Yeremiya 4 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 4:1-31

1“Ngati mukufuna kubwerera, inu Aisraeli,

bwererani kwa Ine,”

akutero Yehova.

“Chotsani mafano anu onyansa pamaso panga

ndipo musasocherenso.

2Muzilumbira mokhulupirika ndiponso mwa chilungamo

kuti, ‘Pali Yehova wamoyo.’

Mukatero anthu a mitundu ina yonse adzandipempha kuti ndiwadalitse

ndipo adzanditamanda.”

3Zimene Yehova akunena kwa anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu ndi izi:

“Limani masala anu

musadzale pakati pa minga.

4Dziperekeni nokha kwa Ine

kuti munditumikire ndi mtima wanu wonse,

inu anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu.

Muzichita zimenezi kuopa kuti mkwiyo wanga ungabuke ngati moto ndi kukutenthani,

chifukwa cha ntchito zanu zoyipazo

popanda wina wowuzimitsa.

Adani Ochokera Kumpoto kwa Yuda

5“Lengeza ku Yuda ndi kulalikira mu Yerusalemu kuti,

‘Lizani lipenga mʼdziko lonse!’

Ndipo fuwulani kuti,

‘Sonkhanani!

Tiyeni tithawire ku mizinda yotetezedwa!’

6Kwezani mbendera kuyangʼana ku Ziyoni!

Musachedwe, thawani kuti mupulumuke!

Pakuti Ine ndikubweretsa chilango kuchokera kumpoto,

kudzakhala chiwonongeko choopsa.”

7Monga mkango umatulukira mʼngaka yake

momwemonso wowononga mayiko

wanyamuka ndi kutuluka ku mbuto yake.

Watero kuti awononge dziko lanu.

Mizinda yanu idzakhala mabwinja

popanda wokhalamo.

8Choncho valani ziguduli,

lirani ndi kubuwula,

pakuti mkwiyo waukulu wa Yehova

sunatichokere.

9“Pa tsiku limenelo, mfumu ndi nduna zake adzataya mtima,

ansembe adzachita mantha kwambiri,

ndipo aneneri adzathedwa nzeru,”

akutero Yehova.

10Ndipo ine ndinati, “Haa, Ambuye Yehova, ndithu munawanyenga anthu awa pamodzi ndi Yerusalemu pamene munanena kuti, ‘Mudzakhala pa mtendere,’ chonsecho lupanga lili pakhosi pathu.”

11Nthawi imeneyo anthu awa ndi Yerusalemu adzawawuza kuti, “Mphepo yotentha yochokera ku magomo a mʼchipululu ikuwomba pa anthu anga, osati mphepo yopeta kapena yoyeretsa; 12koma mphepo yamphamvu kwambiri yochokera kwa Ine. Tsono ndi Ineyo amene ndikuwaweruza.”

13Taonani, adani akubwera ngati mitambo,

magaleta awo akubwera ngati kamvuluvulu,

akavalo awo ndi aliwiro kupambana chiwombankhanga.

Tsoka ilo! Tawonongeka!

14Iwe Yerusalemu, tsuka mtima wako kuchotsa zoyipa kuti upulumuke.

Kodi maganizo ako oyipawo udzakhala nawo mpaka liti?

15Pakuti amithenga akulalika mawu mʼdziko la Dani;

akulengeza za masautso kuchokera ku mapiri a Efereimu.

16Iwo akuti, “Fotokozani zimenezi kwa anthu a mitundu ina,

lengezani zimenezi mu Yerusalemu kuti,

‘Ankhondo akubwera kuchokera ku dziko lakutali,

akufuwula ndi kudzazinga mizinda ya Yuda.

17Azinga Yerusalemu ngati anthu olondera munda,

chifukwa Yerusalemu wandiwukira,’ ”

akutero Yehova.

18“Makhalidwe anu ndi zochita zanu

zakubweretserani zimenezi.

Chimenechi ndiye chilango chanu.

Nʼchowawa kwambiri!

Nʼcholasa mpaka mu mtima!”

19Mayo, mayo,

ndikumva kupweteka!

Aa, mtima wanga ukupweteka,

ukugunda kuti thi, thi, thi.

Sindingathe kukhala chete.

Pakuti ndamva kulira kwa lipenga;

ndamva mfuwu wankhondo.

20Tsoka limatsata tsoka linzake;

dziko lonse lasanduka bwinja.

Mwadzidzidzi matenti athu awonongedwa,

mwa kanthawi kochepa nsalu zake zotchinga zagwetsedwa.

