Yeremiya 36 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 36:1-32

Yehoyakimu Atentha Buku la Yeremiya

1Chaka chachinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti, 2“Tenga buku ndipo ulembemo mawu onse amene ndayankhula nawe otsutsa Israeli, Yuda ndi mitundu yonse ya anthu, kuyambira nthawi imene ndinayamba kuyankhula nawe pa nthawi ya ulamuliro wa Yosiya mpaka lero lino. 3Mwina mwake anthu a ku Yuda adzamva za zoopsa zonse zimene ndakonza kuti ndiwachitire, ndipo munthu aliyense adzatembenuka ndi kusiya ntchito zake zoyipa. Motero ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndi machimo awo.”

4Tsono Yeremiya anayitana Baruki mwana wa Neriya. Baruki analemba mʼbuku mawu onse amene Yeremiya ankamuwuza, mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya. 5Kenaka Yeremiya anawuza Baruki kuti, “Ine andiletsa kupita ku Nyumba ya Mulungu. 6Tsono iwe upite ku Nyumba ya Yehova pa tsiku losala kudya ndipo ukawerenge mawu a Yehova ochokera mʼbukumu amene ndinakulembetsa anthu onse akumva. Ukawawerengere anthu onse a ku Yuda amene amabwera ku Nyumba ya Mulungu kuchokera ku mizinda yawo. 7Mwina mwake adzapempha kwa Yehova ndipo aliyense adzatembenuka ndi kusiya makhalidwe ake oyipa pakuti mkwiyo ndi ukali wa Yehova pa anthu awa ndi woopsa kwambiri.”

8Baruki mwana wa Neriya anachita zonse zimene mneneri Yeremiya anamuwuza kuti achite. Mʼnyumba ya Yehova, iye anawerenga mawu a Yehova ochokera mʼbukulo. 9Pa mwezi wachisanu ndi chinayi wa chaka chachisanu cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, anthu onse a mu Yerusalemu ndi onse amene anabwera kumeneko kuchokera ku mizinda ya Yuda, anapangana za kusala kudya kuti apepese Yehova. 10Atayima pa chipinda cha Gemariya mwana wa mlembi Safani, chimene chinali mʼbwalo lapamwamba, pafupi ndi Chipata Chatsopano cholowera ku Nyumba ya Yehova, Baruki anawerenga mawu onse a Yeremiya amene anali mʼbuku muja kwa anthu onse amene anali ku Nyumba ya Yehova.

11Mikaya mwana wa Gemariya, mwana wa Safani, atamva mawu onse a Yehova ochokera mʼbukumo, 12anapita ku nyumba ya mfumu nakalowa ku chipinda cha mlembi. Akuluakulu, mlembi Elisama, Delaya mwana wa Semaya, Elinatani mwana wa Akibori, Gemariya mwana wa Safani, Zedekiya mwana wa Hananiya pamodzi ndi akuluakulu ena onse, anali atasonkhana kumeneko. 13Tsono Mikaya anawafotokozera mawu onse amene anamva pamene Baruki ankawerenga buku lija anthu onse akumva. 14Pambuyo pake akuluakulu onsewo anatuma Yehudi mwana wa Netaniya, mwana wa Selemiya, mwana wa Kusi, kwa Baruki kukamuwuza kuti, “Bwera ndi buku limene unawerenga kwa anthu.” Ndipo Baruki mwana wa Neriya anapita nalo bukulo kwa anthuwo. 15Iwo anati, “Khala pansi, ndipo tiwerengere bukuli.”

Ndipo Baruki anawawerengera. 16Atamva mawu onsewo, anayangʼanana mwa mantha ndipo anamuwuza Baruki kuti, “Ndithudi tikafotokozera mfumu mawu onsewa.” 17Tsono anamufunsa Baruki kuti, “Tatiwuze, unalemba bwanji mawu onsewa? Kodi ndi Yeremiya anakulembetsa zimenezi?”

18Baruki anayankha kuti, “Inde, ndi Yeremiya amene anandiwuza mawu onsewa, ndipo ine ndinawalemba ndi utoto mʼbukumu.”

19Kenaka akuluakuluwo anamuwuza Baruki kuti, “Iweyo ndi Yeremiya, pitani mukabisale. Munthu aliyense asadziwe kumene muli.”

