Yeremiya 15 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 15:1-21

1Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite! 2Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti,

“ ‘Oyenera kufa adzafa;

oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga;

oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala;

oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’

3“Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga. 4Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.

5“Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu?

Kodi adzakulira ndani?

Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?

6Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova.

“Inu mukubwererabe mʼmbuyo.

Choncho Ine ndidzakukanthani.

Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.

7Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo

monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero.

Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga

chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.

8Ndinachulukitsa amayi awo amasiye

kupambana mchenga wa kunyanja.

Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna

dzuwa lili pamutu.

Mwadzidzidzi ndinawagwetsera

kuwawa mtima ndi mantha.

9Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka

ndipo akupuma wefuwefu.

Dzuwa lake lalowa ukanali usana;

anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru.

Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo

kuti awaphe ndi lupanga,”

akutero Yehova.

10Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine,

munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse!

Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu,

komatu aliyense akunditemberera.

11Yehova anati,

“Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino.

Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka

ndi ya mavuto awo.

12“Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo,

makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.

13Anthu ako ndi chuma chako

ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro,

chifukwa cha machimo anu onse

a mʼdziko lanu lonse.

14Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu

mʼdziko limene inu simulidziwa,

chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto

umene udzakutenthani.”

15Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse;

kumbukireni ndi kundisamalira.

Ndilipsireni anthu ondizunza.

Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga.

Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.

16Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino.

Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala.

Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,

ndimadziwika ndi dzina lanu.

17Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera,

sindinasangalale nawo anthu amenewo.

Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine

ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.

18Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha?

Bwanji chilonda changa sichikupola?

Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe,

kapena ngati kasupe wopanda madzi?”

19Tsono Yehova anandiyankha kuti,

“Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso

ndipo udzakhalanso mtumiki wanga.

Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe,

udzakhalanso mneneri wanga.

Anthu adzabwera kwa iwe

ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.

20Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba

ngati mkuwa kwa anthu awa.

Adzalimbana nawe

koma sadzakugonjetsa,

pakuti Ine ndili nawe

kukulanditsa ndi kukupulumutsa,”

akutero Yehova.

21“Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa

ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иеремия 15:1-21

1И сказал мне Вечный:

– Даже если бы встали передо Мной Мусо и Самуил, Моё сердце не обратилось бы к этому народу. Гони его от Меня прочь, пусть уходит! 2А если станут спрашивать тебя эти люди: «Куда нам идти?» – то ответь им: «Так говорит Вечный:

Обречённые на смерть – пусть умирают;

обречённые на меч – пусть идут под меч;

обречённые на голод – пусть голодают;

обречённые на плен – пусть уходят в плен».

3– Я нашлю на них четыре вида казней, – возвещает Вечный, – меч, чтобы убивать; псов, чтобы терзать; и птиц небесных со зверями земными, чтобы пожирать и губить. 4Я сделаю их ужасом для всех царств на земле из-за того, что натворил в Иерусалиме иудейский царь Манасса, сын Езекии15:4 О правлении царя Манассы см. 4 Цар. 21:1-18; 2 Лет. 33:1-20..

5– Кто пожалеет тебя, Иерусалим?

Кто оплачет тебя?

Кто зайдёт, чтобы узнать о твоих делах?

6Ты отверг Меня, – возвещает Вечный, –

отступил назад.

Свою руку на тебя подниму

и погублю тебя;

Я устал жалеть.

7Я провею Мой народ вилами

во всех городах страны;

Я лишу его детей

и погублю Мой народ,

так как он не свернул с путей своих.

8Вдов у них станет больше,

чем песка в море.

В полдень Я наведу губителя

на матерей их юношей;

внезапно вселю в них

страх и смятение.

9Изнеможет мать семерых15:9 Семь – символ полноты, благополучия и безопасности.

и испустит дух.

Зайдёт её солнце во время дневное;

она будет унижена и опозорена.

А всех уцелевших предам мечу

на глазах их врагов, –

возвещает Вечный.

Жалоба Иеремии и ответ Вечного

10Горе мне, мать моя, что ты родила меня,

человека, что спорит и ссорится с целым светом!

Я не давал денег в рост и в долг не брал,

но всякий меня проклинает.

11Сказал Вечный:

– Я непременно дам свободу тебе во благо,

Я непременно заставлю врагов молить тебя

во время беды и во время скорби.

12Может ли кто-нибудь сломать железо,

железо с севера15:12 Считалось, что лучшее железо привозится с севера. Здесь говорится о том, что Иудее будет невозможно отразить северного врага, Вавилон., или бронзу?

13Ваши богатства и сокровища

Я отдам на разграбление,

отдам бесплатно за все ваши грехи,

совершённые по всей вашей стране.

14Я отдам вас в рабство вашим врагам,

в страну, что вам незнакома,

так как вспыхнул огонь Моего гнева –

он будет пылать против вас.

15Вечный, Ты всё знаешь;

вспомни меня, обрати на меня Свой взор!

Отомсти за меня гонителям.

Ты терпелив: не забирай меня;

Ты знаешь, что ради Тебя я терплю оскорбления.

16Твои слова были обращены ко мне, и я съел их;

Твои слова стали моей радостью

и весельем моему сердцу,

ведь Твоё имя надо мной провозглашено,

о Вечный, Бог Сил.

17Не сидел я в кругу насмешников

и не праздновал с ними;

я сидел одиноко под гнётом Твоей руки,

так как Ты наполнил меня гневом.

18Почему моя боль никак не уймётся,

почему моя рана тяжка и неисцелима?

Неужели будешь Ты для меня ручьём ненадёжным,

источником пересохшим?

19На это так говорит Вечный:

– Если покаешься, Я восставлю тебя

и сделаю тебя Своим рабом;

если будешь говорить важное, а не пустословить,

станешь Моими устами.

Пусть этот народ сам к тебе обращается,

а ты к ним не обращайся.

20Я сделаю тебя для них

укреплённой стеной из бронзы.

Они будут с тобой воевать,

но не одолеют,

потому что Я с тобой,

чтобы избавлять тебя и спасать, –

возвещает Вечный. –

21Я спасу тебя от рук нечестивых

и выкуплю из рук безжалостных.