Yeremiya 6 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 6:1-30

Kuzingidwa kwa Yerusalemu

1“Thawani, inu anthu a ku Benjamini!

Tulukani mu Yerusalemu!

Lizani lipenga ku Tekowa!

Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu!

Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto,

ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.

2Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri,

kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?

3Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo;

adzamanga matenti awo mowuzinga,

ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”

4Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo!

Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano.

Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka,

ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.

5Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno

ndi kuwononga malinga ake!”

6Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Dulani mitengo

ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu.

Mzinda umenewu uyenera kulangidwa;

wadzaza ndi kuponderezana.

7Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi

ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake.

Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo;

nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.

8Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro,

kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere

ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja

mopanda munthu wokhalamo.”

9Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti,

“Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli,

monga momwe amachitira populula mphesa.

Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe

monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”

10Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza?

Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve?

Makutu awo ndi otsekeka

kotero kuti sangathe kumva.

Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo;

sasangalatsidwa nawo.

11Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova,

ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova.

Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu

ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi;

pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa,

pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.

12Nyumba zawo adzazipereka kwa ena,

pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo.

Ndidzatambasula dzanja langa kukantha

anthu okhala mʼdzikomo,”

akutero Yehova.

13“Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,

onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba;

aneneri pamodzi ndi ansembe omwe,

onse amachita zachinyengo.

14Amapoletsa zilonda za anthu anga

pamwamba pokha.

Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’

pamene palibe mtendere.

15Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo?

Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe;

sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe.

Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale;

adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,”

akutero Yehova.

16Yehova akuti,

“Imani pa mphambano ndipo mupenye;

kumeneko ndiye kuli njira zakale,

funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo,

ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu.

Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’

17Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni

ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’

koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’

18Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina;

yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano,

chimene chidzawachitikire anthuwo.

19Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi,

ndikubweretsa masautso pa anthu awa.

Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo.

Iwowa sanamvere mawu anga

ndipo anakana lamulo langa.

20Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba,

kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali?

Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira;

nsembe zanu sizindikondweretsa.”

21Choncho Yehova akuti,

“Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa.

Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa;

anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”

22Yehova akunena kuti,

“Taonani, gulu lankhondo likubwera

kuchokera kumpoto;

mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka

kuchokera kumathero a dziko lapansi.

23Atenga mauta ndi mikondo;

ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo.

Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja.

Akwera pa akavalo awo

ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo,

kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”

24A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo,

ndipo manja anthu alefukiratu.

Nkhawa yatigwira,

ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.

25Musapite ku minda

kapena kuyenda mʼmisewu,

pakuti mdani ali ndi lupanga,

ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.

26Inu anthu anga, valani ziguduli

ndipo gubudukani pa phulusa;

lirani mwamphamvu

ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha,

pakuti mwadzidzidzi wowonongayo

adzabwera kudzatipha.

27“Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo.

Uwayese anthu anga

monga ungayesere chitsulo

kuti uwone makhalidwe awo.

28Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira

ndipo akunka nanena zamiseche.

Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo.

Onse amangochita zoyipa zokhazokha.

29Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri;

mtovu watha kusungunuka ndi moto.

Koma ntchito yosungunulayo sikupindula

chifukwa zoyipa sizikuchokapo.

30Iwo ali ngati siliva wotayidwa,

chifukwa Yehova wawakana.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米书 6:1-30

耶路撒冷被围

1便雅悯人啊,你们要逃离耶路撒冷

你们要在提哥亚吹响号角,

伯·哈基琳发出警报,

因为有大灾难从北方逼近。

2我要毁灭美丽娇弱的锡安城。

3敌人必围攻她,

在她周围安营扎寨,

如同牧人带着羊群在她四周搭起帐篷。

4他们喊道,‘准备作战!

我们中午攻城。’

他们后来说,

‘唉!日已西沉,天色渐暗。

5起来吧,我们要乘夜攻打她,

毁灭她的宫殿。’”

6万军之耶和华说:

“你们要砍伐树木,

修筑高台围攻耶路撒冷

因为这城充满压迫,

该受惩罚。

7她的邪恶如同泉水涌流不息,

暴力和毁灭层出不穷,

疾病和伤痛接连不断。

8耶路撒冷啊,你要接受告诫,

否则我要离弃你,

使你荒无人烟。”

叛逆的以色列人

9万军之耶和华说:

“敌人要把以色列的余民掳掠一空,

如同人摘葡萄摘得一个不剩。”

10我可以警告谁呢?谁会听呢?

他们耳朵闭塞,什么也听不见!

看啊,耶和华的话逆耳,

他们毫不喜欢。

11耶和华啊,我怒你所怒,

无法容忍。

耶和华说:“你把我的怒气发向街头的孩童和聚集成群的青年。

丈夫、妻子和老人都要一同被掳。

12他们的房屋、田地和妻子都要被抢占。

我要伸手攻击这地方的居民。

这是耶和华说的。

13因为他们无论贵贱,

个个都贪图不义之财;

无论是先知还是祭司,

都行为诡诈。

14他们敷衍了事地医治我子民的伤痛,

说,‘没事了,没事了!’

其实情况很糟。

15他们做可憎的事会羞愧吗?

不!他们不知廉耻,

毫不脸红。

因此,他们要与其他人一样灭亡,

死在我的惩罚下。

这是耶和华说的。”

16耶和华说:

“你们要站在路口观望,

寻访古道,

找到正路并行在其上,

便会得到心灵的安宁。”

但你们却说:“我们拒绝这样做。”

17耶和华说:“我为你们设立守望者,

提醒你们要听号角声。”

但你们却说:“我们不听。”

18因此,耶和华说:

“列国啊,你们要听!

众见证人啊,要知道这些百姓的结局!

19地啊,听着!

我要降灾祸给这些百姓。

他们是自作自受,

因为他们没有听从我的话,

拒绝遵守我的律法。

20示巴运来乳香,

从远方带来菖蒲献给我,

有什么用呢?

我不悦纳他们的燔祭,

不喜欢他们的牲畜。”

21因此,耶和华说:

“我要把绊脚石放在他们前面,

使父子一同绊倒,

邻居和朋友一同灭亡。”

22耶和华说:

“看啊,有一个民族从北方来,

有一个强国从地极发动进攻。

23他们残酷无情,毫无怜悯,

手持弓箭长枪,

骑马奔来,声势如狂涛怒吼。

锡安城啊,他们准备列阵攻击你。”

24我们听到这风声,手脚发软,

痛苦万分,

如分娩的妇人。

25不要去田野,

不要在路上走,

因为外面危机四伏,

仇敌杀气腾腾。

26百姓啊,你们要身披麻布,

在灰中打滚;

你们要悲伤痛哭,如丧独子,

因为毁灭者将突然临到我们。

27耶和华对我说:

“我派你考验我的子民,

就像冶炼金属一样,

好察验他们的行为。

28他们顽固不化,

如铜如铁,

四处毁谤,

极其败坏。

29风箱猛力吹火,铅也会熔掉;

但他们被炼了又炼,终是徒然,

因为他们的邪恶仍未除去。

30他们被称为废弃的银渣,

因为耶和华已丢弃他们。”