Yeremiya 3 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 3:1-25

1“Ngati munthu asudzula mkazi wake

ndipo mkaziyo nʼkuchoka nakakwatiwa ndi mwamuna wina,

kodi mwamuna woyambayo angathe kumutenganso mkaziyo?

Kodi atatero sindiye kuti dzikolo layipitsidwa kwambiri?

Koma iwe Israeli wachita zadama ndi zibwenzi zambiri.

Komabe bwerera kwa ine,”

akutero Yehova.

2“Tayangʼana ku zitunda zowuma.

Kodi aliponso malo ena amene iwe sunachitepo zadama?

Iwe unkakhala mʼmbali mwa njira kumadikira zibwenzi zako,

ngati Mluya wobisalira anthu mʼchipululu.

Inu mwayipitsa dziko ndi zadama zanu

ndi ntchito zanu zoyipa.

3Nʼchifukwa chake Yehova wayimitsa mvula,

ndipo mvula ya nthawi ya masika sinagwe.

Komabe uli ndi maonekedwe a mkazi wachiwerewere;

ndipo sukuchita manyazi ndi pangʼono pomwe.

4Kodi iwe siposachedwa pomwepa pamene wanena

kuti, ‘Abambo anga, Inu bwenzi langa la unyamata wanga,

5kodi mudzandikwiyira nthawi zonse?

Kodi ukali wanu udzakhalabe mpaka muyaya?’

Umu ndimo mmene umayankhulira,

koma umapitirizabe kuchita zoyipa monga momwe umathera.”

Kusakhulupirika kwa Israeli

6Pa nthawi ya Mfumu Yosiya Yehova anandiwuza kuti, “Kodi waona zomwe Israeli wosakhulupirika uja wachita? Anakwera pa phiri lililonse lalitali ndi kupita pa tsinde pa mtengo uliwonse wogudira kukapembedza. Choncho anachita za chiwerewere kumeneko. 7Ndinaganiza kuti atachita zonsezi, adzabwerera kwa Ine, koma sanabwerere, ndipo mlongo wake wosakhulupirika uja, Yuda, anaziona zimenezi. 8Anaona kuti ndinasudzula Israeli wosakhulupirikayo ndi kumupirikitsa chifukwa cha zigololo zake. Komabe Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanaope, nayenso anapita kukachita chigololo. 9Chiwerewere cha Israeli chinali chochititsa manyazi kotero kuti chinayipitsa dziko lonse. Anachita chigololo popembedza mafano a miyala ndi mitengo. 10Israeli atachita zonsezi, Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanabwerere kwa Ine ndi mtima wake wonse, koma mwachiphamaso chabe,” akutero Yehova.

11Yehova anandiwuza kuti, “Kusakhulupirika kwa Israeli nʼkochepa kuyerekeza ndi kusakhulupirika kwa Yuda. 12Pita ukalalikire kumpoto uthenga wakuti,

“ ‘Israeli wosakhulupirikawe, bwerera,’ akutero Yehova.

‘Sindidzakukalipira mpaka kalekale,

pakuti ndine wachifundo,’ akutero Yehova.

‘Sindidzakukwiyira mpaka kalekale.

13Ungovomera kulakwa kwako

kuti unawukira Yehova Mulungu wako.

Vomera kuti unayendayenda kukapembedza milungu yachilendo

pansi pa mtengo uliwonse wogudira,

ndiponso kuti sunandimvere,’ ”

akutero Yehova.

14“Bwererani, ana osakhulupirika, pakuti ndine mbuye wanu,” akutero Yehova. “Ndinakusankhani, mmodzimmodzi kuchokera ku mudzi uliwonse ndiponso awiriawiri kuchokera ku banja lililonse. 15Ndipo ndidzakupatsani abusa a pamtima panga amene adzakutsogolerani mwanzeru ndi mwaluntha. 16Masiku amenewo mukadzachulukana kwambiri mʼdzikomo, anthu sadzanenanso za ‘Bokosi la Chipangano la Yehova’ kapena kuliganizira. Sadzalikumbukiranso kapena kulifuna, ndipo sadzapanganso lina,”

akutero Yehova.

17Nthawi imeneyo adzatcha Yerusalemu Mpando Waufumu wa Yehova, ndipo mitundu yonse ya anthu idzasonkhana mu Yerusalemu pamaso pa Yehova. Sadzawumiriranso kutsata mitima yawo yoyipa. 18Masiku amenewo fuko la Yuda lidzaphatikizana ndi fuko la Israeli, onse pamodzi adzachokera ku dziko la kumpoto kupita ku dziko limene ndinapatsa makolo awo, kuti likhale cholowa.

19“Ine mwini ndinati,

“ ‘Ndikanakonda bwanji kukukhazikani pakati pa ana anga

ndikukupatsani dziko labwino kwambiri,

cholowa chokongola kwambiri kuposa cha mitundu ina ya anthu.’

Ndinaganiza kuti mudzanditcha Ine ‘Atate’

ndi kuti simudzaleka kunditsata.

20Koma monga mkazi wosakhulupirika amasiya mwamuna wake,

momwemonso inu mwakhala osakhulupirika kwa Ine, inu fuko la Israeli,”

akutero Yehova.

21Mawu akumveka pa magomo,

Aisraeli akulira ndi kupempha chifundo

chifukwa anatsata njira zoyipa

ndi kuyiwala Yehova Mulungu wawo.

22Inu mukuti, “Bwererani, anthu osakhulupirika;

ndidzachiritsa kubwerera mʼmbuyo kwanu.”

“Inde, tidzabwerera kwa Inu

pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.

23Ndithu kupembedza pa magomo

komanso kuchita maphwando pa mapiri zilibe phindu.

Zoonadi chipulumutso cha Israeli

chili mwa Yehova Mulungu wathu basi.

24Kuyambira pa ubwana wathu milungu yochititsa manyazi ija yakhala ikutiwonongetsa phindu

la ntchito za makolo athu,

nkhosa ndi ngʼombe zawo,

ana awo aamuna ndi aakazi.

25Tilekeni tigone pansi mwa manyazi,

ndipo kunyozeka kwathu kutiphimbe.

Paja tachimwira Yehova Mulungu wathu,

ife pamodzi ndi makolo athu

kuyambira nthawi ya ubwana wathu mpaka lero lino

sitinamvere Yehova Mulungu wathu.”