Yeremiya 8 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 8:1-22

1Yehova akuti, “ ‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa. 2Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka. 3Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’ ”

Tchimo ndi Chilango Chake

4“Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti:

“ ‘Kodi anthu akagwa sangadzukenso?

Munthu akasochera kodi sangathe kubwereranso?

5Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera?

Chifukwa chiyani Yerusalemu akubwerera mʼmbuyo?

Iwo akangamira chinyengo;

akukana kubwerera.

6Ine ndinatchera khutu kumvetsera

koma iwo sanayankhulepo zoona.

Palibe woyipa amene analapapo zoyipa zake,

nʼkumati, ‘Ine ndachita chiyani?’

Aliyense akutsatira njira yake

ngati kavalo wothamangira nkhondo.

7Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa

nthawi yake mlengalenga.

Koma nkhunda, namzeze ndi chingalu

zimadziwa nthawi yonyamukira ulendo,

koma anthu anga sadziwa

malamulo a Yehova.

8“ ‘Inu mukunena bwanji kuti,

‘Ndife anzeru ndipo timasunga malamulo a Yehova?’

Koma ndi alembi anu

amene akulemba zabodza.

9Anthu anzeru achita manyazi;

athedwa nzeru ndipo agwidwa.

Iwo anakana mawu a Yehova.

Nanga tsono nzeru zawo ziwapinduliranji?

10Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena

ndipo minda yawo ndidzayipereka kwa amene adzawagonjetse.

Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,

onse ali ndi khalidwe lofuna kupeza chuma mwakuba.

Aneneri pamodzi ndi ansembe omwe,

onse amachita zachinyengo.

11Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga

pamwamba chabe

nʼkumati, ‘Mtendere, mtendere,’

pamene palibe mtendere.

12Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi?

Ayi, alibe manyazi ndi pangʼono pomwe;

iwo sadziwa nʼkugwetsa nkhope komwe.

Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale;

adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalanga,

akutero Yehova.

13“ ‘Ndidzatenga zokolola zawo,

Sipadzakhalanso mphesa pa mpesa

kapena nkhuyu pa mkuyu,

ndipo masamba ake adzawuma.

Zinthu zimene ndinawapatsa

ndidzawachotsera.’ ”

14Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani?

Tiyeni tonse pamodzi

tithawire ku mizinda yotetezedwa

ndi kukafera kumeneko.

Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa.

Watipatsa madzi aululu kuti timwe,

chifukwa tamuchimwira.

15Tinkayembekezera mtendere

koma palibe chabwino chomwe chinachitika,

tinkayembekezera kuchira

koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.

16Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani

kukumveka kuchokera ku Dani;

dziko lonse likunjenjemera

chifukwa cha kulira kwa akavalowo.

Akubwera kudzawononga dziko

ndi zonse zimene zili mʼmenemo.

Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”

17Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu,

mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza,

ndipo zidzakulumani,”

18Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri,

mtima wanga walefukiratu.

19Imvani kulira kwa anthu anga

kuchokera ku dziko lakutali:

akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni?

Kodi mfumu yake sili kumeneko?”

“Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema,

ndi milungu yawo yachilendo?”

20“Nthawi yokolola yapita,

chilimwe chapita,

koma sitinapulumuke.”

21Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa;

ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.

22Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa?

Kodi kumeneko kulibe singʼanga?

Nanga chifukwa chiyani mabala

a anthu anga sanapole?

Hoffnung für Alle

Jeremia 8:1-23

1Es kommt der Tag, da wird man die Gebeine der Könige und führenden Männer von Juda, die Gebeine der Priester und Propheten, ja, aller Einwohner von Jerusalem wieder aus den Gräbern holen. Darauf gebe ich, der Herr, mein Wort! 2Man wird sie ausstreuen vor der Sonne, dem Mond und den Sternen, ihren geliebten Göttern, denen sie gehorsam dienten, die sie befragt und angebetet haben. Keiner wird die Gebeine je wieder einsammeln und begraben, sie werden zu Dünger auf dem Acker. 3Die wenigen Menschen, die ich von diesem treulosen Volk noch übrig lasse und in fremde Länder vertreibe, wollen dann lieber tot als lebendig sein. Das sage ich, der Herr, der allmächtige Gott!«

Ein Volk rennt ins Verderben

4»Sag ihnen: So spricht der Herr: Wenn jemand hingefallen ist, steht er gleich wieder auf, und wenn einer vom Weg abkommt, kehrt er gern wieder um. 5Warum verlässt dann dieses Volk immer wieder den richtigen Weg? Warum geht Jerusalem ständig in die Irre? Sie klammern sich an ihre trügerischen Götter und weigern sich beharrlich, zu mir umzukehren. 6Ich habe genau gehört, was sie reden: Die Wahrheit ist es nicht! Keiner bereut seine schlechten Taten und sagt: ›Was habe ich getan!‹ Alle rennen auf ihrem falschen Weg weiter wie Schlachtrosse, die in den Kampf stürmen. 7Selbst ein Storch weiß, wann er zurückkehren muss; Taube, Schwalbe und Drossel kommen zur rechten Zeit wieder. Nur mein Volk weiß nicht, welche Ordnungen ich ihm gegeben habe.

