Yeremiya 4 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 4:1-31

1“Ngati mukufuna kubwerera, inu Aisraeli,

bwererani kwa Ine,”

akutero Yehova.

“Chotsani mafano anu onyansa pamaso panga

ndipo musasocherenso.

2Muzilumbira mokhulupirika ndiponso mwa chilungamo

kuti, ‘Pali Yehova wamoyo.’

Mukatero anthu a mitundu ina yonse adzandipempha kuti ndiwadalitse

ndipo adzanditamanda.”

3Zimene Yehova akunena kwa anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu ndi izi:

“Limani masala anu

musadzale pakati pa minga.

4Dziperekeni nokha kwa Ine

kuti munditumikire ndi mtima wanu wonse,

inu anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu.

Muzichita zimenezi kuopa kuti mkwiyo wanga ungabuke ngati moto ndi kukutenthani,

chifukwa cha ntchito zanu zoyipazo

popanda wina wowuzimitsa.

Adani Ochokera Kumpoto kwa Yuda

5“Lengeza ku Yuda ndi kulalikira mu Yerusalemu kuti,

‘Lizani lipenga mʼdziko lonse!’

Ndipo fuwulani kuti,

‘Sonkhanani!

Tiyeni tithawire ku mizinda yotetezedwa!’

6Kwezani mbendera kuyangʼana ku Ziyoni!

Musachedwe, thawani kuti mupulumuke!

Pakuti Ine ndikubweretsa chilango kuchokera kumpoto,

kudzakhala chiwonongeko choopsa.”

7Monga mkango umatulukira mʼngaka yake

momwemonso wowononga mayiko

wanyamuka ndi kutuluka ku mbuto yake.

Watero kuti awononge dziko lanu.

Mizinda yanu idzakhala mabwinja

popanda wokhalamo.

8Choncho valani ziguduli,

lirani ndi kubuwula,

pakuti mkwiyo waukulu wa Yehova

sunatichokere.

9“Pa tsiku limenelo, mfumu ndi nduna zake adzataya mtima,

ansembe adzachita mantha kwambiri,

ndipo aneneri adzathedwa nzeru,”

akutero Yehova.

10Ndipo ine ndinati, “Haa, Ambuye Yehova, ndithu munawanyenga anthu awa pamodzi ndi Yerusalemu pamene munanena kuti, ‘Mudzakhala pa mtendere,’ chonsecho lupanga lili pakhosi pathu.”

11Nthawi imeneyo anthu awa ndi Yerusalemu adzawawuza kuti, “Mphepo yotentha yochokera ku magomo a mʼchipululu ikuwomba pa anthu anga, osati mphepo yopeta kapena yoyeretsa; 12koma mphepo yamphamvu kwambiri yochokera kwa Ine. Tsono ndi Ineyo amene ndikuwaweruza.”

13Taonani, adani akubwera ngati mitambo,

magaleta awo akubwera ngati kamvuluvulu,

akavalo awo ndi aliwiro kupambana chiwombankhanga.

Tsoka ilo! Tawonongeka!

14Iwe Yerusalemu, tsuka mtima wako kuchotsa zoyipa kuti upulumuke.

Kodi maganizo ako oyipawo udzakhala nawo mpaka liti?

15Pakuti amithenga akulalika mawu mʼdziko la Dani;

akulengeza za masautso kuchokera ku mapiri a Efereimu.

16Iwo akuti, “Fotokozani zimenezi kwa anthu a mitundu ina,

lengezani zimenezi mu Yerusalemu kuti,

‘Ankhondo akubwera kuchokera ku dziko lakutali,

akufuwula ndi kudzazinga mizinda ya Yuda.

17Azinga Yerusalemu ngati anthu olondera munda,

chifukwa Yerusalemu wandiwukira,’ ”

akutero Yehova.

18“Makhalidwe anu ndi zochita zanu

zakubweretserani zimenezi.

Chimenechi ndiye chilango chanu.

Nʼchowawa kwambiri!

Nʼcholasa mpaka mu mtima!”

19Mayo, mayo,

ndikumva kupweteka!

Aa, mtima wanga ukupweteka,

ukugunda kuti thi, thi, thi.

Sindingathe kukhala chete.

Pakuti ndamva kulira kwa lipenga;

ndamva mfuwu wankhondo.

20Tsoka limatsata tsoka linzake;

dziko lonse lasanduka bwinja.

Mwadzidzidzi matenti athu awonongedwa,

mwa kanthawi kochepa nsalu zake zotchinga zagwetsedwa.

21Kodi ndikhale ndikuona mbendera ya nkhondo,

ndi kumva kulira kwa lipenga mpaka liti?

22Yehova akuti, “Anthu anga ndi zitsiru;

iwo sandidziwa.

Iwo ndi ana opanda nzeru;

samvetsa chilichonse.

Ali ndi luso lochita zoyipa,

koma sadziwa kuchita zabwino.”

23Ndinayangʼana dziko lapansi,

ndipo linali lopanda anthu ndi lopanda kanthu;

ndinayangʼana thambo,

koma linalibe kuwala kulikonse.

24Ndinayangʼana mapiri,

ndipo ankagwedezeka;

magomo onse ankangosunthira uku ndi uku.

25Ndinayangʼana, ndipo sindinaone anthu;

mbalame iliyonse ya mlengalenga inali itathawa.

26Ndinayangʼana, dziko lachonde linali litasanduka chipululu;

mizinda yake yonse inali itasanduka bwinja

pamaso pa Yehova, chifukwa cha mkwiyo wake.

