Yeremiya 13 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 13:1-27

Lamba Womanga Mʼchiwuno

1Yehova anandiwuza kuti, “Pita kagule lamba wansalu yosalala ndipo ukavale mʼchiwuno mwako, koma usakamuviyike mʼmadzi.” 2Choncho ndinakagula lambayo, monga momwe anandiwuzira Yehova, ndipo ndinamanga mʼchiwuno mwanga.

3Kenaka Yehova anandiyankhulanso kachiwiri kuti, 4“Tenga lamba amene unagula ndi kuvala mʼchiwuno mwako uja. Tsono pita ku mtsinje wa Yufurate ndipo ukamubise lambayo mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.” 5Ndipo ndinapitadi ndi kukabisa lambayo ku Yufurate, monga anenera Yehova.

6Patapita masiku ambiri Yehova anandiwuzanso kuti, “Pitanso ku Yufurate ndipo ukatenge lamba amene ndinakuwuza kuti ukamubise kumeneko.” 7Choncho ndinapita ku Yufurate kukafukula lambayo ndi kumuchotsa pamalo pamene ndinamubisa, koma nthawi imeneyi nʼkuti lambayo atawonongeka kotheratu ndipo analibenso ntchito.

8Pamenepo Yehova anandiwuza kuti, 9“Izi ndi zimene ine ndikunena: ‘Umu ndi mmene ndidzawonongere zimene akunyadira kwambiri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. 10Anthuwa ndi oyipa. Iwo akana kumvera mawu anga. Mʼmalo mwake amawumirira kutsata milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Anthu amenewa adzakhala ngati lamba wopanda ntchitoyu. 11Monga momwe lamba amakanirira mʼchiwuno cha munthu, momwemonso ndinakonza kuti nyumba yonse ya Israeli ndi nyumba yonse ya Yuda indikangamire Ine kuti akhale anthu anga, kuti azitamanda dzina langa ndi kulemekeza Ine. Koma iwo sanamvere,’ akutero Yehova.

Zikopa Zothiramo Vinyo

12“Awuze anthuwo kuti, ‘Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Mtsuko uliwonse adzawudzaza ndi vinyo.’ Ndipo ngati iwo anena kwa iwe kuti, ‘Kodi ngati ife sitikudziwa kuti mtsuko uliwonse udzadzazidwa ndi vinyo?’ 13Tsono iwe uwawuze kuti, Yehova akuti ‘Ine ndidzaledzeretsa anthu onse okhala mʼdziko muno, kuyambira mafumu amene amakhala pa mpando waufumu wa Davide, ansembe, aneneri, pamodzi ndi anthu onse amene akukhala mu Yerusalemu. 14Ndidzawagundanitsa mitu kuti aphwanyane okhaokha ngati mitsuko, makolo ndi ana awo, akutero Yehova. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwachitira chifundo kapena kukhudzidwa nawo kuti ndileke kuwawononga.’ ”

Yuda Adzapita ku Ukapolo

15Imvani inu Aisraeli ndipo tcherani khutu,

musadzitukumule,

pakuti ndi Yehova amene akuyankhula.

16Lemekezani Yehova Mulungu wanu

asanagwetse mdima,

mapazi anu asanayambe kupunthwa

mʼchisisira chamʼmapiri.

Asanasandutse kuwala

mukuyembekezerako kukhala

mdima wandiweyani.

17Koma ngati simumvera,

ndidzalira kwambiri

chifukwa cha kunyada kwanu.

Mʼmaso mwanga

mwadzaza ndi misozi yowawa

chifukwa nkhosa za Yehova zatengedwa ukapolo.

18Uza mfumu pamodzi ndi amayi ake kuti,

“Tsikani pa mipando yaufumuyo,

pakuti zipewa zanu zaufumu zokongolazo

zagwa pansi.”

19Mizinda ya ku Negevi yatsekedwa

ndipo palibe wina woti nʼkuyitsekula.

Yuda yense watengedwa kupita ku ukapolo,

watengedwa yense ukapolo.

20Tukula maso ako kuti uwone

amene akubwera kuchokera kumpoto.

Kodi nkhosa zimene anakusungitsa zili kuti,

nkhosa zanu zokongola zija?

21Kodi udzanena chiyani pamene [Yehova] adzakuyikira

anthu amene unkanena kuti ndi abale ako akukugonjetsa ndi kukulamulira?

Kodi sudzamva zowawa

ngati za mayi pa nthawi yake yochira?

22Ndipo ngati udzadzifunsa kuti,

“Kodi zimenezi zandichitikira chifukwa chiyani?”

Ndi chifukwa cha machimo anu ambiri

kuti zovala zanu zingʼambike

ndiponso kuti akuchitireni nkhanza.