21Kodi ndikhale ndikuona mbendera ya nkhondo,

ndi kumva kulira kwa lipenga mpaka liti?

22Yehova akuti, “Anthu anga ndi zitsiru;

iwo sandidziwa.

Iwo ndi ana opanda nzeru;

samvetsa chilichonse.

Ali ndi luso lochita zoyipa,

koma sadziwa kuchita zabwino.”

23Ndinayangʼana dziko lapansi,

ndipo linali lopanda anthu ndi lopanda kanthu;

ndinayangʼana thambo,

koma linalibe kuwala kulikonse.

24Ndinayangʼana mapiri,

ndipo ankagwedezeka;

magomo onse ankangosunthira uku ndi uku.

25Ndinayangʼana, ndipo sindinaone anthu;

mbalame iliyonse ya mlengalenga inali itathawa.

26Ndinayangʼana, dziko lachonde linali litasanduka chipululu;

mizinda yake yonse inali itasanduka bwinja

pamaso pa Yehova, chifukwa cha mkwiyo wake.

27Yehova akuti,

“Dziko lonse lidzasanduka chipululu

komabe sindidzaliwononga kotheratu.

28Chifukwa chake dziko lapansi lidzalira

ndipo thambo lidzachita mdima,

pakuti ndayankhula ndipo sindidzafewa mtima,

ndatsimikiza ndipo sindidzabwerera mʼmbuyo.”

29Pakumva phokoso la okwera pa akavalo ndi la anthu oponya mivi,

anthu a mʼmizinda adzathawa.

Ena adzabisala ku nkhalango;

ena adzakwera mʼmatanthwe

mizinda yonse nʼkuyisiya;

popanda munthu wokhalamo.

30Iwe Yerusalemu, ndiwe bwinja!

Ukutanthauza chiyani kuvala zovala zofiira

ndi kuvalanso zokometsera zagolide?

Ngakhale udzikonze maso ako powapaka zokometsera,

ukungodzivuta chabe.

Zibwenzi zako zikukunyoza;

zikufuna kuchotsa moyo wako.

31Ndikumva kulira ngati kwa mayi pa nthawi yake yobereka,

kubuwula ngati kwa mayi amene akubereka mwana wake woyamba.

Kuliraku ndi kwa anthu a mu Ziyoni, wefuwefu.

Atambalitsa manja awo nʼkumati,

“Kalanga ife! Tikukomoka.

Moyo wathu waperekedwa kwa anthu otipha.”

Hoffnung für Alle

Jeremia 4:1-31

Fangt ganz neu an!

1Der Herr lässt dir verkünden: »Kehr um, Israel, komm zurück zu mir! Wirf deine abscheulichen Götzen weg und wende dich nicht länger von mir ab. 2Wenn du bei meinem Namen schwörst, sei aufrichtig, ehrlich und halte dich daran. Dann werden auch die anderen Völker einander in meinem Namen Segen wünschen und sich glücklich schätzen, mich zu kennen.

3Ich, der Herr, sage zu den Bewohnern von Juda und Jerusalem: Fangt ganz neu an wie ein Bauer, der ein brachliegendes Feld zum ersten Mal wieder bestellt! Streut eure Saat auf fruchtbaren Boden und nicht unter die Dornen! 4Ändert euch von Grund auf und wendet euch von ganzem Herzen mir zu!4,4 Wörtlich: Beschneidet euch für den Herrn und entfernt die Vorhaut von eurem Herzen! Wenn ihr nicht von euren falschen Wegen umkehrt, entbrennt mein Zorn wie ein Feuer, das niemand löschen kann.«

Unheil aus dem Norden

5»Schlagt Alarm in Juda und in Jerusalem! Blast das Signalhorn überall im Land! Ruft, so laut ihr könnt: ›Sammelt euch und flieht in die befestigten Städte!‹ 6Stellt Wegweiser nach Zion auf! Lauft und bleibt nicht stehen! Denn aus dem Norden bringe ich, der Herr, schreckliches Unheil und Zerstörung über das Land.

7Ein Löwe kommt aus seinem Versteck und geht auf Raubzug: Ganze Völker will er verschlingen. Ja, er verlässt sein Versteck, um euer Land zu verwüsten! Zerstört und entvölkert wird er eure Städte zurücklassen.

