Yeremiya 27 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 27:1-22

Yuda Adzatumikira Nebukadinezara

1Zedekiya mwana wa Yosiya, mfumu ya ku Yuda, atangoyamba kulamulira, Yehova anawuza Yeremiya kuti, 2“Tenga zingwe zomangira ndi mitengo ya goli ndipo uzimangirire mʼkhosi mwako. 3Tsono utumize uthenga kwa mafumu a Edomu, Mowabu, Amoni, Turo ndi Sidoni kudzera mwa amithenga amene abwera ku Yerusalemu kwa Zedekiya, mfumu ya Yuda. 4Uwapatse uthenga wokapereka kwa ambuye awo ndipo uwawuze kuti: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Mukawuze ambuye anu kuti: 5Ndi mphamvu zanga ndi dzanja langa lamphamvu ndinalenga dziko lapansi ndi anthu ake onse pamodzi ndi nyama zili mʼmenemo, ndipo ndimalipereka kwa aliyense amene ndikufuna. 6Tsopano ndidzapereka mayiko anu onse kwa mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni. Ndamupatsanso nyama zakuthengo zonse kuti zimutumikire. 7Anthu a mitundu yonse adzamutumikira iyeyo, mwana wake ndi chidzukulu chake mpaka nthawi itakwana yoti dziko lake liwonongedwe. Pamenepo mitundu yambiri ndi mafumu amphamvu adzamugonjetsa.

8“ ‘Koma ngati anthu a mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse adzakana kutumikira Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kapena kusenza goli lake, Ine ndidzalanga mtundu umenewo ndi lupanga, ndi njala ndi mliri, akutero Yehova, mpaka nditawapereka mʼmanja mwake kotheratu. 9Choncho musamvere aneneri anu, owombeza anu, otanthauza maloto anu, amawula anu kapena amatsenga anu akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni.’ 10Iwo akukuloserani zabodza kotero kuti adani adzakuchotsani mʼdziko lanu nʼkupita nanu ku dziko lakutali. Ndidzakupirikitsani ndi kukuwonongani kotheratu. 11Koma ngati mtundu wina uliwonse udzagonjera mfumu ya ku Babuloni ndi kuyitumukira, ndidzawusiya kuti ukhale mʼdziko lake kuti uzilima ndi kukhalamo, akutero Yehova.’ ”

12Uthenga womwewu ndinawuzanso Hezekiya mfumu ya Yuda. Ndinati, “Gonjerani mfumu ya ku Babuloni. Itumikireni iyoyo pamodzi ndi anthu ake ndipo mudzakhala ndi moyo. 13Nanga inu ndi anthu anu, muferenji ndi lupanga, ndi njala, ndi mliri, zimene Yehova waopsezera mtundu wina uliwonse umene sudzatumikira mfumu ya ku Babuloni? 14Musamvere mawu a aneneri akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni,’ chifukwa zimene akukuloseranizo nʼzabodza. 15Sindinawatume ngakhale iwo akulosera mʼdzina langa. Nʼchifukwa chake, ndidzakupirikitsani ndipo mudzawonongeka kotheratu, inu pamodzi ndi aneneri amene akunenera zabodza kwa inu.”

16Kenaka ndinawuza ansembe pamodzi ndi anthu ena onse kuti, “Yehova akuti: Musamvere aneneri amene akumanena kuti, ‘Posachedwapa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zibwera kuchokera ku Babuloni.’ Iwowo akunenera zabodza kwa inu. 17Musawamvere. Tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo mudzakhala ndi moyo. Mzindawu usandukirenji bwinja? 18Ngati iwo ndi aneneri ndipo ali ndi mawu a Yehova, apempheretu kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti ziwiya zimene zatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndiponso mu Yerusalemu zisatengedwe kupita ku Babuloni. 19Pakuti Yehova akunena za zipilala, za mbiya ya madzi, maphaka ndi ziwiya zina zimene zatsala mu Yerusalemu. 20Izi ndi zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni sanatenge pamene anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda kupita ku Babuloni kuchokera ku Yerusalemu, pamodzi ndi anthu olemekezeka a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. 21Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena za zinthu zimene zinatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndi mu Yerusalemu kuti, 22‘Zidzatengedwa kupita ku Babuloni ndipo zidzakhala kumeneko mpaka tsiku limene ndidzawakumbukirenso,’ akutero Yehova. ‘Pamenepo ndidzazitenganso ndi kuzibwezanso ku malo ano.’ ”

