Yeremiya 47 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 47:1-7

Uthenga Wonena za Afilisti

1Uthenga umene Yehova anamupatsa mneneri Yeremiya wonena za Afilisti, Farao asanathire nkhondo Gaza ndi uwu:

2Yehova akuti,

“Taonani mmene madzi akubwerera kuchokera kumpoto;

adzasanduka mtsinje wosefukira ndi a mkokomo.

Adzasefukira mʼdziko monse ndi kumiza chilichonse mʼmenemo,

mizinda ndi onse okhala mʼmenemo.

Anthu adzafuwula;

anthu onse okhala mʼdzikomo adzalira

3akadzamva mgugu wa ngʼombe zazimuna zothamanga,

phokoso la magaleta ake

ndi kulira kwa mikombero yake.

Makolo sadzatembenuka kuti athandize ana awo;

manja awo adzangoti khoba.

4Pakuti tsiku lafika

lowononga Afilisti onse

ndi kupha onse otsala,

onse amene akanatha kuthandiza Turo ndi Sidoni.

Yehova ali pafupi kuwononga Afilisti,

otsala ochokera ku zilumba za ku Kafitori.

5Anthu a ku Gaza ameta mipala;

anthu a ku Asikeloni akhala chete.

Inu otsala a ku chigwa,

mudzakhala mukudzichekacheka mpaka liti?

6“Mukulira kuti, ‘Aa, lupanga la Yehova,

kodi udzapumula liti?

Bwerera mʼmalo ako;

ukhale momwemo ndipo ukhale chete.’

7Koma lupangalo lidzapumula bwanji

pamene Yehova walilamulira

kuti lithire nkhondo

Asikeloni ndi anthu a mʼmbali mwa nyanja?”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米书 47:1-7

关于非利士的预言

1在法老攻打迦萨之前,耶和华告诉了耶利米先知有关非利士人的事。

2耶和华说:

“看啊,大水将从北方涨溢,

形成一道洪流,

淹没大地和地上的一切,

吞噬城邑和其中的居民。

人们必呼喊,

地上的居民必哀哭。

3一听见马蹄嗒嗒、

战车隆隆、车轮滚滚的声音,

做父亲的就吓得手脚发软,

无力照顾儿女。

4因为毁灭所有非利士人的日子到了,

铲除泰尔西顿剩余帮手的日子到了。

耶和华要灭绝迦斐托岛剩余的非利士人。

5迦萨一片荒凉,

亚实基伦沦为废墟。

谷中的余民啊!

你们要割伤身体到何时呢?

6你们大喊,‘耶和华的刀啊,

你何时才停下来呢?

求你入鞘吧!停下来吧!’

7但耶和华已命令它攻击亚实基伦和沿海一带,

它怎能停下来呢?”