Yeremiya 46 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 46:1-28

1Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.

Uthenga Wonena za Igupto

2Kunena za Igupto:

Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,

3anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo,

ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!

4Mangani akavalo,

ndipo kwerani inu okwerapo!

Khalani pa mzere

mutavala zipewa!

Nolani mikondo yanu,

valani malaya anu ankhondo!

5Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani?

Achita mantha

akubwerera,

ankhondo awo agonjetsedwa.

Akuthawa mofulumirapo

osayangʼananso mʼmbuyo,

ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,”

akutero Yehova.

6Waliwiro sangathe kuthawa

ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka.

Akunka napunthwa ndi kugwa

kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.

7“Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo,

ngati mtsinje wa madzi amkokomo?

8Igupto akusefukira ngati Nailo,

ngati mitsinje ya madzi amkokomo.

Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi;

ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’

9Tiyeni, inu akavalo!

Thamangani inu magaleta!

Tulukani, inu ankhondo,

ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango,

ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.

10Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse;

tsiku lolipsira, lolipsira adani ake.

Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi,

lidzaledzera ndi magazi.

Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe

mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.

11“Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala

iwe namwali Igupto.

Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira;

palibe mankhwala okuchiritsa.

12Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako;

kulira kwako kwadzaza dziko lapansi.

Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana,

onse awiri agwa pansi limodzi.”

13Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:

14“Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli.

Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi.

Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza,

chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’

15Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa?

Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.

16Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa.

Aliyense akuwuza mnzake kuti,

‘Tiyeni tibwerere kwathu,

ku dziko kumene tinabadwira,

tithawe lupanga la adani athu.’

17Kumeneku iwo adzafuwula kuti,

‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti,

Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’

18“Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu,

imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse,

“wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena,

ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.

19Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo

inu anthu a ku Igupto,

pakuti Mefisi adzasanduka chipululu

ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.

20“Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola,

koma chimphanga chikubwera

kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.

21Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye

ali ngati ana angʼombe onenepa.

Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi.

Palibe amene wachirimika.

Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira;

ndiyo nthawi yowalanga.

22Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa

pamene adani abwera ndi zida zawo,

abwera ndi nkhwangwa

ngati anthu odula mitengo.

23Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,”

akutero Yehova,

“ngakhale kuti ndi yowirira.

Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe,

moti sangatheke kuwerengeka.

24Anthu a ku Igupto achita manyazi

atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”

25Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira. 26Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.

27“Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha;

usataye mtima, iwe Israeli.

Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali,

ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo.

Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere,

ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.

28Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha,

pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova.

“Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu

a ku mayiko kumene ndakupirikitsira,

Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu.

Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera;

sindidzakulekerera osakulanga.”

New International Version

Jeremiah 46:1-28

A Message About Egypt

1This is the word of the Lord that came to Jeremiah the prophet concerning the nations:

2Concerning Egypt:

This is the message against the army of Pharaoh Necho king of Egypt, which was defeated at Carchemish on the Euphrates River by Nebuchadnezzar king of Babylon in the fourth year of Jehoiakim son of Josiah king of Judah:

3“Prepare your shields, both large and small,

and march out for battle!

4Harness the horses,

mount the steeds!

Take your positions

with helmets on!

Polish your spears,

put on your armor!

5What do I see?

They are terrified,

they are retreating,

their warriors are defeated.

They flee in haste

without looking back,

and there is terror on every side,”

declares the Lord.

6“The swift cannot flee

nor the strong escape.

In the north by the River Euphrates

they stumble and fall.

7“Who is this that rises like the Nile,

like rivers of surging waters?

8Egypt rises like the Nile,

like rivers of surging waters.

She says, ‘I will rise and cover the earth;

I will destroy cities and their people.’

9Charge, you horses!

Drive furiously, you charioteers!

March on, you warriors—men of Cush46:9 That is, the upper Nile region and Put who carry shields,

men of Lydia who draw the bow.

10But that day belongs to the Lord, the Lord Almighty—

a day of vengeance, for vengeance on his foes.

The sword will devour till it is satisfied,

till it has quenched its thirst with blood.

For the Lord, the Lord Almighty, will offer sacrifice

in the land of the north by the River Euphrates.

11“Go up to Gilead and get balm,

Virgin Daughter Egypt.

But you try many medicines in vain;

there is no healing for you.

12The nations will hear of your shame;

your cries will fill the earth.

One warrior will stumble over another;

both will fall down together.”

13This is the message the Lord spoke to Jeremiah the prophet about the coming of Nebuchadnezzar king of Babylon to attack Egypt:

14“Announce this in Egypt, and proclaim it in Migdol;

proclaim it also in Memphis and Tahpanhes:

‘Take your positions and get ready,

for the sword devours those around you.’

15Why will your warriors be laid low?

They cannot stand, for the Lord will push them down.

16They will stumble repeatedly;

they will fall over each other.

They will say, ‘Get up, let us go back

to our own people and our native lands,

away from the sword of the oppressor.’

17There they will exclaim,

‘Pharaoh king of Egypt is only a loud noise;

he has missed his opportunity.’

18“As surely as I live,” declares the King,

whose name is the Lord Almighty,

“one will come who is like Tabor among the mountains,

like Carmel by the sea.

19Pack your belongings for exile,

you who live in Egypt,

for Memphis will be laid waste

and lie in ruins without inhabitant.

20“Egypt is a beautiful heifer,

but a gadfly is coming

against her from the north.

21The mercenaries in her ranks

are like fattened calves.

They too will turn and flee together,

they will not stand their ground,

for the day of disaster is coming upon them,

the time for them to be punished.

22Egypt will hiss like a fleeing serpent

as the enemy advances in force;

they will come against her with axes,

like men who cut down trees.

23They will chop down her forest,”

declares the Lord,

“dense though it be.

They are more numerous than locusts,

they cannot be counted.

24Daughter Egypt will be put to shame,

given into the hands of the people of the north.”

25The Lord Almighty, the God of Israel, says: “I am about to bring punishment on Amon god of Thebes, on Pharaoh, on Egypt and her gods and her kings, and on those who rely on Pharaoh. 26I will give them into the hands of those who want to kill them—Nebuchadnezzar king of Babylon and his officers. Later, however, Egypt will be inhabited as in times past,” declares the Lord.

27“Do not be afraid, Jacob my servant;

do not be dismayed, Israel.

I will surely save you out of a distant place,

your descendants from the land of their exile.

Jacob will again have peace and security,

and no one will make him afraid.

28Do not be afraid, Jacob my servant,

for I am with you,” declares the Lord.

“Though I completely destroy all the nations

among which I scatter you,

I will not completely destroy you.

I will discipline you but only in due measure;

I will not let you go entirely unpunished.”