Yeremiya 5 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 5:1-31

Palibe Munthu Wolungama

1“Pitani uku ndi uku mʼmisewu ya Yerusalemu,

mudzionere nokha,

funafunani mʼmabwalo ake.

Ngati mungapeze munthu mmodzi

amene amachita zachilungamo ndi kufunafuna choonadi,

ndipo ndidzakhululukira mzinda uno.

2Ngakhale anthu akulumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’

komabe akungolumbira mwachinyengo.”

3Inu Yehova, kodi suja mumafuna anthu onena zoona?

Inu munawakantha anthuwo, koma sanamve kupweteka;

munawaphwanya anthuwo, koma sanatengepo phunziro.

Anawumitsa mitima yawo ngati mwala

ndipo anakaniratu kulapa.

4Ndiye ndinati, “Awa ndi amphawi chabe;

anthu ochita zopusa.

Sadziwa njira ya Yehova,

sazindikira zimene Mulungu wawo amafuna.

5Tsono ndidzapita kwa atsogoleri

ndi kukayankhula nawo;

ndithu iwo amadziwa njira ya Yehova,

amadziwa zomwe Mulungu wawo amafuna.”

Koma ayi, iwonso anathyola goli la Yehova

ndipo anadula msinga zawo.

6Choncho mkango wochokera ku nkhalango udzawapha,

mmbulu wochokera ku thengo udzawawononga,

kambuku adzawabisalira pafupi ndi mizinda yawo

kuti akhadzule aliyense amene adzayesera kutuluka mʼmizindamo

pakuti kuwukira kwawo ndi kwakukulu

ndipo abwerera mʼmbuyo kwambiri.

7Yehova akuti, “Kodi ndingakukhululukireni bwanji ndi zimene mwachita?

Ana anu andisiya Ine

ndipo amapembedza milungu imene si milungu konse.

Ine ndinawapatsa zonse zimene ankasowa,

komabe iwo anachita chigololo

namasonkhana ku nyumba za akazi achiwerewere.

8Monga amachitira akavalo onenepa akamamemesa,

aliyense wa iwo ankathamangira mkazi wa mnzake.

9Tsono ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?”

akutero Yehova.

“Kodi nʼkuleka kuwulipsira

mtundu woterewu?

10“Pitani ku minda yake ya mipesa ndi kukayiwononga,

koma musakayiwononge kotheratu.

Sadzani nthambi zake

pakuti anthu amenewa si a Yehova.

11Nyumba ya Israeli ndi nyumba ya Yuda

onse akhala osakhulupirika kotheratu kwa Ine.”

12Iwowa ankanama ponena za Yehova kuti,

“Yehova sangachite zimenezi!

Choyipa sichidzatigwera;

sitidzaona nkhondo kapena njala.

13Mawu a aneneri azidzangopita ngati mphepo;

ndipo mwa iwo mulibe uthenga wa Yehova.

Choncho zimene amanena zidzawachitikira okha.”

14Chifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akuti,

“Popeza kuti anthu awa ayankhula mawu amenewa,

tsono mawu anga ndidzawasandutsa moto mʼkamwa mwako

ndipo anthu awa ndidzawasandutsa nkhuni zimene moto udzapserezeretu.

15Inu Aisraeli,” Yehova akuti,

“Ndikukubweretserani mtundu wa anthu ochokera kutali,

ndi mtundu umene sunagonjetsedwepo,

mtundu wakalekale umene chiyankhulo chawo inu simuchidziwa,

zimene akunena inu simungazimvetse.

16Zida zawo za nkhondo zapha anthu ambirimbiri;

onsewo ndi ankhondo amphamvu okhaokha.

17Adzakudyerani zokolola zanu ndi chakudya chanu,

adzapha ana anu aamuna ndi aakazi;

adzakupherani nkhosa zanu ndi ngʼombe zanu,

adzawononga mpesa wanu ndi mikuyu yanu.

Ndi malupanga awo adzagwetsa

mizinda yanu yotetezedwa imene mumayidalira.

18“Komabe pa masiku amenewo sindidzakuwonongani kotheratu,” akutero Yehova. 19Ndipo pamene anthu adzafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani Yehova Mulungu wathu wachita zimenezi?” Iwe udzawawuze kuti, “Monga momwe mwasiyira Ine ndi kutumikira milungu yachilendo mʼdziko mwanu, momwemonso mudzatumikira anthu a mʼdzikonso lachilendo.”

