Yeremiya 14 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 14:1-22

Chilala, Njala, Lupanga

1Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:

2“Yuda akulira,

mizinda yake ikuvutika;

anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni,

kulira kwa Yerusalemu kwakula.

3Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi.

Apita ku zitsime

osapezako madzi.

Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi.

Amanyazi ndi othedwa nzeru

adziphimba kumaso.

4Popeza pansi pawumiratu

chifukwa kulibe madzi,

alimi ali ndi manyazi

ndipo amphimba nkhope zawo.

5Ngakhale mbawala yayikazi

ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo

chifukwa kulibe msipu.

6Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu

nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe;

maso awo achita chidima

chifukwa chosowa msipu.”

7Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa,

koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu.

Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu;

ife takuchimwirani.

8Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani

ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso,

chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno?

Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?

9Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa,

kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa?

Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu,

ndipo tikudziwika ndi dzina lanu;

musatitaye ife!”

10Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi:

“Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri;

samatha kudziretsa.

Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire,

ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo

ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”

11Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino. 12Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”

13Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”

14Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo. 15Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala. 16Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.

17“Awuze mawu awa:

“ ‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza

usana ndi usiku;

chifukwa anthu anga okondedwa

apwetekeka kwambiri,

akanthidwa kwambiri.

18Ndikapita kuthengo,

ndikuona amene aphedwa ndi lupanga;

ndikapita mu mzinda,

ndikuona amene asakazidwa ndi njala.

Ngakhale aneneri pamodzi

ndi ansembe onse atengedwa.’ ”

19Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu?

Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni?

Chifukwa chiyani mwatikantha chotere

kuti sitingathenso kuchira?

Ife tinayembekezera mtendere

koma palibe chabwino chomwe chabwera,

tinayembekezera kuchira

koma panali kuopsezedwa kokhakokha.

20Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu

ndiponso kulakwa kwa makolo athu;

ndithu ife tinakuchimwiranidi.

21Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe;

musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero.

Kumbukirani pangano lanu ndi ife

ndipo musachiphwanye.

22Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina,

kodi pali mulungu amene angagwetse mvula?

Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu,

popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu

amene mukhoza kuchita zimenezi.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иеремия 14:1-22

Пророчества во время засухи

1Вот что Вечный сказал Иеремии о засухе:

2– Плачет Иудея,

томятся её врата;

люди скорбно сидят на земле,

и воплем исходит Иерусалим.

3Знать посылает своих слуг за водой;

те приходят к колодцам

и не находят воды.

Несут пустые кувшины домой;

смущённые, обескураженные,

они покрывают свои головы.

4Трескается земля в стране,

поражённой бездождьем,

и земледельцы в смущении

покрывают свои головы.

5Даже лань бросает в поле своего новорождённого детёныша,

потому что не осталось травы.

6Дикие ослы, стоя на голых кряжах,

глотают воздух, словно шакалы;

их глаза потускнели,

потому что погибла зелень.

7– Наши грехи обличают нас, Вечный,

но сделай что-нибудь ради Своего имени!

Тяжко наше отступничество,

мы согрешили перед Тобой.

8Надежда Исроила,

Спаситель во время скорби,

почему же Ты в этой стране как чужак,

словно путник, свернувший с дороги переночевать?

9Почему Ты как оробевший человек,

точно могучий воин, бессильный спасти?

Вечный, Ты среди нас,

Твоё имя над нами провозглашено,

не оставляй нас!

10Так говорит Вечный об этом народе:

– Поистине, любят они бродить

и своих ног не удерживают.

За это Вечный не благоволит к ним;

Он вспомнит их беззакония

и накажет их за грехи.

11Вечный сказал мне:

– Не молись о благополучии этого народа. 12Пусть постятся, но Я не услышу их вопля; пусть возносят всесожжения и хлебные приношения, но Я не приму их. Да, Я погублю их мечом, голодом и мором.

13И тогда сказал я:

– Владыка Вечный, пророки твердят им: «Не увидите меча, и голода не будет, но нерушимый мир подарю Я вам в этом крае».

14И Вечный сказал мне:

– Пророки предрекают ложь от Моего имени. Я не посылал их, не давал им повелений и не говорил с ними. Они пророчествуют вам ложные видения, пустую ворожбу и мечты собственных сердец. 15Поэтому так говорю Я, Вечный, о тех, кто пророчествует от Моего имени: Я не посылал их, но они говорят: «Ни меча, ни голода не будет в этой стране». Эти самые пророки падут от меча и голода. 16А народ, которому они пророчествуют, будет размётан по улицам Иерусалима голодом и мечом, и некому будет хоронить ни их самих, ни их жён, ни их сыновей, ни дочерей. Я обрушу на них беду, которую они заслужили.

17Вот что скажи им:

– Пусть льются из моих глаз слёзы,

не переставая ни днём, ни ночью,

потому что девственная дочь – народ мой –

получила страшную рану,

сражена могучим ударом.

18В поле ли выйду –

там погибшие от меча,

войду ли в город –

там умирающие от голода.

И пророк, и священнослужитель бродят по земле,

не зная, что делают14:18 Или: «идут в землю, которую не знают»..

19Разве навек Ты отверг Иудею?

Разве опротивел Тебе Иерусалим?14:19 Букв.: «Сион».

Зачем Ты поразил нас так,

что нет для нас исцеления?

Ждём мы мира,

а ничего доброго нет;

ждём времени исцеления,

а вместо этого – ужасы.

20О Вечный, мы признаём нашу неправедность

и вину наших отцов;

мы согрешили перед Тобой.

21Не отвергай нас ради Своего имени;

не унижай престол Своей славы.

Вспомни и не расторгай

Своё соглашение с нами.

22Могут ли ничтожные идолы народов ниспослать дождь?

Может ли небо само пролиться ливнем?

Разве не от Тебя это, Вечный, Бог наш?

Мы надеемся лишь на Тебя,

так как Ты всё это творишь.