Yeremiya 40 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 40:1-16

Amasula Yeremiya

1Yehova anayankhula ndi Yeremiya pamene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anamasula Yeremiyayo ku Rama. Anamupeza Yeremiya ali womangidwa ndi unyolo pamodzi ndi amʼndende ena onse a ku Yerusalemu ndi a ku Yuda amene ankapita nawo ku ukapolo ku Babuloni. 2Mtsogoleriyu anamupeza Yeremiya, anamuwuza kuti, “Yehova Mulungu wako analengeza kale zakuti malo ano adzawonongedwa. 3Ndipo tsopano Yehova wachitadi zimenezi monga mmene ananenera. Izi zonse zachitika chifukwa anthu inu munachimwira Yehova ndipo simunamumvere. 4Koma tsopano taona, lero ndikukumasula unyolo umene unali mʼmanja mwako. Ngati ukufuna kupita nane ku Babuloni, tiye ndipo adzakusamala bwino. Koma ngati sukufuna kupita, ndiye usapite. Dziko ndi limeneli monga ukulioneramo. Uli ndi ufulu kupita kulikonse kumene ukufuna.” 5Yeremiya asanayankhe, Nebuzaradani anamuwuzanso kuti, “Ngati supita ndiye pita, ubwerere kwa Gedaliya, mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, amene mfumu ya ku Babuloni inamusankha kuti akhale bwanamkubwa wa Yuda. Ukakhale naye pakati pa anthu, kapena upite kulikonse ukufuna.”

Ndipo mtsogoleri uja anamupatsa Yeremiya chakudya ndi mphatso zina ndi kumulola kuti apite. 6Motero Yeremiya anapita kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu ku Mizipa ndipo anakakhala naye kumeneko pakati pa anthu amene anatsala mʼdzikomo.

Kuphedwa kwa Gedaliya

7Panali atsogoleri ena a nkhondo ndi anthu awo amene sanadzipereke nawo. Iwowa anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu kukhala bwanamkubwa wa dzikolo ndipo kuti yamuyika kukhala wolamulira amuna, akazi ndi ana amene anali osauka kwambiri mʼdzikomo, amene sanawagwire ukapolo kupita nawo ku Babuloni. 8Iwowa anapita ku Mizipa kwa Gedaliya. Amene anapitawo ndi awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani ndi Yonatani ana a Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti, ana a Efai a ku Netofa, ndi Yezaniya mwana wa Maaka, iwowo pamodzi ndi anthu awo. 9Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, anawalonjeza iwo pamodzi ndi anthuwo mwalumbiro. Ndipo anati, “Musaope kuwatumikira Ababuloni. Khalani mʼdziko muno, tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino. 10Ine ndidzakhala ku Mizipa kuti ndizikuyimirirani kwa Ababuloni amene azidzabwera kwa ife, koma inu muzikolola vinyo wanu, zipatso zanu, mafuta anu ndi kuzisunga mʼmitsuko yanu, nʼkumakhala mʼmizinda imene mwalandayo.”

11Nawonso Ayuda onse a ku Mowabu, ku Amoni, ku Edomu ndi a ku mayiko ena onse anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasiyako anthu ena ku Yuda ndipo kuti inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala bwanamkubwa wawo. 12Tsono Ayuda onsewo anabwerera ku Yuda, ku Mizipa kwa Gedaliya, kuchokera ku mayiko onse kumene anabalalikira. Ndipo anakolola zipatso zochuluka ndi vinyo wambiri.

13Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri a ankhondo onse amene sanadzipereke aja anabwera ku Mizipa kwa Gedaliya 14ndipo anamufunsa kuti, “Kodi sukudziwa kuti Baalisi mfumu ya Aamoni watuma Ismaeli mwana wa Netaniya kuti akuphe?” Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu sanawankhulupirire.

15Tsono Yohanani mwana wa Kareya, mwamseri anawuza Gedaliya ku Mizipa kuti, “Loleni ndipite ndikaphe Ismaeli mwana wa Netaniya, ndipo palibe amene ati adziwe. Akuphereninji ndi kuchititsa Ayuda onse, amene akuzungulirani kuti abalalike ndi kuti otsala a ku Yuda awonongeke?”

16Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu anawuza Yohanani mwana wa Kareya kuti, “Usachite zimenezo! Zimene ukunena za Ismaeli ndi zabodza.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иеремия 40:1-16

Иеремия освобождён

1Слово Вечного, которое было к Иеремии после того, как Невузарадан, начальник царской охраны, освободил его в Раме. Тот нашёл Иеремию, закованного в цепи, среди всех пленников из Иерусалима и Иудеи, которых угоняли в плен в Вавилон. 2Разыскав Иеремию, начальник охраны сказал ему:

– Вечный, твой Бог, сулил такую беду этой стране. 3А ныне она разразилась: как Вечный говорил, так Он и сделал. Это случилось потому, что вы грешили против Вечного и не слушались Его. 4Но сегодня я освобождаю тебя от цепей, что на твоих руках. Если хочешь, пойдём со мной в Вавилон, и я позабочусь о тебе, а не хочешь, так и не ходи. Смотри, вся земля перед тобой: ступай, куда хочешь.

5Не успел Иеремия отойти, как Невузарадан добавил:

– Возвращайся к Гедалии, сыну Ахикама, внуку Шафана, которого царь Вавилона назначил начальником над городами Иудеи, и живи у него среди народа. Или ступай, куда хочешь.

Затем начальник охраны дал ему припасов в дорогу и подарок и отпустил его. 6И Иеремия пошёл к Гедалии, сыну Ахикама, в Мицпу, и поселился там у него среди народа, который был оставлен в стране.

Убийство Гедалии

(4 Цар. 25:22-26)

7Когда все военачальники и их люди, оставшиеся в этой стране, услышали, что царь Вавилона назначил Гедалию, сына Ахикама, наместником над страной, и что ему поручили заботы о мужчинах, женщинах и детях, которые были самыми бедными в стране и не были угнаны в плен в Вавилон, 8они пришли к Гедалии в Мицпу. Это были Исмоил, сын Нетании, Иоханан и Ионафан, сыновья Кареаха, Серая, сын Танхумета, сыновья Ефая из Нетофы, Иазания, сын маахитянина, со своими людьми. 9Гедалия, сын Ахикама, внук Шафана, поклялся им, чтобы успокоить их и их людей:

– Не бойтесь служить вавилонянам, – сказал он. – Селитесь в земле, служите царю Вавилона, и вам будет хорошо. 10Сам я буду жить в Мицпе, чтобы представлять вас перед вавилонянами, которые будут приходить к нам, а вы собирайте и запасайте вино, летние плоды и оливковое масло в кувшины и живите себе в городах, которые заняли.

11Когда все иудеи в Моаве, Аммоне, Эдоме и во всех других странах услышали, что вавилонский царь оставил в Иудее часть народа и назначил Гедалию, сына Ахикама, внука Шафана, их наместником, 12все они вернулись в землю Иудеи к Гедалии, в Мицпу, из всех стран, куда были изгнаны. Они собрали в изобилии вина и летних плодов.

13Иоханан, сын Кареаха, и все военачальники, всё ещё пребывавшие в поле, явились к Гедалии в Мицпу 14и сказали ему:

– Неужели ты не знаешь, что Баалис, царь аммонитян, подослал Исмоила, сына Нетании, чтобы убить тебя?

Но Гедалия, сын Ахикама, не поверил им. 15Тогда Иоханан, сын Кареаха, тайно сказал Гедалии в Мицпе:

– Давай я пойду и убью Исмоила, сына Нетании, так, что никто об этом не узнает. Зачем позволять ему лишать тебя жизни, чтобы все иудеи, которые собрались вокруг тебя, были рассеяны, чтобы оставшиеся в Иудее погибли?!

16Но Гедалия, сын Ахикама, сказал Иоханану, сыну Кареаха:

– Не делай этого! То, что ты говоришь об Исмоиле, – неправда.