Yeremiya 42 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 42:1-22

1Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita 2kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala. 3Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”

4Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”

5Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze. 6Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”

7Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya. 8Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe. 9Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti, 10“Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu. 11Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake. 12Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.

13“Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno, 14ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’ 15Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko, 16ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko. 17Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’ 18Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’

19“Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani 20kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’ 21Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni. 22Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 42:1-22

耶利米警告猶大人勿去埃及

1加利亞的兒子約哈難何沙雅的兒子耶撒尼亞和其他將領及各階層的民眾前來, 2耶利米先知說:「求你答應我們的懇求,為我們這些餘民向我們的上帝耶和華祈求。你也看見了,我們本來人數眾多,現在卻寥寥無幾。 3願你的上帝耶和華指示我們該去哪裡,該做什麼。」 4耶利米先知說:「好。我必照你們說的向你們的上帝耶和華祈求,並把祂的話毫不隱瞞地告訴你們。」 5他們說:「倘若我們不照你的上帝耶和華說的去做,願誠實可靠的耶和華作證指控我們! 6不論我們的上帝耶和華說什麼,我們都願意聽從。我們若聽祂的話,就必亨通。」

7十天之後,耶和華的話傳給了耶利米8耶利米便召集加利亞的兒子約哈難和眾將領及各階層的民眾, 9對他們說:「你們讓我向以色列的上帝耶和華祈求,耶和華這樣說, 10『如果你們留在這地方,我必扶持你們,決不毀滅你們;我必栽培你們,決不剷除你們。因為我為降在你們身上的災禍而難過。 11不要懼怕巴比倫王,不要怕他,因為我必與你們同在,拯救你們脫離他的權勢。這是耶和華說的。 12我必憐憫你們,也要讓他憐憫你們,使你們重歸故土。』 13然而,如果你們不聽你們的上帝耶和華的話,不留在這地方, 14非要去埃及住,以為那裡沒有戰爭,聽不見號角聲,也不會忍饑挨餓, 15那麼,你們這些猶大的餘民就要聽聽耶和華的話。以色列的上帝——萬軍之耶和華說,『如果你們決意去埃及住, 16你們所害怕的戰爭和饑荒必緊緊地跟著你們。你們必死在埃及17凡決意去埃及住的人必要死於戰爭、饑荒和瘟疫,無人能逃脫我降的災禍。』

18以色列的上帝——萬軍之耶和華說,『我曾把烈怒傾倒在耶路撒冷人身上,如果你們去埃及,我也要把我的怒氣傾倒在你們身上。你們的下場將很可怕,被人責罵、咒詛和羞辱,再也見不到故土。』 19猶大的餘民啊,耶和華已告訴你們不要去埃及。別忘了我今日給你們的警告, 20你們是在自欺,因為原是你們請我去向我們的上帝耶和華祈求,讓我毫不隱瞞地把祂的話告訴你們,你們也答應遵行。 21今日,我把你們上帝耶和華的話告訴了你們,你們卻不聽從。 22因此,你們要清楚知道,你們如果決意去埃及住,必死於戰爭、饑荒和瘟疫。」