝。

這是耶和華說的。」

7因此,萬軍之耶和華說:

「看啊,我要熬煉、試驗這些罪惡的子民,

除此之外,我別無選擇。

8他們舌如毒箭,說話詭詐,

對鄰居口蜜腹劍。

9難道我不該懲罰他們嗎?

難道我不該報應這樣的民族嗎?

這是耶和華說的。」

10我要為眾山悲傷痛哭,

為曠野的草原唱哀歌,

因為那裡一片荒涼,杳無人跡,

聽不見牲畜的叫聲,

飛鳥和走獸也逃去無蹤。

11耶和華說:「我要使耶路撒冷淪為廢墟,

成為豺狼出沒之地;

我要使猶大的城邑荒涼,

不見人煙。」

12誰有智慧明白這事呢?誰曾受過耶和華的指教可以講解這事呢?為什麼這片土地被蹂躪,變得荒涼、杳無人跡? 13耶和華說:「這是因為他們棄絕我賜給他們的律法,不聽從我的話,不遵守我的命令, 14執迷不悟,隨從他們祖先的教導去供奉巴力。」 15因此,以色列的上帝——萬軍之耶和華說:「看啊,我要使這百姓吃苦艾,喝毒藥; 16我要把他們分散到他們及其祖先都不認識的列國;我要使敵人追殺他們,直到滅絕他們。」

17萬軍之耶和華說:

「把陪哭的婦人請來,

把最會哭的婦人帶來,

18叫她們速來為我的子民哀哭,

哭得他們淚盈滿眶,

哭得他們淚如泉湧。

19因為從錫安傳出哀鳴,

『我們滅亡了!

我們受了奇恥大辱!

我們的家園被毀,

我們只好背井離鄉。』」

20婦人啊,你們要聽耶和華的話,

接受祂的教誨;

你們要教導女兒哀哭,

教導鄰居唱輓歌。

21因為死亡從窗戶爬進我們的城堡,

吞滅街上的孩童和廣場上的青年。

22耶和華說:「人們必屍橫遍野,

像散佈在田野上的糞便,

又像收割者身後沒有收集的禾捆。」

23耶和華說:「智者不要誇耀自己的智慧,勇士不要誇耀自己的力量,富人不要誇耀自己的財富。 24若有人誇耀,就讓他誇耀自己認識我是耶和華,知道我喜歡在地上憑慈愛、公平和正義行事。這是耶和華說的。」 25耶和華說:「看啊,時候將到,我要懲罰所有只在身體受過割禮的人, 26就是埃及人、猶大人、以東人、亞捫人、摩押人和所有住在曠野、剃了鬢髮的人,因為這些人,包括以色列人,都沒有受過真正的割禮,沒有受過內心的割禮。」