20Atayika bukulo mʼchipinda cha mlembi Elisama, analowa mʼbwalo, napita kwa mfumu ndi kukayifotokozera zonse. 21Itamva zimenezi mfumu inatuma Yehudi kuti akatenge bukulo, ndipo Yehudi anakalitenga ku chipinda cha mlembi Elisama ndipo anawerengera mfumu pamodzi ndi akuluakulu ake amene anali naye. 22Unali mwezi wachisanu ndi chinayi ndipo mfumu inali mʼnyumba ya pa nyengo yozizira, ikuwotha moto umene anasonkha. 23Yehudi ankati akawerenga masamba atatu kapena anayi a bukulo, mfumu inkawangʼamba ndi mpeni ndi kuwaponya pa moto ndipo anapitiriza kuchita zimenezi mpaka buku lonse linapsa. 24Mfumu pamodzi ndi omutumikira ake onse amene anamva mawu onsewa sanachite mantha kapena kungʼamba zovala zawo. 25Ngakhale kuti Elinatani, Delaya, ndi Gemariya anapempha mfumu kuti isatenthe bukulo, mfumuyo sinawamvere. 26Mʼmalo mwake, mfumu inalamula Yerahimeeli mwana wake, Seraya mwana wa Azirieli ndi Selemiya mwana wa Abideeli kuti agwire mlembi Baruki ndi mneneri Yeremiya. Koma pamenepo nʼkuti Yehova atawabisa.

27Mfumu itatentha buku limene linali ndi mawu amene Yeremiya anamulembetsa Baruki, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti, 28“Tenganso buku lina ndipo ulembe mawu onse amene anali mʼbuku loyamba lija, limene Yehoyakimu analitentha. 29Ndiponso akamuwuze Yehoyakimu mfumu ya Yuda kuti, ‘Yehova akuti: Iwe unatentha buku lija ndipo unati: Nʼchifukwa chiyani unalemba kuti mfumu ya ku Babuloni idzabwera ndithu kudzawononga dziko lino ndi kupha anthu pamodzi ndi nyama zomwe?’ 30Nʼchifukwa chake kunena za Yehoyakimu mfumu ya Yuda Yehova akuti sipadzaoneka munthu wina wolowa mʼmalo mwake pa mpando wa Davide. Akadzafa mtembo wake udzaponyedwa kunja ndipo udzakhala pa dzuwa masana, ndi pachisanu chowundana usiku. 31Ndidzamulanga pamodzi ndi ana ake ndiponso omutumikira ake chifukwa cha zoyipa zawo; ndidzagwetsa pa iwo ndi pa onse amene akukhala mu Yerusalemu ndiponso pa anthu a ku Yuda masautso onse amene ndinawanena, chifukwa sanamvere.”

32Choncho Yeremiya anatenga buku lina napatsa mlembi Baruki mwana wa Neriya, ndipo Yeremiya anamulembetsa mawu onse amene anali mʼbuku limene Yehoyakimu mfumu ya Yuda anatentha. Ndipo anawonjezerapo mawu ambiri monga omwewo.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иеремия 36:1-32

Иоаким сжигает свиток Иеремии

1В четвёртом году правления иудейского царя Иоакима, сына Иосии (в 605 г. до н. э.), Вечный сказал Иеремии:

2– Возьми свиток и запиши в него все слова, которые Я говорил тебе об Исроиле, Иудее и всех народах с того времени, как Я начал говорить с тобой в дни правления Иосии вплоть до этого дня. 3Может быть, когда народ Иудеи услышит о всех невзгодах, которые Я задумал наслать на них, каждый из них оставит свой злой путь; тогда Я прощу им их вину и грех.

4Иеремия призвал Баруха, сына Нерии, и под диктовку Иеремии Барух записал в свиток все слова, которые Вечный говорил Иеремии.

5Затем Иеремия сказал Баруху:

– Мне запрещено входить в храм Вечного. 6Поэтому ты пойди в дом Вечного в день поста и прочитай народу из свитка слова Вечного, которые ты записал с моих слов. Прочитай их всему народу Иудеи, который соберётся со всех городов. 7Может быть, они вознесут к Вечному свою молитву и отвратится каждый со своего злого пути – ведь страшны гнев и ярость Вечного, которые грозят этому народу.

