Yeremiya 49 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 49:1-39

Uthenga Wonena za Aamoni

1Yehova ananena izi:

Amoni,

“Kodi Israeli alibe ana aamuna?

Kapena alibe mlowamʼmalo?

Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi?

Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?

2Koma nthawi ikubwera,”

akutero Yehova,

“pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo

ku Raba, likulu la Amoni;

ndipo malo awo opembedzera milungu yawo

adzatenthedwa ndi moto.

Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo

kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,”

akutero Yehova.

3“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika!

Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba!

Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu;

thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga,

chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo,

pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.

4Chifukwa chiyani mukunyadira

chigwa chanu,

inu anthu osakhulupirika

amene munadalira chuma chanu nʼkumati:

‘Ndani angandithire nkhondo?’

5Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe

zochokera kwa onse amene akuzungulira,”

akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse.

“Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake.

Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.

6“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,”

akutero Yehova.

Uthenga Wonena za Edomu

7Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu:

“Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani?

Kodi anzeru analeka kupereka uphungu?

Kodi nzeru zawo zinatheratu?

8Inu anthu a ku Dedani, thawani,

bwererani ndi kukabisala ku makwalala

chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau

popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.

9Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu

akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?

Anthu akuba akanafika usiku

akanangotengako zimene akuzifuna zokha?

10Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau.

Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo,

kotero kuti sadzathanso kubisala.

Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka.

Palibe wonena kuti,

11‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza.

Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’ ”

12Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho. 13Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”

14Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova:

Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti,

“Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu!

Konzekerani nkhondo!”

15“Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina.

Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.

16Kuopseza kwako kwakunyenga;

kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,

iwe amene umakhala mʼmapanga

a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri.

Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga,

ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”

akutero Yehova.

17“Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha.

Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo

chifukwa cha kuwonongeka kwake.

18Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora,

pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,”

akutero Yehova,

“motero palibe munthu

amene adzakhala mu Edomu.

19“Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani

kupita ku malo a msipu wobiriwira,

Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo.

Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine.

Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani?

Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”

20Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova

ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani.

Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo

ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.

21Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera;

kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.

22Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka

nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.

Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu

idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.

Uthenga Wonena za Damasiko

23Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa:

“Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha

chifukwa amva nkhani yoyipa.

Mitima yawo yagwidwa ndi mantha

ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.

24Anthu a ku Damasiko alefuka.

Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa

chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu.

Ali ndi nkhawa komanso mantha

ngati za mayi pa nthawi yake yochira.

25Mzinda wotchuka

ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!

26Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa;

ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

27“Ndidzatentha malinga a Damasiko;

moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”

Uthenga Wonena za Kedara ndi Hazori

28Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa:

“Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara.

Kawonongeni anthu a kummawako.

29Landani matenti awo ndi nkhosa zawo,

ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo.

Mutengenso ngamira zawo.

Anthu adzafuwula kwa iwo kuti,

‘Kuli zoopsa mbali zonse!’

30“Thawani mofulumira!

Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,”

akutero Yehova.

“Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu;

wakonzekera zoti alimbane nanu.

31“Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere,

umene ukukhala mosatekeseka,”

akutero Yehova,

“mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo;

anthu ake amakhala pa okha.

32Ngamira zawo zidzafunkhidwa,

ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa.

Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali.

Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,”

akutero Yehova.

33“Hazori adzasanduka bwinja,

malo okhalamo nkhandwe

mpaka muyaya.

Palibe munthu amene adzayendemo.”

Uthenga Wonena za Elamu

34Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:

35Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu,

umene uli chida chawo champhamvu.

36Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu

kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga;

ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi,

ndipo sipadzakhala dziko

limene anthu a ku Elamu sadzafikako.

37A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo

komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo.

Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga

ndipo adzakhala pa mavuto,”

akutero Yehova.

“Ndidzawapirikitsa ndi lupanga

mpaka nditawatheratu.

38Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu

ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,”

akutero Yehova.

39“Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera

anthu a ku Elamu dziko lawo,”

akutero Yehova.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иеремия 49:1-39

Пророчество об Аммоне

1Об аммонитянах.

Так говорит Вечный:

– Разве нет у Исроила сыновей?