23Kodi wa dziko la Kusi nʼkusintha khungu lake,

kapena kambuku kusintha mawanga ake?

Inunso amene munazolowera kuchita

zoyipa simungathe kusintha.

24“Ine ndidzakumwazani ngati mankhusu

amene amawuluka ndi mphepo ya ku chipululu.

25Limeneli ndiye gawo lanu,

chilango chimene ndakukonzerani

chifukwa chondiyiwala Ine

ndi kutumikira milungu yabodza,

akutero Yehova.

26Ine ndidzakwinya zovala zanu mpaka ku maso

kuti umaliseche wanu uwonekere.

27Ndaona zonyansa zanu: zigololo zanu, kutchetcherera kwanu

ndi ziwerewere zanu,

zochitika pa mapiri ndi mʼminda.

Tsoka iwe Yerusalemu!

Udzakhala wosayeretsedwa

pa zachipembedzo mpaka liti?”

King James Version

Jeremiah 13:1-27

1Thus saith the LORD unto me, Go and get thee a linen girdle, and put it upon thy loins, and put it not in water. 2So I got a girdle according to the word of the LORD, and put it on my loins. 3And the word of the LORD came unto me the second time, saying, 4Take the girdle that thou hast got, which is upon thy loins, and arise, go to Euphrates, and hide it there in a hole of the rock. 5So I went, and hid it by Euphrates, as the LORD commanded me. 6And it came to pass after many days, that the LORD said unto me, Arise, go to Euphrates, and take the girdle from thence, which I commanded thee to hide there. 7Then I went to Euphrates, and digged, and took the girdle from the place where I had hid it: and, behold, the girdle was marred, it was profitable for nothing. 8Then the word of the LORD came unto me, saying, 9Thus saith the LORD, After this manner will I mar the pride of Judah, and the great pride of Jerusalem. 10This evil people, which refuse to hear my words, which walk in the imagination of their heart, and walk after other gods, to serve them, and to worship them, shall even be as this girdle, which is good for nothing.13.10 imagination: or, stubbornness 11For as the girdle cleaveth to the loins of a man, so have I caused to cleave unto me the whole house of Israel and the whole house of Judah, saith the LORD; that they might be unto me for a people, and for a name, and for a praise, and for a glory: but they would not hear.

12¶ Therefore thou shalt speak unto them this word; Thus saith the LORD God of Israel, Every bottle shall be filled with wine: and they shall say unto thee, Do we not certainly know that every bottle shall be filled with wine? 13Then shalt thou say unto them, Thus saith the LORD, Behold, I will fill all the inhabitants of this land, even the kings that sit upon David’s throne, and the priests, and the prophets, and all the inhabitants of Jerusalem, with drunkenness. 14And I will dash them one against another, even the fathers and the sons together, saith the LORD: I will not pity, nor spare, nor have mercy, but destroy them.13.14 one…: Heb. a man against his brother13.14 but…: Heb. from destroying them

15¶ Hear ye, and give ear; be not proud: for the LORD hath spoken. 16Give glory to the LORD your God, before he cause darkness, and before your feet stumble upon the dark mountains, and, while ye look for light, he turn it into the shadow of death, and make it gross darkness. 17But if ye will not hear it, my soul shall weep in secret places for your pride; and mine eye shall weep sore, and run down with tears, because the LORD’s flock is carried away captive. 18Say unto the king and to the queen, Humble yourselves, sit down: for your principalities shall come down, even the crown of your glory.13.18 principalities: or, head tires 19The cities of the south shall be shut up, and none shall open them: Judah shall be carried away captive all of it, it shall be wholly carried away captive. 20Lift up your eyes, and behold them that come from the north: where is the flock that was given thee, thy beautiful flock? 21What wilt thou say when he shall punish thee? for thou hast taught them to be captains, and as chief over thee: shall not sorrows take thee, as a woman in travail?13.21 punish: Heb visit upon

22¶ And if thou say in thine heart, Wherefore come these things upon me? For the greatness of thine iniquity are thy skirts discovered, and thy heels made bare.13.22 made…: or, shall be violently taken away 23Can the Ethiopian change his skin, or the leopard his spots? then may ye also do good, that are accustomed to do evil.13.23 accustomed: Heb. taught 24Therefore will I scatter them as the stubble that passeth away by the wind of the wilderness. 25This is thy lot, the portion of thy measures from me, saith the LORD; because thou hast forgotten me, and trusted in falsehood. 26Therefore will I discover thy skirts upon thy face, that thy shame may appear. 27I have seen thine adulteries, and thy neighings, the lewdness of thy whoredom, and thine abominations on the hills in the fields. Woe unto thee, O Jerusalem! wilt thou not be made clean? when shall it once be?13.27 when…: Heb. after when yet?