8Барух, сын Нерии, сделал всё, что велел ему пророк Иеремия, – он прочитал слова Вечного из свитка в храме Вечного. 9В девятом месяце пятого года правления иудейского царя Иоакима, сына Иосии (поздней осенью 604 г. до н. э.), для всех жителей Иерусалима и для тех, кто пришёл в Иерусалим из городов Иудеи, был объявлен пост перед Вечным. 10В комнате писаря Гемарии, сына Шафана, которая находилась в верхнем дворе у входа в Новые ворота храма, Барух прочёл всему народу, пришедшему в храм Вечного, слова Иеремии из свитка.

11Когда Михей, сын Гемарии, внук Шафана, услышал все слова Вечного из свитка, 12он пошёл в комнаты писарей в царском дворце, где сидели все придворные сановники: писарь Элишама, Делая, сын Шемаи, Элнафан, сын Ахбора, Гемария, сын Шафана, Цедекия, сын Ханании, и все остальные придворные. 13Когда Михей рассказал им всё, что он услышал, всё, что читал Барух народу из свитка, 14все вельможи отправили Иегуди, сына Нетании, внука Шелемии, правнука Куши, сказать Баруху: «Принеси свиток, который ты читал народу, и сам приходи». И Барух, сын Нерии, пришёл к ним со свитком в руках.

15Они сказали ему:

– Садись, просим тебя прочитать и нам.

Барух прочитал им. 16Услышав все эти слова, они в страхе переглянулись и сказали Баруху:

– Мы непременно должны доложить об этом царю.

17Потом они спросили Баруха:

– Просим тебя, расскажи нам, как ты написал всё это? Со слов Иеремии?

18– Да, – ответил Барух, – он говорил мне все эти слова, а я записывал чернилами в свиток.

19Тогда вельможи сказали Баруху:

– Ты и Иеремия идите и спрячьтесь, и пусть никто не знает, где вы.

20Оставив свиток в комнате писаря Элишамы, они пошли в царский двор и доложили обо всём царю. 21Царь послал Иегуди взять свиток. Иегуди принёс его из комнаты писаря Элишамы и стал читать его царю и всем вельможам, которые стояли возле него. 22Был девятый месяц (конец осени), и царь сидел в зимней комнате перед жаровней, в которой горел огонь. 23Когда Иегуди прочитывал три или четыре столбца свитка, царь отрезал их писарским ножом и бросал в жаровню. Он делал так до тех пор, пока в огне не сгорел весь свиток. 24Царь и все его слуги, слышавшие все эти слова, не ужаснулись и не разорвали в знак покаяния на себе одежду. 25Элнафан, Делая и Гемария упрашивали царя не сжигать свиток, но он не послушал их. 26Вместо этого царь приказал Иерахмеилу, члену царской семьи, Серае, сыну Азриила, и Шелемии, сыну Авдеила, взять под стражу писаря Баруха и пророка Иеремию. Но Вечный укрыл их.

27После того как царь сжёг свиток со словами, которые Барух записал со слов Иеремии, Вечный сказал Иеремии:

28– Возьми другой свиток и запиши в него все слова, какие были в первом свитке, который сжёг Иоаким, царь Иудеи. 29А Иоакиму, царю Иудеи, скажи: Так говорит Вечный: «Ты сжёг этот свиток и сказал: „Зачем ты написал, что царь Вавилона непременно явится и погубит эту землю, поразив на ней и людей, и зверей?“» 30Поэтому так говорит Вечный об Иоакиме, царе Иудеи: «Не будет у него потомка, который воцарился бы на престоле Довуда; а его мёртвое тело бросят незахороненным на дневной зной и ночной холод. 31Я накажу его, его детей и его слуг за их беззакония; Я нашлю на них, и на жителей Иерусалима, и на народ Иудеи все невзгоды, которыми Я им грозил, потому что они не слушали Меня».

32Тогда Иеремия взял другой свиток, отдал его писарю Баруху, сыну Нерии, и под диктовку Иеремии Барух записал в него все слова того свитка, который был сожжён царём Иудеи Иоакимом. И к словам сожжённого свитка было прибавлено много похожих слов.