Разве нет у него наследника?

Почему же Гадом завладел Молох49:1 Или: «их царь»; также в ст. 3. Молох – аммонитский бог, в жертвы которому приносились дети.,

и народ его живёт в городах Гада?

2Но настанут дни, –

возвещает Вечный, –

когда по Моей воле прозвучит боевой клич

под аммонитской столицей Рабба.

Она превратится в груду развалин,

и окрестные селения сгорят дотла.

Тогда Исроил прогонит тех,

кто прогнал его, –

возвещает Вечный. –

3Плачь, Хешбон, так как разрушен Гай!

Голосите, жители Раббы!

Оденьтесь в рубище,

рыдайте и ходите вдоль стен,

потому что Молох уходит в плен

со своими священнослужителями и знатью.

4Что ты хвастаешься долинами?

Что ты кичишься плодородными долинами?49:4 Или: «Твоя долина уничтожена»; или: «Потекла твоя долина кровью»; или: «Утекает сила твоя».

Дочь-отступница, ты уповаешь на сокровища,

говоря: «Кто против меня выступит?»

5Я нагоню на тебя страх

со всех сторон, –

возвещает Владыка Вечный, Повелитель Сил, –

всех вас разгонят,

и никто не соберёт бегущих.

6Но после этого Я верну аммонитянам благополучие, –

возвещает Вечный.

Пророчество об Эдоме

7Об Эдоме.

Так говорит Вечный, Повелитель Сил:

– Разве нет больше мудрости в Темане49:7 Теман – важный эдомитский город, получивший своё название от имени внука Эсова, родоначальника Эдома (см. Нач. 36:15). Здесь под именем Теман подразумевается вся страна Эдом.,

и нет рассудка у разумных,

что их мудрость оскудела?

8Повернитесь, бегите и скройтесь в глубоких пещерах,

жители Дедана49:8 Дедан – арабское племя, произошедшее от Иброхима и его второй жены Хеттуры (см. Нач. 25:1-3).,

так как Я наведу на Эсова49:8 Эсов – родоначальник эдомитян (см. Нач. 25:25, 30), представляющий здесь всю страну Эдом. бедствие,

когда придёт время его наказать.

9Если придут к тебе собиратели винограда,

разве не оставят они нескольких виноградин на лозе?

И если ночью явятся воры,

разве они не украдут лишь столько, сколько им нужно?

10А Я донага оберу Эсова,

открою его тайные места,

и он не сможет укрыться.

Его дети, сородичи и соседи погибнут,

и не станет его.

11Оставь своих сирот, Я защищу их;

твои вдовы могут надеяться на Меня.

12Так говорит Вечный:

– Если даже те, кто не заслужил пить из чаши, должны будут испить из неё, то уйдёшь ли ты безнаказанным? Не уйдёшь безнаказанным: непременно выпьешь до дна. 13Клянусь Самим Собой, – возвещает Вечный, – что ужасом, посмешищем, запустением и проклятием станет Боцра49:13 Боцра – важный эдомитский город, представляющий здесь всю страну Эдом., а все её города придут в вечное запустение.

14Я слышал весть от Вечного,

что посланник отправлен к народам сказать:

«Сходитесь, чтобы напасть на него!

Поднимайтесь на битву!»

15– Я сделаю тебя малым среди народов,

презренным среди людей.

16Страх, что ты внушаешь,

и гордость сердца твоего обманули тебя,

тебя, живущего среди расщелин скал,

владетеля вершин холмов.

Хоть ты и вьёшь себе гнездо высоко, как орёл,

но и оттуда Я низвергну тебя, –

возвещает Вечный. –

17Ужасом станет Эдом;

каждый, кто пройдёт мимо, ужаснётся

и поиздевается над всеми его ранами.

18Как были низвергнуты Содом и Гоморра

с окрестными городами49:18 См. Нач. 18:20–19:29., –

возвещает Вечный, –

так никто не будет жить и там,

ни один человек не поселится.

19Словно лев, который выходит из иорданской чащи

на роскошные пастбища,

Я в мгновение ока изгоню Эдом из его земель

и поставлю над ним того, кого изберу.

