Yeremiya 23 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 23:1-40

Nthambi Yolungama

1“Tsoka kwa abusa amene akuwononga ndi kubalalitsa nkhosa za pabusa panga!” akutero Yehova. 2Nʼchifukwa chake Yehova, Mulungu wa Israeli, ponena za abusa amene akuweta anthu anga akuti, “Mwabalalitsa ndi kumwaza nkhosa zanga. Komanso simunazisamale bwino. Choncho ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu,” akutero Yehova. 3“Pambuyo pake Ine mwini wakene ndidzasonkhanitsa nkhosa zanga zotsala, kuzichotsa ku mayiko onse kumene ndinazibalalitsira ndi kuzibweretsanso ku msipu wawo. Kumeneko zidzaswana ndi kuchulukana. 4Ndidzazipatsa abusa amene adzaziweta, ndipo sizidzaopanso kapena kuchita mantha, ndipo palibe imene idzasochera,” akutero Yehova.

5Yehova akuti, “Masiku akubwera,

pamene ndidzaphukitsira Davide Nthambi yowongoka.

Imeneyi ndiye mfumu imene idzalamulira mwanzeru, mwachilungamo ndi mosakondera mʼdziko.

6Pa masiku a ulamuliro wake Yuda adzapulumuka

ndipo Israeli adzakhala pamtendere.

Dzina limene adzamutcha ndi ili:

Yehova ndiye Chilungamo Chathu.

7Choncho, masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene anthu sadzanenanso polumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku Igupto,’ 8koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa zidzukulu za Israeli ku dziko lakumpoto ndi ku mayiko konse kumene anawabalalitsira.’ Ndipo iwo adzawabweretsa ku dziko lawolawo.”

Aneneri Onyenga

9Kunena za aneneri awa:

Mtima wanga wasweka;

mʼnkhongono mwati zii.

Ndakhala ngati munthu woledzera,

ngati munthu amene wasokonezeka ndi vinyo,

chifukwa cha Yehova

ndi mawu ake opatulika.

10Dziko ladzaza ndi anthu achigololo;

lili pansi pa matemberero.

Dziko lasanduka chipululu ndipo msipu wawuma.

Aneneri akuchita zoyipa

ndipo akugwiritsa ntchito mphamvu zawo molakwika.

11“Mneneri ngakhale wansembe onse sapembedza Yehova.

Amachita zoyipa ngakhale mʼnyumba yanga,”

akutero Yehova.

12“Nʼchifukwa chake njira zawo zidzakhala zoterera;

adzawapirikitsira ku mdima

ndipo adzagwera kumeneko.

Adzaona zosaona

mʼnthawi ya chilango chawo,”

akutero Yehova.

13“Pakati pa aneneri a ku Samariya

ndinaona chonyansa ichi:

Ankanenera mʼdzina la Baala

ndipo anasocheretsa anthu anga, Aisraeli.

14Ndipo pakati pa aneneri a ku Yerusalemu

ndaonapo chinthu choopsa kwambiri:

amachita chigololo, amanena bodza

ndipo amalimbitsa mtima anthu ochita zoyipa.

Choncho palibe amene amasiya zoyipa zake.

Kwa Ine anthu onsewa

ali ngati a ku Sodomu ndi Gomora.”

15Choncho ponena za aneneriwa Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Ndidzawadyetsa zakudya zowawa

ndi kuwamwetsa madzi a ndulu,

chifukwa uchimo umene wafalikira mʼdziko lonse

ndi wochokera kwa aneneri a ku Yerusalemuwa.”

16Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Musamvere zimene aneneri amenewa akulosera kwa inu;

zomwe aloserazo nʼzachabechabe.

Iwo akungoyankhula za masomphenya a mʼmitima mwawo basi,

osati zochokera kwa Yehova.

17Iwo amapita ndi kumakawuza amene amandinyoza Ine kuti,

‘zinthu zidzakuyenderani bwino.’

Kwa iwo amene amawumirira kutsata zofuna za mitima yawo amakawawuza kuti,

‘palibe choyipa chimene chidzakugwereni.’ ”

18Ine ndikuti, “Koma ndani wa iwo amene anakhalapo mu msonkhano wa Yehova?

Ndani anaonapo kapena kumvapo mawu ake?

Ndani mwa iwo analabadirako za mawu ake ndi kuwamvera?

19Taonani ukali wa Yehova

uli ngati chimphepo chamkuntho,

inde ngati namondwe.

Ndipo adzakantha mitu ya anthu oyipa.

20Mkwiyo wa Yehova sudzaleka

mpaka atachita zonse zimene

anatsimikiza mu mtima mwake.

Mudzazizindikira bwino zimenezi

masiku akubwerawa.”

21Yehova anati, “Ine sindinatume aneneri amenewa,

komabe iwo athamanga uku ndi uku kulalikira uthenga wawo;

Ine sindinawayankhule,

komabe iwo ananenera.

22Iwo akanakhala pa msonkhano wanga

ndiye kuti akanamayankhula mawu anga kwa anthu anga.