New Russian Translation

Иеремия 27:1-22

Иудея должна покориться Вавилону

1В начале правления иудейского царя Цедекии, сына Иосии27:1 Цедекия правил в 597–586 гг. до н. э., к Иеремии было такое слово от Господа: 2Так мне сказал Господь:

– Сделай ярмо из ремней и палок и надень его на шею. 3И пошли весть27:3 Или: «пошли такие же». царям Эдома, Моава, Аммона, Тира и Сидона через послов, которые прибыли в Иерусалим к Цедекии, царю Иудеи. 4Вели им передать известие своим господам, накажи им: «Так говорит Господь Сил, Бог Израиля: „Скажите своим господам вот что: 5Своей великой силой и простертой рукой Я создал землю, людей и животных на земле, и Я даю это кому пожелаю. 6Ныне Я отдам все ваши земли Моему слуге Навуходоносору, царю Вавилона; Я покорю ему даже диких зверей. 7Все народы будут служить ему, и его сыну, и его внуку, пока не пробьет час этой страны. Ему покорятся многочисленные народы и великие цари.

8А если какой-нибудь народ или царство не станет служить Навуходоносору, царю Вавилона, и не пригнет свою шею под его ярмо, Я буду наказывать этот народ мечом, голодом и мором, – возвещает Господь, – пока не погублю их его рукой. 9Поэтому не слушайте ваших лжепророков, ворожей, толкователей снов, вызывателей умерших и чародеев, которые говорят вам: «Вы не будете служить царю Вавилона». 10Они пророчествуют вам ложь, которая удалит вас от ваших земель; Я изгоню вас, и вы погибнете. 11А если какой-нибудь народ пригнет шею под ярмо царя Вавилона и будет ему служить, Я оставлю этот народ на его земле, чтобы он возделывал ее и жил на ней“», – возвещает Господь.

12Цедекии, царю Иудеи, я говорил то же самое. Я сказал:

– Пригни шею под ярмо царя Вавилона; служи ему и его народу, и будешь жить. 13Зачем тебе и твоему народу гибнуть от меча, голода и мора, которыми Господь грозит всякому народу, что не станет служить царю Вавилона? 14Не слушай слов лжепророков, говорящих тебе: «Вы не будете служить царю Вавилона», так как они пророчествуют тебе ложь. 15«Я не посылал их, – возвещает Господь. – Они пророчествуют Моим именем ложь, чтобы Я изгнал вас, и вы погибли – и вы, и пророки, которые вам пророчествуют».

16Затем я сказал священникам и всему народу:

– Так говорит Господь: Не слушайте пророков, которые говорят: «Скоро утварь Господнего дома принесут из Вавилона обратно»27:16 См. 4 Цар. 24:10-13.. Они пророчествуют вам ложь. 17Не слушайте их. Служите царю Вавилона и будете жить. Зачем этому городу превращаться в развалины? 18Если они пророки и у них слово Господне, то пусть лучше попросят Господа Сил, чтобы та утварь, которая еще осталась в доме Господа, во дворце царя Иудеи и в Иерусалиме, не отправилась в Вавилон. 19Ведь так говорит Господь Сил о колоннах, о бронзовом море27:19 Море – это большой бронзовый бассейн, находившийся во дворе храма и предназначавшийся для ритуальных омовений священников (см. 3 Цар. 7:23-26; 2 Пар. 4:6)., и передвижных подставках и прочей утвари, оставшейся в городе, 20которую Навуходоносор, царь Вавилона, не забрал с собой, когда он увел иудейского царя Иехонию, сына Иоакима, в плен из Иерусалима в Вавилон вместе со знатью Иудеи и Иерусалима – 21да, так Господь Сил, Бог Израиля, говорит об утвари, оставшейся в доме Господнем, во дворце царя Иудеи и в Иерусалиме: 22Ее заберут в Вавилон, и она останется там до того дня, когда Я приду за ней, – возвещает Господь. – Тогда Я заберу ее и верну на это место.