27Yehova akuti,

“Dziko lonse lidzasanduka chipululu

komabe sindidzaliwononga kotheratu.

28Chifukwa chake dziko lapansi lidzalira

ndipo thambo lidzachita mdima,

pakuti ndayankhula ndipo sindidzafewa mtima,

ndatsimikiza ndipo sindidzabwerera mʼmbuyo.”

29Pakumva phokoso la okwera pa akavalo ndi la anthu oponya mivi,

anthu a mʼmizinda adzathawa.

Ena adzabisala ku nkhalango;

ena adzakwera mʼmatanthwe

mizinda yonse nʼkuyisiya;

popanda munthu wokhalamo.

30Iwe Yerusalemu, ndiwe bwinja!

Ukutanthauza chiyani kuvala zovala zofiira

ndi kuvalanso zokometsera zagolide?

Ngakhale udzikonze maso ako powapaka zokometsera,

ukungodzivuta chabe.

Zibwenzi zako zikukunyoza;

zikufuna kuchotsa moyo wako.

31Ndikumva kulira ngati kwa mayi pa nthawi yake yobereka,

kubuwula ngati kwa mayi amene akubereka mwana wake woyamba.

Kuliraku ndi kwa anthu a mu Ziyoni, wefuwefu.

Atambalitsa manja awo nʼkumati,

“Kalanga ife! Tikukomoka.

Moyo wathu waperekedwa kwa anthu otipha.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 4:1-31

1耶和華說:「以色列啊,

如果你回轉歸向我,

回轉歸向我,

從我眼前除掉可憎的神像,

不再離開我;

2如果你本著誠實、正直、公義,

憑永活的耶和華起誓,

你必成為萬國的祝福,

得到他們的尊敬4·2 你必成為萬國的祝福,得到他們的尊敬」或譯「萬國必得到耶和華的祝福,並以祂為榮」。。」

3耶和華對猶大人和耶路撒冷人說:

「要開墾你們的荒地,

不要在荊棘中撒種。

4你們要自行割禮,

除掉心中的污垢,歸向耶和華。

不然,我必因你們的惡行而發烈怒,如火燃燒,

無人能夠撲滅。

5「你們要在猶大耶路撒冷宣告,

『要在全國吹起號角』,高聲呼喊,

『要集合起來,

我們要逃進堅城。』

6你們要向錫安舉起旗幟,

趕快逃亡,不要遲延,

因為我要從北方降下災禍,

大肆毀滅。」

7毀滅列國者已發起攻擊,

如獅子衝出巢穴,

要使你們的土地荒涼,

城邑淪為廢墟,無人居住。

8為此,你們要腰束麻布,

嚎啕大哭,

因為耶和華向我們發的烈怒還沒有止息。

9耶和華說:「到那天,君王和官長必喪膽,祭司和先知必驚駭。」 10我說:「唉!主耶和華啊,你完全欺騙了這群百姓和耶路撒冷人,因為你說,『你們會安享太平。』其實劍鋒已指著他們的咽喉了。」

11那時,耶和華必對這群百姓和耶路撒冷人說:「一陣熱風從荒野光禿的山頭吹向我的子民,不是為揚場、吹淨糠秕。 12那是我發出的一陣強風。現在我要宣告我對他們的審判。」

13看啊,仇敵必如雲湧來,

他的戰車快如旋風,

他的戰馬比飛鷹還快。

我們有禍了!

我們滅亡了!

14耶路撒冷啊,

要洗去你內心的邪惡,

這樣你才能得救。

你心懷惡念要到何時呢?

15傳來消息,

以法蓮山區報出惡訊。

16耶和華說:「你們去通知列國,

耶路撒冷宣告,

『圍攻的人從遠方來,

猶大的城邑高聲喊殺,

17像看守田園一樣包圍耶路撒冷

因為耶路撒冷背叛了我。』

這是耶和華說的。

18你的所作所為給你招致這災禍,

是你自食惡果,你會痛徹心肺!」

19我的心啊,我的心啊!

我傷心欲絕,煩躁不安。

我無法保持緘默,

因為我聽見了號角聲和呐喊聲。

20惡訊頻傳,山河破碎,

我的帳篷忽然倒塌,

幔子頃刻破裂。

21我還要看這旌旗、

聽這號聲到何時呢?

22耶和華說:「我的子民愚頑,

不認識我,

是蒙昧無知的兒女,

只知行惡,不知行善。」

23我俯瞰大地,

一片空虛混沌;

我仰望天空,毫無亮光。

24我眺望群山,大山在顫抖,

小山在搖晃。

25我四下觀看,只見杳無人煙,

飛鳥絕跡。

26我四下觀看,只見良田變荒野,

城邑都在耶和華的烈怒下淪為廢墟。

27耶和華說:「遍地將要荒涼,

然而不會被我徹底毀滅。

28因此,地要悲哀,

天要昏暗,

因為我言出必行,

決不反悔。」

29各城的人聽到騎兵和弓箭手的呐喊,

都紛紛逃命。

有的跑入叢林,有的爬進岩洞。

各城荒棄,無人居住。

30你這荒涼的城啊!

你在做什麽?

縱然你穿上紅袍,

戴上金飾,

描眉畫眼,

又有什麼用呢?

你的情人藐視你,

要殺害你。

31我聽見好像婦人分娩時的喊叫聲,

好像婦人生頭胎時的痛苦呻吟。

那是錫安4·31 」希伯來文是「女子」,可能是對錫安的暱稱,下同6·223的喊叫聲,

她在喘息,伸出雙手說:

「噢!我有禍了,

我要死在殺戮者手上了。」