Komanso bwenzi atawachotsa anthu anga mʼnjira zawo zoyipa

kuti aleke machimo awo.”

23Yehova akuti, “Kodi ndimakhala Mulungu pokhapokha ndikakhala pafupi,

ndiye sindine Mulungu?

24Kodi wina angathe kubisala

Ine osamuona?”

“Kodi Ine sindili ponseponse kumwamba ndi dziko lapansi?”

Akutero Yehova.

25“Ndamva zimene aneneri akuyankhula. Iwo amalosera zabodza mʼdzina langa nʼkumati, ‘Ndalota! Ndalota!’ 26Kodi zabodzazi zidzakhalabe mʼmitima ya aneneriwa mpaka liti? Iwotu amalosera zonyenga za mʼmitima yawo. 27Aneneriwa amakhulupirira kuti anthu anga adzayiwala mawu anga akamamva za maloto awo amene amayankhulana ngati mmene anachitira makolo awo popembedza Baala. 28Mneneri amene ali ndi maloto afotokoze malotowo. Koma iye amene ali ndi mawu anga alalikire mawuwo mokhulupirika. Kodi phesi lingafanane ndi chimanga? 29Kodi suja mawu anga amatentha ngati moto? Suja mawu anga amaphwanya monga ichitira nyundo kuphwanya miyala?” Akutero Yehova.

30Yehova akuti, “Nʼchifukwa chake, Ine ndikudana nawo aneneri amene amaberana okhaokha mawu nʼkumati mawuwo ndi a Yehova.” 31Yehova akuti, “Inde, Ine ndikudana ndi aneneri amene amakonda kuyankhula zabodza nʼkumanena kuti, ‘Amenewa ndi mawu a Yehova.’ ” 32Yehova akuti, “Ndithudi, Ine ndikudana ndi aneneri a maloto abodzawa. Iwo amafotokoza malotowo nʼkumasocheretsa anthu anga ndi bodza lawo losachita nalo manyazilo, chonsecho Ine sindinawatume kapena kuwalamula. Iwo sathandiza anthuwa ndi pangʼono pomwe,” akutero Yehova.

Uthenga Wabodza ndi Aneneri Abodza

33Yehova anawuza Yeremiya kuti, “Anthu awa, kapena mneneri, kapenanso wansembe, akakufunsa kuti, ‘Kodi uthenga wolemetsa wa Yehova ukuti chiyani?’ uwawuze kuti, ‘Inuyo ndinu katundu wolemetsa Yehova, ndipo adzakutayani.’ 34Ngati mneneri kapena wansembe kapenanso munthu wina aliyense anena kuti, ‘Uthenga wolemetsa wa Yehova ndi uwu,’ Ine ndidzalanga munthu ameneyo pamodzi ndi banja lake. 35Koma chimene aliyense wa inu azifunsa kwa mnzake kapena mʼbale wake ndi ichi: ‘Kodi Yehova wayankha chiyani?’ kapena ‘Yehova wayankhula chiyani?’ 36Koma musanenenso kuti ‘nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ chifukwa mawu a munthu aliyense ndiwo uthenga wa iye mwini, kotero kuti inu mumakhotetsa mawu a Mulungu wamoyo, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wathu. 37Tsono iwe Yeremiya udzamufunse mneneri kuti, ‘Kodi Yehova wakuyankha chiyani?’ kapena, ‘Kodi Yehova wayankhula chiyani?’ 38Ngati mudzanena kuti, ‘Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ ndiye tsono Yehova akuti, ‘Popeza mwagwiritsa ntchito mawu akuti: Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova, mawu amene ndinakuletsani kuti musawatchule, 39ndiye kuti Ine ndidzakunyamulani ngati katundu nʼkukuponyani kutali. Ndidzakuchotsani pamaso panga, inuyo pamodzi ndi mzinda umene ndinakupatsani inu ndi makolo anu. 40Ndidzakunyozani mpaka muyaya. Ndidzakuchititsani manyazi osayiwalika.’ ”

King James Version

Jeremiah 23:1-40

1Woe be unto the pastors that destroy and scatter the sheep of my pasture! saith the LORD. 2Therefore thus saith the LORD God of Israel against the pastors that feed my people; Ye have scattered my flock, and driven them away, and have not visited them: behold, I will visit upon you the evil of your doings, saith the LORD. 3And I will gather the remnant of my flock out of all countries whither I have driven them, and will bring them again to their folds; and they shall be fruitful and increase. 4And I will set up shepherds over them which shall feed them: and they shall fear no more, nor be dismayed, neither shall they be lacking, saith the LORD.

5¶ Behold, the days come, saith the LORD, that I will raise unto David a righteous Branch, and a King shall reign and prosper, and shall execute judgment and justice in the earth. 6In his days Judah shall be saved, and Israel shall dwell safely: and this is his name whereby he shall be called, THE LORD OUR RIGHTEOUSNESS.23.6 THE LORD…: Heb. Jehovah-tsidkenu 7Therefore, behold, the days come, saith the LORD, that they shall no more say, The LORD liveth, which brought up the children of Israel out of the land of Egypt; 8But, The LORD liveth, which brought up and which led the seed of the house of Israel out of the north country, and from all countries whither I had driven them; and they shall dwell in their own land.

