Yeremiya 35 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 35:1-19

Arekabu

1Yehova anayankhula ndi Yeremiya nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, kuti: 2“Pita ku banja la Arekabu ndipo ukawayitane kuti abwere mʼchipinda chimodzi cha Nyumba ya Yehova ndipo akafika uwapatse vinyo kuti amwe.”

3Choncho ndinakatenga Yaazaniya (mwana wa Yeremiya winanso amene anali mwana wa Habaziniya), abale ake, ana ake onse aamuna ndi banja lonse la Arekabu. 4Ndinabwera nawo ku Nyumba ya Yehova, ku chipinda cha ophunzira a mneneri Hanani mwana wa Igidaliya, munthu wa Mulungu. Chipinda chimenechi chinali pafupi ndi chipinda cha akuluakulu, chimene chinali pamwamba pa chipinda cha Maaseya mwana wa Salumu, mlonda wa pa khomo. 5Kenaka ndinayika mabotolo odzaza ndi vinyo ndi zikho zake pamaso pa Arekabu ndipo ndinawawuza kuti, “Imwani vinyoyu.”

6Koma iwo anayankha kuti, “Ife sitimwa vinyo, chifukwa kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula kuti, ‘Inuyo ngakhale zidzukulu zanu, musadzamwe vinyo mpaka kalekale. 7Musadzamange nyumba kapena kufesa mbewu, kapena kulima minda ya mpesa; musadzakhale ndi zinthu zimenezi. Mʼmalo mwake muzidzakhale mʼmatenti. Mukadzatero mudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukukhalamo.’ 8Ife takhala tikumvera zonse zimene kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula. Ife ngakhale akazi athu kapena ana athu aamuna ndi aakazi sitinamwepo vinyo 9kapena kumanga nyumba kuti tizikhalamo kapenanso kukhala ndi minda ya mpesa, minda ina iliyonse kapena mbewu. 10Koma takhala mʼmatenti ndipo tamvera kwathunthu chilichonse chimene kholo lathu Yehonadabu anatilamula. 11Koma pamene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anathira nkhondo dziko lino, ife tinati, ‘Tiyeni tichoke, tipite ku Yerusalemu kuti tithawe magulu ankhondo a Akasidi ndi Aaramu.’ Kotero ife takhala tikukhala mu Yerusalemu.”

12Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya kuti, 13“Iyeyu, Yehova Mulungu wa Israeli anawuza Yeremiya kuti: Pita ukawawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Kodi simungatengeko phunziro ndi kumvera mawu anga?’ akutero Yehova. 14‘Yehonadabu mwana wa Rekabu analamula ana ake kuti asamwe vinyo ndipo lamulo limeneli alisunga. Mpaka lero lino iwo samwa vinyo, chifukwa akumvera lamulo la kholo lawo. Koma Ine ndakhala ndikuyankhula nanu kawirikawiri kukuchenjezani, koma inu simunandimvere Ine. 15Kawirikawiri ndakhala ndikutumiza atumiki anga, aneneri, kwa inu. Iwo akhala akukuwuzani kuti, ‘Aliyense wa inu asiye ntchito zake zoyipa ndi kukonza makhalidwe ake; musatsatire milungu ina ndi kumayitumikira. Pamenepo mudzakhala mʼdziko limene ndinakupatsani ndi makolo anu.’ Komabe inu simunasamale zimenezi kapena kundimvera Ine. 16Zidzukulu za Yehonadabu mwana wa Rekabu zakhala zikumvera lamulo limene kholo lawo anazilamula, koma inuyo simunandimvere Ine.

17“Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndidzagwetsera pa Yuda ndi pa onse okhala mu Yerusalemu masautso onse amene ndinakonza chifukwa sanandimvere. Ndinawayitana koma iwo sanayankhe.’ ”

18Yeremiya anawuza banja la Arekabu mawu onse a Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, kuti, “Munamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu ndipo mwatsatira malangizo ake onse ndi kuchita chilichonse chimene anakulamulani.” 19Tsono Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Yehonadabu mwana wa Rekabu sadzasowa munthu wonditumikira Ine nthawi zonse.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 35:1-19

順服的利甲族和悖逆的猶大人

1猶大約西亞的兒子約雅敬執政期間,耶和華對耶利米說: 2「你去利甲族那裡,邀請他們到耶和華殿的一間廂房,給他們酒喝。」 3於是,我將哈巴洗尼雅的孫子、雅利米雅的兒子雅撒尼亞,以及雅撒尼亞的弟兄和兒子等利甲全族的人, 4領到耶和華的殿,進入上帝的僕人伊基大利之子哈難眾兒子的房間。這房間靠近官長的房間,在殿門守衛沙龍的兒子瑪西雅的房間上面。 5我把盛滿酒的杯和壺擺在利甲全族面前,請他們喝酒。 6他們卻說:「我們不喝酒,因為我們的祖先利甲的兒子約拿達曾吩咐我們和我們的子孫永遠不可喝酒、 7蓋房、撒種、栽植葡萄或擁有葡萄園,一輩子都要住帳篷,以便在異鄉長久居住。 8我們遵守他的一切吩咐,我們和我們的妻子兒女從不喝酒, 9不蓋房,也沒有葡萄園、田地和種子。 10我們住帳篷,遵守我們祖先約拿達的一切吩咐。 11但當巴比倫尼布甲尼撒進攻這裡的時候,我們決定來耶路撒冷躲避迦勒底亞蘭的軍隊。因此,我們現在住在耶路撒冷。」

12耶和華對耶利米說: 13「這是以色列的上帝——萬軍之耶和華的話,你去把我的話告訴猶大人和耶路撒冷的居民,『耶和華說,你們要聽從我的教導。 14利甲的兒子約拿達吩咐他的子孫不可喝酒,他們直到現在都不喝酒。但我屢次告誡你們,你們卻不聽我的話。 15我再三差遣我的僕人——眾先知勸你們改邪歸正,不要追隨、祭拜別的神明,以便你們可以在我賜給你們和你們祖先的土地上安居樂業,你們卻充耳不聞,毫不理會。 16利甲的兒子約拿達的子孫尚且聽從他們祖先的吩咐,你們卻不聽從我的話。 17因此,以色列的上帝——萬軍之耶和華說,我要給猶大耶路撒冷的居民降下我說過的災禍。因為我對他們說話,他們不聽;我呼喚他們,他們不理會。』」

18然後,耶利米利甲族人說:「以色列的上帝——萬軍之耶和華說,『你們聽從祖先利甲的兒子約拿達的吩咐,遵守他的一切命令, 19因此,利甲的兒子約拿達的子孫必永遠事奉我。這是以色列的上帝——萬軍之耶和華說的。』」