20“Lengeza izi kwa ana a Yakobo

ndipo mulalikire kwa anthu a ku Yuda kuti,

21Imvani izi, inu anthu opusa ndi opanda nzeru,

inu amene maso muli nawo koma simupenya,

amene makutu muli nawo koma simumva.

22Kodi simuyenera kuchita nane mantha?”

Akutero Yehova.

“Kodi simuyenera kunjenjemera pamaso panga?

Ine ndinayika mchenga kuti ukhale malire a nyanja,

malire a muyaya amene nyanjayo singadutsepo.

Mafunde angawombe motani, koma sangathe kupitirira malirewo;

mafunde angakokome motani, koma sangadutse malirewo.

23Koma anthu awa ndi nkhutukumve ndiponso a mitima yowukira;

andifulatira ndipo andisiyiratu.

24Sananenepo mʼmitima mwawo kuti,

‘Tiyeni tizipembedza Yehova Mulungu wathu.

Kodi suja amatipatsa pa nthawi yake mvula yachizimalupsa ndi yamasika.

Iye salephera konse kutipatsa nyengo ya kholola.’

25Koma zolakwa zanu zalepheretsa zonsezi;

ndipo machimo anu akumanitsani zabwino.

26“Pakati pa anthu anga pali anthu ena oyipa

amene amabisalira anzawo monga amachitira mlenje mbalame

ndiponso ngati amene amatchera misampha kuti akole anthu anzawo.

27Nyumba zawo zadzaza ndi chuma chochipeza mwa chinyengo

ngati zikwere zodzaza ndi mbalame.

Nʼchifukwa chake asanduka otchuka ndi olemera.

28Ndipo ananenepa ndi kukhala ndi matupi osalala.

Ntchito zawo zoyipa nʼzopanda malire;

saweruza mwachilungamo nkhani ya ana amasiye kuti iyende bwino,

sateteza ufulu wa anthu osauka.

29Kodi Ine ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?

Kodi ndisawulipsire

mtundu woterewu?

Akutero Yehova.

30“Chinthu chothetsa nzeru ndi choopsa kwambiri

chachitika mʼdzikomo:

31Aneneri akunenera zabodza,

ndipo ansembe akuvomerezana nawo,

ndipo anthu anga akukonda zimenezi.

Koma mudzatani potsiriza?

Hoffnung für Alle

Jeremia 5:1-31

Keine Vergebung mehr!

1Gott sagt: »Geht doch einmal durch die Straßen von Jerusalem und schaut euch um! Sucht alle Plätze ab! Wenn ihr auch nur einen Einzigen findet, der sich an das Recht hält und zu seinem Wort steht, dann will ich ganz Jerusalem vergeben. 2Denn die Leute in dieser Stadt lügen selbst dann noch, wenn sie bei meinem Namen schwören.«

3Doch du, Herr, suchst nach aufrichtigen Menschen. Du hast dieses Volk geschlagen, aber sie haben sich nicht davon beeindrucken lassen; du hast sie fast ausgelöscht, und doch blieben sie hart wie Stein. Sie weigern sich beharrlich, zu dir umzukehren. 4Ich dachte: »So sind nur die Ungebildeten, die den Willen des Herrn und die Gebote ihres Gottes nicht kennen. 5Ich will mich an die führenden Männer dieses Volkes wenden und mit ihnen reden. Sie kennen ja den Willen Gottes und wissen, was er im Gesetz von ihnen verlangt.« Doch gerade sie wollen von Gott nichts mehr wissen. Seine Gebote sind für sie wie ein schweres Joch, das sie abgeworfen haben.

6»Darum werden die Feinde kommen und sie zerreißen wie Löwen, die plötzlich aus dem Dickicht springen, wie Steppenwölfe werden sie über sie herfallen und wie Leoparden draußen vor der Stadt lauern. Wer hinausgeht, wird zerfleischt. Denn dieses Volk hat große Schuld auf sich geladen und mir immer wieder die Treue gebrochen.

