Yeremiya 48 – CCL & CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 48:1-47

Uthenga Wonena za Mowabu

1Ponena za Mowabu:

Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,

“Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa.

Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa;

linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.

2Palibenso amene akutamanda Mowabu;

ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa:

‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’

Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete;

ankhondo adzakupirikitsani.

3Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu.

Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’

4Mowabu wawonongeka;

ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.

5Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti,

akulira kwambiri pamene akupita.

Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka

pa njira yotsikira ku Horonaimu.

6Thawani! Dzipulumutseni;

khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.

7Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu,

nanunso mudzatengedwa ukapolo,

ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo,

pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.

8Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse,

ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke.

Chigwa chidzasanduka bwinja

ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa

monga Yehova wayankhulira.

9Mtsineni khutu Mowabu

chifukwa adzasakazika;

mizinda yake idzasanduka mabwinja,

wopanda munthu wokhalamo.

10“Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika!

Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!

11“Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake,

ngati vinyo wokhazikika pa masese ake,

osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina;

iye sanatengedwepo ukapolo.

Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja

ndipo fungo lake silinasinthe.

12Nʼchifukwa chake masiku akubwera,”

akutero Yehova,

“pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko

ndipo adzamukhutula;

adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake

pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.

13Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi,

monga momwe Aisraeli anachitira manyazi

ndi Beteli amene ankamukhutulira.

14“Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali.

Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’

15Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake;

anyamata ake okongola apita kukaphedwa,”

ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

16Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi;

masautso ake akubwera posachedwa.

17Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira,

inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake;

nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija,

taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”

18“Tsikani pa ulemerero wanu

ndipo khalani pansi powuma,

inu anthu okhala ku Diboni,

pakuti wowononga Mowabu

wabwera kudzamenyana nanu,

wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.

19Inu amene mumakhala ku Aroeri,

imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera.

Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka,

afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’ ”

20Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika.

Lirani mwachisoni ndipo fuwulani!

Lengezani ku mtsinje wa Arinoni

kuti Mowabu wawonongedwa.

21Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri,

ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,

22Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,

23Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,

24Keriyoti ndi Bozira

ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.

25Mphamvu za Mowabu zawonongeka;

mkono wake wathyoka,”

akutero Yehova.

26“Muledzeretseni Mowabu,

chifukwa anadzikuza powukira Yehova.

Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake;

mulekeni akhale chinthu chomachiseka.

27Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka?

Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba

kuti nthawi zonse poyankhula za iye,

iwe uzimupukusira mutu momunyoza?

28Inu amene mumakhala ku Mowabu,

siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe.

Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake

pa khomo la phanga.

29“Tamva za kunyada kwa Mowabu,

kunyada kwake nʼkwakukulu.

Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula.

Ali ndi mtima wodzikweza.

30Ine ndikuzidziwa ntchito zake,

akutero Yehova.

Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.

31Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu,

ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu,

ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.

32Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri.

Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa

imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja;

zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri.

Wowononga wasakaza

zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.

33Chimwemwe ndi chisangalalo zatha

ku minda ya zipatso ya ku Mowabu.

Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa;

palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa.

Ngakhale kufuwula kulipo,

koma sikufuwula kwa chimwemwe.

34“A ku Hesiboni ndi Eleali akulira

ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi,

kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya.

Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.

35Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu

kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera

ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,”

akutero Yehova.

36“Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro.

Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro

chifukwa chuma chimene anachipata chatha.

37Aliyense wameta mutu wake

ndi ndevu zake;

manja a munthu aliyense ndi ochekacheka,

ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.

38Pa madenga onse a ku Mowabu

ndiponso mʼmisewu yake

anthu akungolira,

pakuti ndaphwanya Mowabu

ngati mtsuko wopanda ntchito,”

akutero Yehova.

39“Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira!

Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi.

Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka,

chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”

40Yehova akuti,

“Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga

chimene chatambalitsa mapiko ake.

41Mizinda idzagwidwa

ndipo malinga adzalandidwa.

Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu

idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.

42Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu

chifukwa unadzikuza powukira Yehova.

43Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira

inu anthu a ku Mowabu,”

akutero Yehova.

44“Aliyense wothawa zoopsa

adzagwera mʼdzenje,

aliyense wotuluka mʼdzenje

adzakodwa mu msampha.

Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu

pa nthawi ya chilango chake,”

akutero Yehova.

45“Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni

chifukwa chotopa.

Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni,

malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni.

Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu,

dziko la anthu onyada.

46Tsoka kwa iwe Mowabu!

Anthu opembedza Kemosi awonongeka.

Ana ako aamuna ndi aakazi

atengedwa ukapolo.

47“Komabe masiku akutsogolo

ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,”

akutero Yehova.

Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 48:1-47

Uthenga Wonena za Mowabu

1Ponena za Mowabu:

Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,

“Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa.

Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa;

linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.

2Palibenso amene akutamanda Mowabu;

ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa:

‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’

Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete;

ankhondo adzakupirikitsani.

3Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu.

Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’

4Mowabu wawonongeka;

ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.

5Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti,

akulira kwambiri pamene akupita.

Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka

pa njira yotsikira ku Horonaimu.

6Thawani! Dzipulumutseni;

khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.

7Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu,

nanunso mudzatengedwa ukapolo,

ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo,

pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.

8Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse,

ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke.

Chigwa chidzasanduka bwinja

ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa

monga Yehova wayankhulira.

9Mtsineni khutu Mowabu

chifukwa adzasakazika;

mizinda yake idzasanduka mabwinja,

wopanda munthu wokhalamo.

10“Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika!

Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!

11“Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake,

ngati vinyo wokhazikika pa masese ake,

osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina;

iye sanatengedwepo ukapolo.

Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja

ndipo fungo lake silinasinthe.

12Nʼchifukwa chake masiku akubwera,”

akutero Yehova,

“pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko

ndipo adzamukhutula;

adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake

pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.

13Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi,

monga momwe Aisraeli anachitira manyazi

ndi Beteli amene ankamukhutulira.

14“Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali.

Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’

15Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake;

anyamata ake okongola apita kukaphedwa,”

ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

16Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi;

masautso ake akubwera posachedwa.

17Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira,

inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake;

nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija,

taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”

18“Tsikani pa ulemerero wanu

ndipo khalani pansi powuma,

inu anthu okhala ku Diboni,

pakuti wowononga Mowabu

wabwera kudzamenyana nanu,

wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.

19Inu amene mumakhala ku Aroeri,

imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera.

Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka,

afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’ ”

20Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika.

Lirani mwachisoni ndipo fuwulani!

Lengezani ku mtsinje wa Arinoni

kuti Mowabu wawonongedwa.

21Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri,

ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,

22Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,

23Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,

24Keriyoti ndi Bozira

ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.

25Mphamvu za Mowabu zawonongeka;

mkono wake wathyoka,”

akutero Yehova.

26“Muledzeretseni Mowabu,

chifukwa anadzikuza powukira Yehova.

Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake;

mulekeni akhale chinthu chomachiseka.

27Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka?

Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba

kuti nthawi zonse poyankhula za iye,

iwe uzimupukusira mutu momunyoza?

28Inu amene mumakhala ku Mowabu,

siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe.

Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake

pa khomo la phanga.

29“Tamva za kunyada kwa Mowabu,

kunyada kwake nʼkwakukulu.

Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula.

Ali ndi mtima wodzikweza.

30Ine ndikuzidziwa ntchito zake,

akutero Yehova.

Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.

31Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu,

ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu,

ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.

32Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri.

Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa

imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja;

zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri.

Wowononga wasakaza

zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.

33Chimwemwe ndi chisangalalo zatha

ku minda ya zipatso ya ku Mowabu.

Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa;

palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa.

Ngakhale kufuwula kulipo,

koma sikufuwula kwa chimwemwe.

34“A ku Hesiboni ndi Eleali akulira

ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi,

kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya.

Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.

35Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu

kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera

ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,”

akutero Yehova.

36“Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro.

Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro

chifukwa chuma chimene anachipata chatha.

37Aliyense wameta mutu wake

ndi ndevu zake;

manja a munthu aliyense ndi ochekacheka,

ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.

38Pa madenga onse a ku Mowabu

ndiponso mʼmisewu yake

anthu akungolira,

pakuti ndaphwanya Mowabu

ngati mtsuko wopanda ntchito,”

akutero Yehova.

39“Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira!

Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi.

Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka,

chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”

40Yehova akuti,

“Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga

chimene chatambalitsa mapiko ake.

41Mizinda idzagwidwa

ndipo malinga adzalandidwa.

Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu

idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.

42Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu

chifukwa unadzikuza powukira Yehova.

43Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira

inu anthu a ku Mowabu,”

akutero Yehova.

44“Aliyense wothawa zoopsa

adzagwera mʼdzenje,

aliyense wotuluka mʼdzenje

adzakodwa mu msampha.

Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu

pa nthawi ya chilango chake,”

akutero Yehova.

45“Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni

chifukwa chotopa.

Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni,

malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni.

Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu,

dziko la anthu onyada.

46Tsoka kwa iwe Mowabu!

Anthu opembedza Kemosi awonongeka.

Ana ako aamuna ndi aakazi

atengedwa ukapolo.

47“Komabe masiku akutsogolo

ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,”

akutero Yehova.

Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.