Yeremiya 2 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 2:1-37

Aisraeli Asiya Mulungu

1Yehova anandiwuza kuti, 2“Pita ukalengeze kwa anthu a ku Yerusalemu kuti Yehova akuti,

“ ‘Ine ndikukumbukira mmene umakhulupirikira pa unyamata wako,

mmene unkandikondera ngati momwe amachitira mkwatibwi,

mmene unkanditsata mʼchipululu muja;

mʼdziko losadzalamo kanthu.

3Israeli anali wopatulika wa Yehova,

anali ngati zipatso zake zoyamba kucha pa nthawi yokolola;

onse amene anamuzunza anapezeka kuti ndi olakwa

ndipo mavuto anawagwera,’ ”

akutero Yehova.

4Imvani mawu a Yehova, inu zidzukulu za Yakobo,

inu mafuko onse a Israeli.

5Yehova akuti,

“Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji,

kuti andithawe?

Iwo anatsata milungu yachabechabe,

nawonso nʼkusanduka achabechabe.

6Iwo sanafunse nʼkomwe kuti, ‘Kodi Yehova ali kuti,

amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto

natitsogolera mʼchipululu mʼdziko lowuma

ndi lokumbikakumbika,

mʼdziko lopanda mvula ndi la mdima,

dziko limene munthu sadutsamo ndipo simukhala munthu aliyense?’

7Ndinakufikitsani ku dziko lachonde

kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina.

Koma inu mutafika munaliyipitsa dziko langa

ndi kusandutsa cholowa changa kukhala chonyansa.

8Ansembe nawonso sanafunse kuti,

‘Yehova ali kuti?’

Iwo amene amaphunzitsa malamulo sanandidziwe;

atsogoleri anandiwukira.

Aneneri ankanenera mʼdzina la Baala,

ndi kutsatira mafano achabechabe.

9“Chifukwa chake Ine ndidzakuyimbaninso mlandu,”

akutero Yehova.

“Ndipo ndidzayimbanso mlandu zidzukulu zanu.

10Pitani kumadzulo ku chilumba cha Kitimu, ndipo mukaone,

tumizani anthu ku Kedara kuti akafufuze bwino;

ndipo muona kuti zinthu zoterezi sizinachitikepo nʼkale lomwe:

11Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse umene unasinthapo milungu yake?

(Ngakhale kuti si milungu nʼkomwe).

Koma anthu anga asinthitsa Mulungu wawo waulemerero

ndi mafano achabechabe.

12Inu mayiko akumwamba, dabwani ndi zimenezi,

ndipo njenjemerani ndi mantha aakulu,”

akutero Yehova.

13“Popeza anthu anga achita machimo awiri:

Andisiya Ine

kasupe wa madzi a moyo,

ndi kukadzikumbira zitsime zawo,

zitsime zongʼaluka, zomwe sizingathe kusunga madzi.

14Israeli si wantchito kapena kapolo wobadwira mʼnyumba, ayi.

Nanga nʼchifukwa chiyani amuwononga chotere?

15Adani ake abangulira

ndi kumuopseza ngati mikango.

Dziko lake analisandutsa bwinja;

mizinda yake anayitentha popanda wokhalamo.

16Ndiponso Aigupto a ku Mefisi ndi a ku Tapanesi

akuphwanyani mitu.

17Zimenezitu zakuchitikirani

chifukwa munasiya Yehova Mulungu wanu

pamene Iye ankakutsogolerani pa njira yanu?

18Tsopano mudzapindula chiyani mukapita ku Igupto,

kukamwa madzi a mu Sihori?

Ndipo mudzapindulanji mukapita ku Asiriya,

kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?

19Kuyipa kwanuko kudzakulangani;

kubwerera mʼmbuyo kwanuko kudzakutsutsani.

Tsono ganizirani bwino,

popeza ndi chinthu choyipa

kundisiya Ine Yehova Mulungu wanu;

ndi chinthu chowawa ndithu kusandiopa Ine Mulungu wanu.

Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.

20“Kuyambira kalekale inu munathyola goli lanu

ndi kudula msinga zanu;

munanena kuti, ‘Sitidzakutumikirani!’