7Wie sollte ich euch da vergeben? Ihr habt mich verlassen und schwört bei Göttern, die keine sind. Ich habe euch genug zu essen gegeben – und ihr? Ihr treibt Ehebruch und lauft scharenweise ins Hurenhaus! 8Ihr seid wie überfütterte, geile Hengste: Jeder wiehert nach der Frau des anderen. 9Und das sollte ich ungestraft lassen, ich, der Herr? Muss ich ein solches Volk nicht zur Rechenschaft ziehen? 10Zerstört die Mauern dieses Weinbergs, doch verwüstet ihn nicht ganz. Reißt seine Ranken ab, denn er gehört mir nicht mehr!«

Ich ziehe euch zur Rechenschaft

11»Ich, der Herr, sage: Die Bewohner von Juda und Israel sind mir ganz und gar untreu geworden. 12Mich, ihren Herrn, haben sie verleugnet, als sie behaupteten: ›Er kümmert sich um nichts! Uns wird schon kein Unglück treffen. Von Krieg und Hungersnot bleiben wir verschont. 13Was die Propheten uns angedroht haben, ist leeres Geschwätz! Gott spricht nicht durch sie. Das Unheil soll sie selbst treffen!‹«

14Doch der Herr, der allmächtige Gott, hat zu mir gesagt: »Weil dieses Volk so vermessen redet, lasse ich die Worte, die ich dir in den Mund gelegt habe, zu einem Feuersturm werden. Das Volk mache ich zu Brennholz, das vom Feuer verzehrt wird. 15Hört, ihr Israeliten, ich sorge dafür, dass ein Volk von weit her kommt und in euer Land einfällt. Das Volk ist sehr viel älter als ihr, es ist unbezwingbar, und seine Sprache versteht ihr nicht. 16Seine Bogenschützen treffen mit tödlicher Sicherheit, und die Soldaten sind alle erfahrene Kämpfer. 17Dieses Volk wird eure Ernte und eure Vorräte vernichten, eure Söhne und Töchter töten, eure Schafe und Rinder schlachten und eure Weinstöcke und Feigenbäume umhauen. Eure befestigten Städte, auf die ihr euch verlasst, wird es blutig erobern.

18Doch auch dann werde ich euch nicht völlig auslöschen. Darauf gebe ich, der Herr, mein Wort. 19Und wenn sie dich, Jeremia, fragen: ›Warum hat uns der Herr, unser Gott, dies angetan?‹, dann sollst du antworten: ›Ihr habt ihn verlassen und in eurem eigenen Land fremden Göttern gedient, nun müsst ihr in einem anderen Land fremden Herren dienen!‹

20Verkündet den Nachkommen von Jakob, sagt dem Volk von Juda: 21Hört, ihr Leute ohne Sinn und Verstand! Ihr habt Augen und Ohren, und trotzdem seht und hört ihr nicht! 22Ich, der Herr, frage euch: Solltet ihr mich nicht fürchten und vor mir zittern? Ich habe dem Meer eine Grenze aus Sand gesetzt, die es niemals überschreiten kann. Wie wild seine Wellen auch toben, wie hoch die Wogen sich auch türmen – über die Grenze kommen sie nicht hinaus.

23Aber ihr wagt es, euch gegen mich aufzulehnen, und geht eigene Wege. Ihr seid stur und widerspenstig. 24Keiner von euch sagt sich: ›Wir sollten dem Herrn, unserem Gott, mit Ehrfurcht begegnen! Denn er sendet uns den Herbst- und Frühjahrsregen zur rechten Zeit und lässt Jahr für Jahr die Früchte reifen, damit wir sie ernten können.‹ 25Aber nun sind Regen und Ernte ausgeblieben; eure eigene Schuld hat euch um all diese guten Gaben gebracht!

26Ja, in meinem Volk gibt es gewissenlose Menschen, die wie Vogelfänger auf der Lauer liegen. Sie warten darauf, dass ihnen Menschen in die Falle laufen. 27Ihre Häuser sind vollgestopft wie der Käfig eines Vogelfängers, sie häufen dort ihren Besitz auf, den sie mit Trug und List erbeutet haben. Mächtig und reich sind sie geworden, 28fett und feist. Ihre Bosheit kennt keine Grenzen. Sie verhelfen keinem Waisenkind zu seinem Recht, den Armen verweigern sie jede Gerechtigkeit. 29Und das sollte ich ungestraft lassen, ich, der Herr? Muss ich ein solches Volk nicht zur Rechenschaft ziehen?

30Was in diesem Land geschieht, ist abscheulich und unerhört: 31Die Propheten weissagen im Namen der Lüge, die Priester herrschen eigenmächtig, und meinem Volk gefällt das auch noch. Doch was werdet ihr tun, wenn das Ende kommt?«