Yeremiya 20 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 20:1-18

Yeremiya ndi Pasuri

1Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi. 2Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova. 3Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse. 4Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo. 5Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni. 6Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’ ”

Madandawulo a Yeremiya

7Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi;

Inu ndi wamphamvu kuposa ine ndipo munandipambana.

Anthu akundinyoza tsiku lonse.

Aliyense akundiseka kosalekeza.

8Nthawi iliyonse ndikamayankhula,

ndimafuwula kunena kuti, ziwawa kuno! Tikuwonongeka!

Mawu anu Yehova andisandutsa chinthu chonyozeka

ndipo ndimachitidwa chipongwe tsiku lonse.

9Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye

kapena kuyankhulanso mʼdzina lake,”

mawu anu amayaka ngati moto mu mtima mwanga,

amakhaladi ngati moto wotsekeredwa mʼmafupa anga.

Ndapirira kusunga mawu anu mu mtima mwanga osawatulutsa,

koma sindingathe kupirirabe.

10Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti,

“Zoopsa ku mbali zonse!

Kamunenezeni! Tiyeni tikamuneneze!”

Onse amene anali abwenzi anga

akuyembekezera kuti ndigwa pansi, akumanena kuti,

“Mwina mwake adzanyengedwa;

tidzamugwira

ndi kulipsira pa iye.”

11Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu.

Nʼchifukwa chake ondizunza adzalephera ndipo sadzandipambana.

Adzachita manyazi kwambiri chifukwa sadzapambana.

Manyazi awo sadzayiwalika konse.

12Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama

ndipo mupenya za mu mtima mwa munthu.

Ndiloleni kuti ndione kuti mwalipsira adani anga

popeza ndapereka mlandu wanga kwa Inu.

13Imbirani Yehova!

Mutamandeni Yehova!

Iye amapulumutsa wosauka

mʼmanja mwa anthu oyipa.

14Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa!

Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!

15Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga

ndi uthenga woti:

“Kwabadwa mwana wamwamuna!”

16Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene

Yehova anayiwononga mopanda chisoni.

Amve mfuwu mmawa,

phokoso la nkhondo masana.

17Chifukwa sanandiphere mʼmimba,

kuti amayi anga asanduke manda anga,

mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.

18Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni

kuti moyo wanga

ukhale wamanyazi wokhawokha?

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米书 20:1-18

耶利米受迫害

1音麦的儿子巴施户珥祭司在耶和华的殿中做总管。他听见耶利米预言这些事, 2便下令殴打耶利米先知,把他囚禁在耶和华殿的便雅悯上门处。 3第二天,他释放了耶利米耶利米对他说:“耶和华不再叫你巴施户珥,要叫你玛歌珥·米撒毕20:3 玛歌珥·米撒毕”意思是“四面有恐怖”。4因为耶和华说,‘我要使你和你的朋友都惊慌失措,让你亲眼看见你的朋友死在敌人刀下;我要把犹大人都交在巴比伦王手中,使他们或被杀或被掳到巴比伦5我要把这城里所有的财富、出产、珍宝,甚至犹大列王的宝物都交给敌人,带到巴比伦作战利品。 6巴施户珥、你所有的家人以及听你说假预言的朋友都要被掳到巴比伦,死在那里,葬在那里。’”

耶利米的抱怨

7耶和华啊,

你欺骗我,我被你骗了。

你制服我,胜过我。

如今,我成了人们终日嘲笑、戏弄的对象。

8我每次说预言,都大声疾呼:

“暴力和毁灭要来了!”

我因传讲耶和华的话而终日遭受侮辱和讥笑。

9有时我打算不再提起耶和华,

不再奉祂的名宣讲,

但祂的话如一团火在我心中燃烧,

憋在我骨头里,

我无法忍住不说。

10我听见许多人窃窃私语:

“看那个说‘四面有恐怖’的人,

我们告发他!告发他!”

我的好友都盼着我灭亡,说:

“或许他会受骗,

那样我们便能打倒他,

一泄心头之恨。”

11但耶和华与我同在,

祂像勇猛的战士。

迫害我的人必一败涂地,

羞愧难当,留下永远的耻辱。

12考验义人、洞悉人心的万军之耶和华啊,

求你让我看见你报应他们,

因为我已向你禀明冤情。

13你们要歌颂耶和华!

要赞美耶和华!

因为祂从恶人手中救出穷人。

14愿我出生的那天受咒诅!

愿我母亲生我的那天不蒙祝福!

15愿那告诉我父亲喜得贵子、

使他欢喜的人受咒诅!

16愿那人像被耶和华无情毁灭的城!

愿他早晨听见哀鸣,

中午听见战争的呐喊,

17因为他没有把我杀死在母腹中,

没有使母腹成为我的坟墓,

让我永远留在里面。

18为什么我要从母胎出来,

经历患难和痛苦,

在羞辱中度过一生呢?