Yeremiya 43 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 43:1-13

1Yeremiya atatsiriza kuwawuza anthuwo mawu onse a Yehova Mulungu wawo, amene Yehova anamutuma kuti akawawuze, 2Azariya mwana wa Hosayia ndi Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi anthu onse odzikuza anawuza Yeremiya kuti, “Ukunama iwe! Yehova Mulungu wathu sanakutume kuti unene kuti, ‘Musapite ku Igupto kukakhala kumeneko.’ 3Koma ndi Baruki mwana wa Neriya amene akukulimbikitsa kuti utiletse zopita ku Igupto ndi kuti mʼmalo mwake tidzipereke mʼmanja mwa Ababuloni, kuti iwo atiphe kapena kutitenga ukapolo ku Babuloni.”

4Motero Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi anthu onse sanamvere lamulo la Yehova loti akhale mʼdziko la Yuda. 5Mʼmalo mwake, Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo anatenga anthu onse otsala a ku Yuda amene anabwera kudzakhala mʼdziko la Yuda kuchokera ku mayiko onse kumene anabalakirako. 6Mʼgulu la anthu otengedwalo munali amuna onse, akazi ndi ana, ana aakazi a mfumu, ndiponso anthu amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anawasiya kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani pamodzinso ndi mneneri Yeremiya ndi Baruki mwana wa Neriya. 7Kotero anthuwo analowa mʼdziko la Igupto chifukwa anakana kumvera Yehova, nakafika ku Tapanesi.

8Ndipo Yehova anayankhula ndi Yeremiya ku Tapanesi kuti, 9“Tenga miyala inayi yayikulu ndipo uyikwirire mʼdothi pa chiwundo cha polowera ku nyumba yaufumu ya Farao ku Tapanesi. Uchite zimenezi Ayuda onse akuona. 10Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayitana mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzakhazika mpando wake waufumu pa miyala imene ndayikwirira apayi. Iye adzafunyulula tenti yake yaufumu pa miyala imeneyi. 11Iye adzabwera kudzathira nkhondo Igupto. Iwo oyenera kufa ndi mliri adzafa ndi mliri, iwo oyenera kutengedwa ukapolo adzatengedwa ukapolo, ndipo iwo oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga. 12Adzayatsa moto mʼnyumba zopembedzera milungu ya Igupto. Adzayeretsa dziko la Igupto monga momwe mʼbusa amayeretsera chovala chake pochotsamo nsabwe. Pambuyo pake adzachoka mʼdziko la Igupto mwa mtendere. 13Ku Iguptoko adzagwetsa zipilala zachipembedzo za ku nyumba yopembedzera mulungu wa dzuwa. Adzatentha ndi moto nyumba za milungu ya ku Igupto.’ ”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 43:1-13

耶利米被帶到埃及

1耶利米向眾人宣告了他們的上帝耶和華的話,就是他們的上帝耶和華派他去說的一切話。 2何沙雅的兒子亞撒利雅加利亞的兒子約哈難和一些狂妄之徒對耶利米說:「你在撒謊!我們的上帝耶和華並沒有派你來告訴我們不可去埃及住。 3尼利亞的兒子巴錄慫恿你反對我們,好叫我們落在迦勒底人手中,任由他們宰殺或擄到巴比倫。」 4於是,加利亞的兒子約哈難和眾將領及民眾都不聽從耶和華讓他們留在猶大的命令。 5-7加利亞的兒子約哈難和眾將領率領民眾下到埃及答比匿。民眾中有流亡到各國又返回猶大的餘民和護衛長尼布撒拉旦留給沙番的孫子、亞希甘的兒子基大利管理的男女婦孺、公主以及耶利米先知和尼利亞的兒子巴錄。他們沒有聽從耶和華的命令。

8耶和華在答比匿耶利米說: 9「你當著猶大人的面搬幾塊大石頭,埋在答比匿的法老宮門前的磚路下面, 10然後告訴他們以色列的上帝——萬軍之耶和華說,『看啊,我必召來我的僕人巴比倫尼布甲尼撒,把他的寶座安置在我讓你埋的石頭上面,他要在上面搭起他的帳篷。 11他要前來攻打埃及,叫那些該死的死、該被擄的被擄、該被殺的被殺。 12他要焚燒埃及的神廟,擄走神像;他要像牧人披上外衣一樣輕而易舉地征服埃及,然後安然離去。 13他要摧毀埃及太陽神廟的神柱,燒毀埃及的神廟。』」