Yeremiya 15 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 15:1-21

1Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite! 2Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti,

“ ‘Oyenera kufa adzafa;

oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga;

oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala;

oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’

3“Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga. 4Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.

5“Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu?

Kodi adzakulira ndani?

Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?

6Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova.

“Inu mukubwererabe mʼmbuyo.

Choncho Ine ndidzakukanthani.

Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.

7Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo

monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero.

Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga

chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.

8Ndinachulukitsa amayi awo amasiye

kupambana mchenga wa kunyanja.

Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna

dzuwa lili pamutu.

Mwadzidzidzi ndinawagwetsera

kuwawa mtima ndi mantha.

9Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka

ndipo akupuma wefuwefu.

Dzuwa lake lalowa ukanali usana;

anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru.

Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo

kuti awaphe ndi lupanga,”

akutero Yehova.

10Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine,

munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse!

Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu,

komatu aliyense akunditemberera.

11Yehova anati,

“Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino.

Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka

ndi ya mavuto awo.

12“Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo,

makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.

13Anthu ako ndi chuma chako

ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro,

chifukwa cha machimo anu onse

a mʼdziko lanu lonse.

14Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu

mʼdziko limene inu simulidziwa,

chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto

umene udzakutenthani.”

15Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse;

kumbukireni ndi kundisamalira.

Ndilipsireni anthu ondizunza.

Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga.

Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.

16Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino.

Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala.

Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,

ndimadziwika ndi dzina lanu.

17Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera,

sindinasangalale nawo anthu amenewo.

Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine

ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.

18Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha?

Bwanji chilonda changa sichikupola?

Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe,

kapena ngati kasupe wopanda madzi?”

19Tsono Yehova anandiyankha kuti,

“Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso

ndipo udzakhalanso mtumiki wanga.

Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe,

udzakhalanso mneneri wanga.

Anthu adzabwera kwa iwe

ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.

20Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba

ngati mkuwa kwa anthu awa.

Adzalimbana nawe

koma sadzakugonjetsa,

pakuti Ine ndili nawe

kukulanditsa ndi kukupulumutsa,”

akutero Yehova.

21“Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa

ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米书 15:1-21

犹大的厄运

1耶和华对我说:“就算摩西撒母耳站在我面前求情,我也不会怜悯这些百姓。你把他们从我面前赶走吧! 2如果他们问你,‘我们该去哪里,’你就告诉他们,耶和华这样说,

“‘该死的死,

该被杀的被杀,

该遭饥荒的遭饥荒,

该被掳的被掳。’

3“我要让他们遭受四种祸患——刀杀、狗撕、鸟啄、兽吞。这是耶和华说的。 4因为犹大希西迦的儿子玛拿西耶路撒冷的所作所为,我要使他们的遭遇令天下万国惊惧。

5耶路撒冷啊,谁会同情你?

谁会为你悲哀?

谁会驻足向你问安?

6你背弃我,远离我,

因此我要伸手攻击你,毁灭你,

不再怜悯你。

这是耶和华说的。

7我要在这片土地上的各城门口用簸箕簸散我的子民,

使他们丧掉儿女;

我要灭绝他们,

因为他们不思悔改。

8我要使他们的寡妇比海沙还多,

使毁灭者在午间突然夺取青年的性命,

以致母亲们陷入痛苦、惊恐中。

9生过七个孩子的母亲心力枯竭,奄奄一息。

她羞愧难当,

她的希望突然破灭,

犹如白昼突然变成黑夜。

我必使其余的人丧身在敌人刀下。

这是耶和华说的。”

耶利米诉苦

10母亲啊,我真不幸,因为你生了我这个跟全犹大争论、激辩的人。我没有向人借贷,也没有借贷给人,然而人人都咒骂我。 11耶和华说:“我必拯救你,我必使仇敌在灾祸、困难来临时哀求你。 12谁能折断来自北方之敌的铁拳铜臂呢? 13因为你们境内罪恶泛滥,我要使敌人任意抢掠你们的财宝, 14把你们掳到陌生的地方。我的怒火要烧灭你们。”

15耶和华啊,你知道我的遭遇。

求你顾念我,眷顾我,

报应迫害我的人。

求你不要取我的性命,

因为你不轻易发怒,

你知道我为了你忍受辱骂。

16万军之上帝耶和华啊,

我把你的话视为甘饴,

它们是我心中的快乐和喜悦,

因为我属于你的名下。

17我没有与作乐的人为伍,

没有与他们同乐。

你要我独坐一处,

他们的罪恶使我怒气填胸。

18为什么我的痛楚无休无止?

为什么我的创伤无法医治?

难道你要像一条时断时流的小溪让我无法依靠吗?

19耶和华对我说:

“如果你回心转意,

我就让你重新事奉我。

如果你说有益的话,

不说无益的话,

就可以做我的发言人,

百姓便会归向你,

但你不可受他们的影响。

20我要使你成为坚固的铜墙,

他们要攻击你,却不能胜过你,

因为我与你同在,我会保护你,

拯救你。

这是耶和华说的。

21我要把你从恶人手中救出,

从残暴之徒的权势下赎回。”