8Ihr behauptet: ›Wir sind weise, wir besitzen ja das Gesetz des Herrn!‹ Aber eure Gesetzeslehrer haben es durch ihre Auslegung völlig verdreht. 9Eure Weisen werden sich schämen und zu Tode erschrecken, wenn das Unheil sie einholt. Denn sie haben mein Wort abgelehnt – welche Weisheit bleibt ihnen da noch?

10Darum werde ich eure Frauen anderen Männern geben und eure Äcker neuen Besitzern. Ihr alle, vom einfachen Volk bis zu den Mächtigen, wollt nur eines: Gewinn um jeden Preis! Auch die Priester und Propheten betrügen euch, 11weil sie eure tiefen Wunden nur schnell verbinden. ›Es ist halb so schlimm, alles wird wieder gut!‹, sagen sie. Nein, nichts wird gut!8,11 Wörtlich: Sie sagen: ›Friede, Friede!‹, und da ist doch kein Friede!

12Schämen müssten sie sich über ihre abscheulichen Taten, aber sie kennen keine Scham mehr, sie werden nicht einmal rot! Doch wenn die Zeit gekommen ist, werden sie stürzen; wenn ich sie strafe, werden sie mit allen anderen in Israel untergehen. Darauf gebe ich, der Herr, mein Wort.

13Mit Stumpf und Stiel werde ich sie ausrotten, denn sie sind wie ein schlechter Weinstock,8,13 Oder: Wenn ich bei meinem Volk ernten will, dann sind sie wie ein schlechter Weinstock. – Der hebräische Text ist nicht sicher zu deuten. der keine Trauben hat, und wie ein Feigenbaum, der keine Früchte hervorbringt, ja, selbst die Blätter sind welk! Darum werde ich Feinde schicken, die ihnen auch das Letzte noch nehmen!

14›Warum sitzen wir hier unschlüssig herum?‹, fragen die Leute von Juda. ›Kommt, wir ziehen uns in die befestigten Städte zurück. Lieber sterben wir dort als hier! Der Herr, unser Gott, hat uns ja doch zum Tod verurteilt; vergiftetes Wasser gibt er uns zu trinken, weil wir gegen ihn gesündigt haben. 15Wir hofften, alles werde wieder gut – doch vergeblich! Wir dachten, die Wunden unseres Volkes würden heilen – aber wir erleben nichts als Schrecken! 16Die Feinde haben bereits die Stadt Dan erreicht. Schon hören wir das Schnauben und Wiehern ihrer Pferde. Das ganze Land erbebt davon. Die Feinde kommen und werden alles vernichten: unsere Felder und was darauf wächst, unsere Städte und ihre Bewohner!‹

17Ich, der Herr, sage: Ich lasse Schlangen auf euch los, giftige Ottern, die ihr nicht beschwören könnt, und sie werden euch beißen!«

Jeremia leidet an seinem Volk

(Kapitel 8,18–12,17)

Jeremia beweint sein Volk

18Niemand kann mich trösten! Der Kummer hat mich überwältigt und macht mich ganz krank! 19Hört, wie mein Volk überall im Land verzweifelt schreit: »Wohnt der Herr nicht mehr auf dem Berg Zion, regiert er dort nicht mehr als König?« Und er antwortet: »Warum habt ihr mich mit euren Götzenstatuen herausgefordert und fremde Götter verehrt, die euch doch nicht helfen können?«

20Das Volk klagt: »Der Sommer ist vergangen, die Ernte ist vorüber, und noch immer ist keine Rettung in Sicht!«

21Wenn ich mit ansehe, wie mein Volk zerbricht, dann bricht es auch mir das Herz. Ich trauere und bin völlig niedergeschlagen. 22Gibt es denn in Gilead keine Salben mehr, ist dort kein Arzt zu finden? Warum heilen die Wunden meines Volkes nicht? 23Ich wünschte, mein Kopf wäre ein Brunnen und meine Augen Tränenquellen, dann würde ich unsere Toten Tag und Nacht beweinen!