Кто подобен Мне? Кто спросит с Меня?

Какой правитель49:19 Букв.: «пастух»; также в 50:44. может противостоять Мне?

20Выслушайте же замысел Вечного об Эдоме

и Его намерения о жителях Темана:

молодняк отар будет угнан прочь,

и пастбища их Он погубит.

21От шума их падения вздрогнет земля;

их крик будет слышен у Тростникового моря49:21 Тростниковое море – буквальный перевод с языка оригинала. Среди современных специалистов существуют различные мнения, о каком водоёме здесь идёт речь. Тростниковым морем могли называть как цепи озёр, расположенных на Суэцком перешейке и, вероятно, соединявшихся тогда проливами с Красным морем, так и Суэцкий и Акабский заливы Красного моря (см. напр., 3 Цар. 9:26). В Инджиле эти же воды названы Красным морем..

22Он, как орёл, поднимется и налетит,

простирая свои крылья над Боцрой.

В тот день сердца воинов Эдома

затрепещут, словно сердце роженицы.

Пророчество о Дамаске

23О Дамаске.

– Пали духом Хамат и Арпад,

услышав плохие вести;

мечутся от страха, волнуются, словно море,

и покоя себе не находят.

24Дамаск обессилел,

повернулся, чтобы бежать,

охватил его страх;

пронзили его муки и боль,

боль, как у женщины в родах.

25Разве не брошен прославленный город,

город Моей радости?

26Итак, его юноши падут на улицах от меча;

все его воины умолкнут в тот день, –

возвещает Вечный, Повелитель Сил. –

27Я зажгу огонь на стенах Дамаска;

он пожрёт крепости Бен-Адада49:27 Бен-Адад – истории известны три сирийских царя, носивших это имя..

Пророчество о Кедаре и Хацоре

28О Кедаре и царствах Хацора49:28 Кедар и Хацор – районы, где жили арабские племена., куда вторгся Навуходоносор, царь Вавилона.

Так говорит Вечный:

– Вставайте, идите против Кедара!

Губите народ Востока!

29Их шатры и стада отберут у них;

их завесы, и всё добро,

и верблюды будут отняты.

Им будут кричать:

«Ужас со всех сторон!»

30Бегите скорее!

Селитесь в глубоких пещерах,

жители Хацора, –

возвещает Вечный. –

Царь Вавилона Навуходоносор принял о вас решение

и обдумал свой замысел о вас.

31Вставайте, идите против беспечного народа,

который живёт беззаботно, –

возвещает Вечный, –

у которого нет ни дверей, ни засовов,

против народа, который живёт отдельно.

32Их верблюды станут чужой добычей,

и множество их стад будет расхищено.

Я развею по всем ветрам тех, кто стрижёт волосы на висках49:32 См. сноску на 9:26.,

и со всех сторон пошлю на них гибель, –

возвещает Вечный. –

33Хацор превратится в логово шакалов,

запустеет навеки,

и никто не будет в нём жить,

ни один человек не поселится.

Пророчество о Еламе

34Слово Вечного, которое было к пророку Иеремии о Еламе49:34 Елам – царство, которое было расположено восточнее Вавилона, на территории современного Ирана. в начале правления иудейского царя Цедекии49:34 Цедекия правил Иудеей с 597 по 586 гг. до н. э..

35Так говорит Вечный, Повелитель Сил:

– Я сломаю лук Елама,

опору его могущества.

36Я пошлю на Елам четыре ветра

с четырёх краёв небес;

Я развею его по четырём ветрам,

и не будет такого народа,

к которому не пошли бы изгнанники-еламиты.

37Я разобью Елам перед его неприятелями,

перед теми, кто желает его смерти;

Я нашлю на него беду

и даже Мой пылающий гнев, –

возвещает Вечный. –

Я буду преследовать их мечом,

пока не истреблю их окончательно.

38Я поставлю в Еламе Свой престол

и погублю его царя и вельмож, –

возвещает Вечный. –

39Но в будущем Я верну Еламу благополучие, –

возвещает Вечный.