Yeremiya 20 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 20:1-18

Yeremiya ndi Pasuri

1Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi. 2Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova. 3Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse. 4Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo. 5Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni. 6Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’ ”

Madandawulo a Yeremiya

7Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi;

Inu ndi wamphamvu kuposa ine ndipo munandipambana.

Anthu akundinyoza tsiku lonse.

Aliyense akundiseka kosalekeza.

8Nthawi iliyonse ndikamayankhula,

ndimafuwula kunena kuti, ziwawa kuno! Tikuwonongeka!

Mawu anu Yehova andisandutsa chinthu chonyozeka

ndipo ndimachitidwa chipongwe tsiku lonse.

9Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye

kapena kuyankhulanso mʼdzina lake,”

mawu anu amayaka ngati moto mu mtima mwanga,

amakhaladi ngati moto wotsekeredwa mʼmafupa anga.

Ndapirira kusunga mawu anu mu mtima mwanga osawatulutsa,

koma sindingathe kupirirabe.

10Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti,

“Zoopsa ku mbali zonse!

Kamunenezeni! Tiyeni tikamuneneze!”

Onse amene anali abwenzi anga

akuyembekezera kuti ndigwa pansi, akumanena kuti,

“Mwina mwake adzanyengedwa;

tidzamugwira

ndi kulipsira pa iye.”

11Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu.

Nʼchifukwa chake ondizunza adzalephera ndipo sadzandipambana.

Adzachita manyazi kwambiri chifukwa sadzapambana.

Manyazi awo sadzayiwalika konse.

12Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama

ndipo mupenya za mu mtima mwa munthu.

Ndiloleni kuti ndione kuti mwalipsira adani anga

popeza ndapereka mlandu wanga kwa Inu.

13Imbirani Yehova!

Mutamandeni Yehova!

Iye amapulumutsa wosauka

mʼmanja mwa anthu oyipa.

14Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa!

Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!

15Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga

ndi uthenga woti:

“Kwabadwa mwana wamwamuna!”

16Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene

Yehova anayiwononga mopanda chisoni.

Amve mfuwu mmawa,

phokoso la nkhondo masana.

17Chifukwa sanandiphere mʼmimba,

kuti amayi anga asanduke manda anga,

mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.

18Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni

kuti moyo wanga

ukhale wamanyazi wokhawokha?

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Jeremías 20:1-18

Jeremías y Pasur

1Cuando el sacerdote Pasur hijo de Imer, que era el oficial principal de la casa del Señor, oyó lo que Jeremías profetizaba, 2mandó que golpearan al profeta Jeremías y que lo colocaran en el cepo ubicado en la puerta alta de Benjamín, junto a la casa del Señor. 3A la mañana siguiente, cuando Pasur liberó a Jeremías del cepo, Jeremías le dijo: «El Señor ya no te llama Pasur, sino “Terror por todas partes”. 4Porque así dice el Señor: “Te voy a convertir en terror para ti mismo y para tus amigos, los cuales caerán bajo la espada de sus enemigos, y tú mismo lo verás. Entregaré a todo Judá en manos del rey de Babilonia, el cual los deportará a Babilonia o los matará a filo de espada. 5Además, pondré en manos de sus enemigos toda la riqueza de esta ciudad, todos sus productos y objetos de valor, y todos los tesoros de los reyes de Judá, para que los saqueen y se los lleven a Babilonia. 6Y tú, Pasur, irás al cautiverio de Babilonia junto con toda tu familia. Allí morirás, y allí serás enterrado, con todos tus amigos, a quienes profetizabas mentiras”».

Quejas de Jeremías

7¡Me sedujiste, Señor,

y yo me dejé seducir!

Fuiste más fuerte que yo,

y me venciste.

Todo el mundo se burla de mí;

se ríen de mí todo el tiempo.

8Cada vez que hablo, es para gritar:

«¡Violencia! ¡Violencia!»

Por eso la palabra del Señor

no deja de ser para mí

un oprobio y una burla.

9Si digo: «No me acordaré más de él,

ni hablaré más en su nombre»,

entonces su palabra en mi interior

se vuelve un fuego ardiente

que me cala hasta los huesos.

He hecho todo lo posible por contenerla,

pero ya no puedo más.

10Escucho a muchos decir con sorna:

«¡Hay terror por todas partes!»

y hasta agregan: «¡Denunciadlo!

¡Vamos a denunciarlo!»

Aun mis mejores amigos

esperan que tropiece.

También dicen: «Quizá lo podamos seducir.

Entonces lo venceremos

y nos vengaremos de él».

11Pero el Señor está conmigo

como un guerrero poderoso;

por eso los que me persiguen

caerán y no podrán prevalecer,

fracasarán y quedarán avergonzados.

Eterna será su deshonra;

jamás será olvidada.

12Tú, Señor Todopoderoso,

que examinas al justo,

que sondeas el corazón y la mente,

hazme ver tu venganza sobre ellos,

pues a ti he encomendado mi causa.

13¡Cantad al Señor, alabadlo!

Él salva a los pobres

del poder de los malvados.

14¡Maldito el día en que nací!

¡Maldito el día en que mi madre me dio a luz!

15¡Maldito el hombre que alegró a mi padre

cuando le dijo: «¡Te ha nacido un hijo varón!»!

16¡Que sea tal hombre como las ciudades

que el Señor destruyó sin compasión!

¡Que oiga gritos en la mañana

y alaridos de guerra al mediodía!

17¿Por qué Dios no me dejó morir

en el seno de mi madre?

Así ella habría sido mi tumba,

y yo jamás habría salido de su vientre.

18¿Por qué tuve que salir del vientre

solo para ver problemas y aflicción,

y para terminar mis días en vergüenza?