Ndithudi, inu mwakhala ngati mkazi wachiwerewere.

Mukupembedza milungu ina pa phiri lililonse lalitali

ndiponso pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.

21Ine ndinakudzala iwe ngati mtengo wampesa wosankhika;

unali mpesa wabwino kwambiri ndi wodalirika.

Nanga nʼchifukwa chiyani wasanduka mpesa

wachabechabe wonga wa kutchire?

22Ngakhale utasamba ndi soda

kapena kusambira sopo wambiri,

kuthimbirira kwa machimo ako kumaonekabe pamaso panga,”

akutero Ambuye Yehova.

23“Iwe ukunena bwanji kuti, ‘Ine sindinadziyipitse;

sindinatsatire Abaala’?

Takumbukira mmene unkandichimwira mʼchigwa muja;

zindikira bwino zomwe wachita.

Iwe uli ngati ngamira yayikazi yaliwiro

yomangothamanga uku ndi uku,

24wakhala ngati mbidzi yozolowera mʼchipululu,

yonka ninunkhiza pa nthawi yachisika.

Ndani angayiretse chilakolako chakecho?

Mphongo iliyonse yoyikhumba sidzavutika.

Pa nthawi yachisika chakecho mphongoyo idzayipeza.

25Iwe usathamange, nsapato zingakuthere kuphazi

ndi kukhosi kwako kuwuma ndi ludzu.

Koma unati, ‘Zamkutu!

Ine ndimakonda milungu yachilendo,

ndipo ndidzayitsatira.’

26“Monga momwe mbala imachitira manyazi pamene yagwidwa,

moteronso nyumba ya Israeli idzachita manyazi;

Aisraeliwo, mafumu ndi akuluakulu awo,

ansembe ndi aneneri awo.

27Iwo amawuza mtengo kuti, ‘Iwe ndiwe abambo athu,’

ndipo amawuza mwala kuti, ‘Iwe ndiye amene unatibala.’

Iwo andifulatira Ine,

ndipo safuna kundiyangʼana;

Koma akakhala pa mavuto amati,

‘Bwerani mudzatipulumutse!’

28Nanga ili kuti milungu yanu imene munadzipangira nokha?

Ibweretu ngati ingathe kukupulumutsani

pamene muli pamavuto!

Inu anthu a ku Yuda,

milungu yanu ndi yambiri kuchuluka kwake ngati mizinda yanu.

29“Kodi mukundizengeranji mlandu?

Nonse mwandiwukira,”

akutero Yehova.

30“Ine ndinalanga anthu ako popanda phindu;

iwo sanaphunzirepo kanthu.

Monga mkango wolusa,

lupanga lanu lapha aneneri anu.

31“Inu anthu a mʼbado uno, ganizirani bwino mawu a Yehova:

“Kodi Ine ndinakhalapo ngati chipululu kwa Israeli

kapena ngati dziko la mdima wandiweyani?

Chifukwa chiyani anthu anga akunena kuti, ‘Ife tili ndi ufulu omayendayenda;

sitidzabweranso kwa Inu’?

32Kodi namwali amayiwala zokongoletsera zake,

kapena kuyiwala zovala zake za ukwati?

Komatu anthu anga andiyiwala

masiku osawerengeka.

33Mumadziwa bwino njira zopezera zibwenzi!

Choncho ngakhale akazi oyipa omwe mumawaphunzitsa njira zanu.

34Ngakhale pa zovala zako anthu amapezapo

magazi a anthu osauka osalakwa.

Anthuwo simunawapeze akuthyola nyumba.

Komabe ngakhale zinthu zili chomwechi,

35inu mukunena kuti, ‘Ndife osalakwa,

sadzatikwiyira.’

Ndidzakuyimbani mlandu

chifukwa mukunena kuti, ‘Ife sitinachimwe.’

36Chifukwa chiyani

mukunkabe nimusinthasintha njira zanu?

Aigupto adzakukhumudwitsani

monga momwe Asiriya anakuchititsani manyazi.

37Mudzachokanso kumeneko

manja ali kunkhongo.

Popeza Ine Yehova ndawakana anthu amene munkawadalira,

choncho sadzakuthandizani konse.