8Zieht Trauergewänder an, weint und klagt: ›Immer noch lastet der glühende Zorn des Herrn auf uns!‹

9Wenn das geschieht, werden der König und die führenden Männer allen Mut verlieren, die Priester werden entsetzt sein und die Propheten starr vor Schreck. Darauf gebe ich, der Herr, mein Wort!«

10»Ach, Herr, mein Gott«, rief ich, »du hast dieses Volk und die Einwohner von Jerusalem schlimm getäuscht! Frieden hast du ihnen versprochen, und nun sitzt ihnen das Messer an der Kehle!« 11Der Herr erwiderte: »Wenn es so weit ist, wird man den Einwohnern von Jerusalem und dem ganzen Volk zurufen: ›Ein Glutwind kommt von den kahlen Höhen in der Wüste!‹ Er wird meinem Volk direkt ins Gesicht blasen. Es ist kein Wind, mit dem man Spreu und Weizen voneinander trennen kann, 12dazu ist er zu stark. Er kommt auf meinen Befehl. Jetzt werde ich persönlich mein Urteil über euch sprechen!

13Ihr schreit: ›Seht! Der Feind rückt heran wie eine Gewitterfront! Seine Streitwagen brausen daher wie ein Wirbelsturm, seine Pferde sind schneller als Adler! Wir sind dem Untergang geweiht, wir sind verloren!‹

14Jerusalem, reinige dein Herz von aller Bosheit, damit du gerettet wirst! Wie lange noch willst du Unheil ausbrüten?

15Boten kommen aus der Stadt Dan und vom Bergland Ephraim. Sie bringen eine Schreckensnachricht: 16›Meldet Jerusalem und den umliegenden Völkern: Aus einem fernen Land rückt ein Heer zur Eroberung heran!‹ Vor den Städten Judas werden sie das Kriegsgeschrei anstimmen, 17sich aufstellen und sie umringen wie Wächter, die ein Feld bewachen; denn dieses Volk hat sich gegen mich, den Herrn, aufgelehnt. 18Das alles habt ihr euch selbst zu verdanken, eure eigenen Taten und Irrwege haben es euch eingebracht. Nun bekommt ihr den Lohn für eure Bosheit und müsst spüren, wie bitter und schmerzlich es ist, mich zu verlassen!«

Jeremia leidet mit seinem Volk

19Was sind das für Qualen! Ich winde mich vor Schmerzen, und das Herz klopft mir bis zum Hals. Ich kann nicht schweigen, denn ich höre das Signalhorn und das Kriegsgeschrei! 20Man meldet eine Niederlage nach der anderen, das ganze Land ist schon verwüstet! Ganz plötzlich wurden unsere Zelte zerstört und ihre Decken zerfetzt. 21Wie lange muss ich die Feldzeichen der Feinde noch sehen und ihre Signalhörner hören?

22Der Herr spricht: »Mein Volk ist töricht und verbohrt, sie wollen mich nicht kennen. Sie sind wie unverständige und dumme Kinder. Böses zu tun, damit kennen sie sich aus, aber wie man Gutes tut, das wissen sie nicht!«

23Ich sah die Erde an – sie war leer und ohne Leben. Ich blickte zum Himmel empor – dort schien kein Licht. 24Ich schaute zu den Bergen hinüber – sie bebten, und alle Hügel schwankten. 25Im ganzen Land sah ich keine Menschen mehr, selbst die Vögel waren fortgeflogen. 26Die einst fruchtbaren Felder waren eine trostlose Wüste, und die Städte lagen in Trümmern. Das hat der Herr getan in seinem glühenden Zorn. 27Er sprach: »Ich will dieses Land verwüsten – doch nicht ganz und gar! 28Die Erde trauert, und der Himmel verfinstert sich. Denn ich, der Herr, habe den Befehl dazu gegeben und bereue es nicht. Mein Entschluss steht fest.

29Die Reiter und Bogenschützen stürmen mit lautem Geschrei heran, die Einwohner der Städte fliehen in die dichten Wälder und verstecken sich in Höhlen. Alle Städte sind verlassen und unbewohnt.

30Aber du, Jerusalem, was machst du da? Deine Eroberer stehen schon vor der Tür, und du ziehst dein leuchtend rotes Festkleid an, hängst dir goldenen Schmuck um den Hals und schminkst deine Augen? Umsonst machst du dich schön! Deine Liebhaber haben dich satt, jetzt trachten sie dir nach dem Leben.« 31Da, ein Schrei wie von einer Frau, die zum ersten Mal in den Wehen liegt! Es ist die Stadt Zion. Sie ringt nach Luft, streckt Hilfe suchend ihre Hände aus und ruft: »Ich bin verloren! Sie bringen mich um!«