Yeremiya 42 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 42:1-22

1Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita 2kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala. 3Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”

4Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”

5Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze. 6Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”

7Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya. 8Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe. 9Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti, 10“Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu. 11Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake. 12Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.

13“Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno, 14ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’ 15Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko, 16ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko. 17Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’ 18Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’

19“Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani 20kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’ 21Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni. 22Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米书 42:1-22

耶利米警告犹大人勿去埃及

1加利亚的儿子约哈难何沙雅的儿子耶撒尼亚和其他将领及各阶层的民众前来, 2耶利米先知说:“求你答应我们的恳求,为我们这些余民向我们的上帝耶和华祈求。你也看见了,我们本来人数众多,现在却寥寥无几。 3愿你的上帝耶和华指示我们该去哪里,该做什么。” 4耶利米先知说:“好。我必照你们说的向你们的上帝耶和华祈求,并把祂的话毫不隐瞒地告诉你们。” 5他们说:“倘若我们不照你的上帝耶和华说的去做,愿诚实可靠的耶和华作证指控我们! 6不论我们的上帝耶和华说什么,我们都愿意听从。我们若听祂的话,就必亨通。”

7十天之后,耶和华的话传给了耶利米8耶利米便召集加利亚的儿子约哈难和众将领及各阶层的民众, 9对他们说:“你们让我向以色列的上帝耶和华祈求,耶和华这样说, 10‘如果你们留在这地方,我必扶持你们,决不毁灭你们;我必栽培你们,决不铲除你们。因为我为降在你们身上的灾祸而难过。 11不要惧怕巴比伦王,不要怕他,因为我必与你们同在,拯救你们脱离他的权势。这是耶和华说的。 12我必怜悯你们,也要让他怜悯你们,使你们重归故土。’ 13然而,如果你们不听你们的上帝耶和华的话,不留在这地方, 14非要去埃及住,以为那里没有战争,听不见号角声,也不会忍饥挨饿, 15那么,你们这些犹大的余民就要听听耶和华的话。以色列的上帝——万军之耶和华说,‘如果你们决意去埃及住, 16你们所害怕的战争和饥荒必紧紧地跟着你们。你们必死在埃及17凡决意去埃及住的人必要死于战争、饥荒和瘟疫,无人能逃脱我降的灾祸。’

18以色列的上帝——万军之耶和华说,‘我曾把烈怒倾倒在耶路撒冷人身上,如果你们去埃及,我也要把我的怒气倾倒在你们身上。你们的下场将很可怕,被人责骂、咒诅和羞辱,再也见不到故土。’ 19犹大的余民啊,耶和华已告诉你们不要去埃及。别忘了我今日给你们的警告, 20你们是在自欺,因为原是你们请我去向我们的上帝耶和华祈求,让我毫不隐瞒地把祂的话告诉你们,你们也答应遵行。 21今日,我把你们上帝耶和华的话告诉了你们,你们却不听从。 22因此,你们要清楚知道,你们如果决意去埃及住,必死于战争、饥荒和瘟疫。”