9¶ Mine heart within me is broken because of the prophets; all my bones shake; I am like a drunken man, and like a man whom wine hath overcome, because of the LORD, and because of the words of his holiness. 10For the land is full of adulterers; for because of swearing the land mourneth; the pleasant places of the wilderness are dried up, and their course is evil, and their force is not right.23.10 swearing: or, cursing23.10 course: or, violence 11For both prophet and priest are profane; yea, in my house have I found their wickedness, saith the LORD. 12Wherefore their way shall be unto them as slippery ways in the darkness: they shall be driven on, and fall therein: for I will bring evil upon them, even the year of their visitation, saith the LORD. 13And I have seen folly in the prophets of Samaria; they prophesied in Baal, and caused my people Israel to err.23.13 folly: or, an absurd thing: Heb. unsavoury 14I have seen also in the prophets of Jerusalem an horrible thing: they commit adultery, and walk in lies: they strengthen also the hands of evildoers, that none doth return from his wickedness: they are all of them unto me as Sodom, and the inhabitants thereof as Gomorrah.23.14 an…: or, filthiness 15Therefore thus saith the LORD of hosts concerning the prophets; Behold, I will feed them with wormwood, and make them drink the water of gall: for from the prophets of Jerusalem is profaneness gone forth into all the land.23.15 profaneness: or, hypocrisy 16Thus saith the LORD of hosts, Hearken not unto the words of the prophets that prophesy unto you: they make you vain: they speak a vision of their own heart, and not out of the mouth of the LORD. 17They say still unto them that despise me, The LORD hath said, Ye shall have peace; and they say unto every one that walketh after the imagination of his own heart, No evil shall come upon you.23.17 imagination: or, stubbornness 18For who hath stood in the counsel of the LORD, and hath perceived and heard his word? who hath marked his word, and heard it?23.18 counsel: or, secret 19Behold, a whirlwind of the LORD is gone forth in fury, even a grievous whirlwind: it shall fall grievously upon the head of the wicked. 20The anger of the LORD shall not return, until he have executed, and till he have performed the thoughts of his heart: in the latter days ye shall consider it perfectly. 21I have not sent these prophets, yet they ran: I have not spoken to them, yet they prophesied. 22But if they had stood in my counsel, and had caused my people to hear my words, then they should have turned them from their evil way, and from the evil of their doings. 23Am I a God at hand, saith the LORD, and not a God afar off? 24Can any hide himself in secret places that I shall not see him? saith the LORD. Do not I fill heaven and earth? saith the LORD. 25I have heard what the prophets said, that prophesy lies in my name, saying, I have dreamed, I have dreamed. 26How long shall this be in the heart of the prophets that prophesy lies? yea, they are prophets of the deceit of their own heart; 27Which think to cause my people to forget my name by their dreams which they tell every man to his neighbour, as their fathers have forgotten my name for Baal. 28The prophet that hath a dream, let him tell a dream; and he that hath my word, let him speak my word faithfully. What is the chaff to the wheat? saith the LORD.23.28 that hath a dream: Heb. with whom is, etc 29Is not my word like as a fire? saith the LORD; and like a hammer that breaketh the rock in pieces? 30Therefore, behold, I am against the prophets, saith the LORD, that steal my words every one from his neighbour. 31Behold, I am against the prophets, saith the LORD, that use their tongues, and say, He saith.23.31 that…: or, that smooth their tongues 32Behold, I am against them that prophesy false dreams, saith the LORD, and do tell them, and cause my people to err by their lies, and by their lightness; yet I sent them not, nor commanded them: therefore they shall not profit this people at all, saith the LORD.

33¶ And when this people, or the prophet, or a priest, shall ask thee, saying, What is the burden of the LORD? thou shalt then say unto them, What burden? I will even forsake you, saith the LORD. 34And as for the prophet, and the priest, and the people, that shall say, The burden of the LORD, I will even punish that man and his house.23.34 punish: Heb. visit upon 35Thus shall ye say every one to his neighbour, and every one to his brother, What hath the LORD answered? and, What hath the LORD spoken? 36And the burden of the LORD shall ye mention no more: for every man’s word shall be his burden; for ye have perverted the words of the living God, of the LORD of hosts our God. 37Thus shalt thou say to the prophet, What hath the LORD answered thee? and, What hath the LORD spoken? 38But since ye say, The burden of the LORD; therefore thus saith the LORD; Because ye say this word, The burden of the LORD, and I have sent unto you, saying, Ye shall not say, The burden of the LORD; 39Therefore, behold, I, even I, will utterly forget you, and I will forsake you, and the city that I gave you and your fathers, and cast you out of my presence: 40And I will bring an everlasting reproach upon you, and a perpetual shame, which shall not be forgotten.