Yeremiya 7 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 7:1-34

Chipembedzo Chabodza Nʼchopanda Phindu

1Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa, 2“Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu:

“ ‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova. 3Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano. 4Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’ 5Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama, 6ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni, 7Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya. 8Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.

9“Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe, 10ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi? 11Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”

12“ ‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli. 13Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha, 14choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo. 15Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’ ”

16“Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera. 17Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu? 18Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima. 19Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”

20“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.

21“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo! 22Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo, 23koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino. 24Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo. 25Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri. 26Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.

27“Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha. 28Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’

29“Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”

Chigwa cha Imfa

30“Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa. 31Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe. 32Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika. 33Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse. 34Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иеремия 7:1-34

Иеремия пророчествует в храме

1Слово Вечного, которое было к Иеремии:

2– Встань у ворот дома Вечного и провозгласи там следующее: Слушай слово Вечного, весь народ Иудеи, идущий через эти ворота для поклонения Вечному. 3Так говорит Вечный, Повелитель Сил, Бог Исроила: «Оставьте свои злые пути и дела, и Я позволю вам жить на этом месте. 4Не полагайтесь на лживые слова: „Здесь храм Вечного, храм Вечного, храм Вечного!“ 5Если вы действительно оставите свои нечестивые мысли и дела и будете поступать друг с другом справедливо, 6если не будете притеснять чужеземцев, сирот и вдов и проливать невинную кровь на этом месте, если не будете себе же во вред следовать за чужими богами, 7то Я позволю вам жить на этом месте, на земле, которую Я дал вашим предкам навеки.

8Но вот вы полагаетесь на лживые слова, в которых нет прока. 9Вы крадёте и убиваете, нарушаете супружескую верность и лжесвидетельствуете, возжигаете благовония Баалу и следуете за чужими богами, которых прежде не знали, 10а потом приходите, встаёте предо Мной в этом доме, который называется Моим именем, и говорите: „Мы спасены“ – лишь для того, чтобы вновь совершать все эти мерзости? 11Разве вы не превратили дом, который называется Моим именем, в разбойничье логово? Но Я всё это вижу, – возвещает Вечный.

12Пойдите в Моё святилище в Шило, где Я прежде устроил дом для поклонения Мне, и посмотрите, что Я с ним сделал за злодеяния Моего народа Исроила7:12 В Шило во время завоевания Ханона и правления судей находился священный шатёр с сундуком соглашения. Но когда иудеи отвернулись от Всевышнего, этот город был разрушен филистимлянами примерно в 1050 г. до н. э., а сундук соглашения был захвачен (см. 1 Цар. 4:1-11; ср. Заб. 77:56-64).. 13Пока вы предавались этим порокам, – возвещает Вечный, – Я снова и снова говорил с вами, а вы не слушали; Я звал вас, а вы не отвечали. 14То же, что Я сделал с Шило, Я сделаю и с домом, который называется Моим именем, с храмом, на который вы полагаетесь, с местом, которое Я дал вам и вашим отцам. 15Я отвергну вас от Себя, как отверг ваших братьев, народ Ефраима»7:15 Ефраим – так часто называли Северное царство – Исроил, где наиболее влиятельным был род Ефраима..

Непокорство народа

16– А ты не молись за этот народ, не проси за них в молитвах; не умоляй Меня, Я не стану тебя слушать. 17Разве ты не видишь, что они делают в городах Иудеи и на улицах Иерусалима? 18Дети собирают дрова, отцы разводят огонь, а женщины месят тесто и пекут лепёшки для богини неба7:18 Богиня неба – скорее всего, здесь имеется в виду Астарта, ханонская богиня любви и плодородия.. Они совершают жертвенные возлияния чужим богам, чтобы разгневать Меня. 19Но Мне ли они делают хуже? – возвещает Вечный. – Нет, самим себе, к своему стыду!

20Поэтому так говорит Владыка Вечный:

– Мой яростный гнев обрушится на эту землю, на людей и скот, на деревья в поле и на плоды земли, он будет пылать, не угасая.

21Так говорит Вечный, Повелитель Сил, Бог Исроила:

– Ваши жертвы не угодны Мне! Так что ешьте мясо жертв сами, даже то, которое нужно полностью сжечь7:21 См. таблицу «Жертвоприношения в Исроиле» на странице ##.. 22Ведь когда Я вывел ваших предков из Египта, Я не просто говорил и давал им повеления о всесожжениях и жертвах, 23но и повелел им: «Слушайтесь Меня, и Я буду вашим Богом, а вы – Моим народом. Исполняйте то, что Я вам велю, и тогда вы будете благополучны». 24Но они не послушали и не вняли Моим словам, и по своему упрямству жили по собственным замыслам, шли назад, а не вперёд. 25С того дня, как ваши предки покинули Египет, и до этого дня, день за днём, снова и снова Я посылал к вам Моих рабов пророков. 26Но вы не слушали и не внимали им. Вы были упрямыми и делали ещё больше зла, чем ваши предки.

27Когда ты будешь говорить им всё это, они не станут тебя слушать, и когда будешь звать их, они не ответят. 28Поэтому скажи им: «Вот народ, который не слушается Вечного, своего Бога, и не принимает наставлений. Истина погибла, она исчезла с их уст. 29Обрей свои волосы и выбрось; подними на голых вершинах плач, потому что Вечный отверг и покинул поколение, которое Его разгневало».

Долина Бойни

30– Народ Иудеи делал зло в Моих глазах, – возвещает Вечный. – Они поставили своих ничтожных идолов в доме, который называется Моим именем, осквернив его. 31В долине Бен-Гинном они приготовили место для жертвоприношений, которое называется Тофет, чтобы сжигать там своих сыновей и дочерей, чего Я не повелевал, о чём даже не думал. 32Но теперь приближаются дни, – возвещает Вечный, – когда люди будут называть эту долину уже не Тофетом или долиной Бен-Гинном, а долиной Бойни, так как в Тофете будут хоронить мёртвых до тех пор, пока там не останется места. 33Трупы этого народа станут пищей птицам в небе и зверям на земле, и некому будет их отпугнуть. 34Я положу конец крикам радости и веселья, не слышны будут в городах Иудеи и на улицах Иерусалима голоса невесты и жениха, потому что страна будет опустошена.