Yeremiya 13 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 13:1-27

Lamba Womanga Mʼchiwuno

1Yehova anandiwuza kuti, “Pita kagule lamba wansalu yosalala ndipo ukavale mʼchiwuno mwako, koma usakamuviyike mʼmadzi.” 2Choncho ndinakagula lambayo, monga momwe anandiwuzira Yehova, ndipo ndinamanga mʼchiwuno mwanga.

3Kenaka Yehova anandiyankhulanso kachiwiri kuti, 4“Tenga lamba amene unagula ndi kuvala mʼchiwuno mwako uja. Tsono pita ku mtsinje wa Yufurate ndipo ukamubise lambayo mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.” 5Ndipo ndinapitadi ndi kukabisa lambayo ku Yufurate, monga anenera Yehova.

6Patapita masiku ambiri Yehova anandiwuzanso kuti, “Pitanso ku Yufurate ndipo ukatenge lamba amene ndinakuwuza kuti ukamubise kumeneko.” 7Choncho ndinapita ku Yufurate kukafukula lambayo ndi kumuchotsa pamalo pamene ndinamubisa, koma nthawi imeneyi nʼkuti lambayo atawonongeka kotheratu ndipo analibenso ntchito.

8Pamenepo Yehova anandiwuza kuti, 9“Izi ndi zimene ine ndikunena: ‘Umu ndi mmene ndidzawonongere zimene akunyadira kwambiri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. 10Anthuwa ndi oyipa. Iwo akana kumvera mawu anga. Mʼmalo mwake amawumirira kutsata milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Anthu amenewa adzakhala ngati lamba wopanda ntchitoyu. 11Monga momwe lamba amakanirira mʼchiwuno cha munthu, momwemonso ndinakonza kuti nyumba yonse ya Israeli ndi nyumba yonse ya Yuda indikangamire Ine kuti akhale anthu anga, kuti azitamanda dzina langa ndi kulemekeza Ine. Koma iwo sanamvere,’ akutero Yehova.

Zikopa Zothiramo Vinyo

12“Awuze anthuwo kuti, ‘Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Mtsuko uliwonse adzawudzaza ndi vinyo.’ Ndipo ngati iwo anena kwa iwe kuti, ‘Kodi ngati ife sitikudziwa kuti mtsuko uliwonse udzadzazidwa ndi vinyo?’ 13Tsono iwe uwawuze kuti, Yehova akuti ‘Ine ndidzaledzeretsa anthu onse okhala mʼdziko muno, kuyambira mafumu amene amakhala pa mpando waufumu wa Davide, ansembe, aneneri, pamodzi ndi anthu onse amene akukhala mu Yerusalemu. 14Ndidzawagundanitsa mitu kuti aphwanyane okhaokha ngati mitsuko, makolo ndi ana awo, akutero Yehova. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwachitira chifundo kapena kukhudzidwa nawo kuti ndileke kuwawononga.’ ”

Yuda Adzapita ku Ukapolo

15Imvani inu Aisraeli ndipo tcherani khutu,

musadzitukumule,

pakuti ndi Yehova amene akuyankhula.

16Lemekezani Yehova Mulungu wanu

asanagwetse mdima,

mapazi anu asanayambe kupunthwa

mʼchisisira chamʼmapiri.

Asanasandutse kuwala

mukuyembekezerako kukhala

mdima wandiweyani.

17Koma ngati simumvera,

ndidzalira kwambiri

chifukwa cha kunyada kwanu.

Mʼmaso mwanga

mwadzaza ndi misozi yowawa

chifukwa nkhosa za Yehova zatengedwa ukapolo.

18Uza mfumu pamodzi ndi amayi ake kuti,

“Tsikani pa mipando yaufumuyo,

pakuti zipewa zanu zaufumu zokongolazo

zagwa pansi.”

19Mizinda ya ku Negevi yatsekedwa

ndipo palibe wina woti nʼkuyitsekula.

Yuda yense watengedwa kupita ku ukapolo,

watengedwa yense ukapolo.

20Tukula maso ako kuti uwone

amene akubwera kuchokera kumpoto.

Kodi nkhosa zimene anakusungitsa zili kuti,

nkhosa zanu zokongola zija?

21Kodi udzanena chiyani pamene [Yehova] adzakuyikira

anthu amene unkanena kuti ndi abale ako akukugonjetsa ndi kukulamulira?

Kodi sudzamva zowawa

ngati za mayi pa nthawi yake yochira?

22Ndipo ngati udzadzifunsa kuti,

“Kodi zimenezi zandichitikira chifukwa chiyani?”

Ndi chifukwa cha machimo anu ambiri

kuti zovala zanu zingʼambike

ndiponso kuti akuchitireni nkhanza.

23Kodi wa dziko la Kusi nʼkusintha khungu lake,

kapena kambuku kusintha mawanga ake?

Inunso amene munazolowera kuchita

zoyipa simungathe kusintha.

24“Ine ndidzakumwazani ngati mankhusu

amene amawuluka ndi mphepo ya ku chipululu.

25Limeneli ndiye gawo lanu,

chilango chimene ndakukonzerani

chifukwa chondiyiwala Ine

ndi kutumikira milungu yabodza,

akutero Yehova.

26Ine ndidzakwinya zovala zanu mpaka ku maso

kuti umaliseche wanu uwonekere.

27Ndaona zonyansa zanu: zigololo zanu, kutchetcherera kwanu

ndi ziwerewere zanu,

zochitika pa mapiri ndi mʼminda.

Tsoka iwe Yerusalemu!

Udzakhala wosayeretsedwa

pa zachipembedzo mpaka liti?”

Hoffnung für Alle

Jeremia 13:1-27

Das Maß der Sünden Judas ist voll

(Kapitel 13–20)

Der verrottete Gürtel

1Der Herr sprach zu mir: »Kauf dir einen Gürtel aus Leinen, binde ihn dir um und sorg dafür, dass er nicht nass wird!« 2Ich kaufte einen Gürtel und legte ihn an, so wie der Herr es mir befohlen hatte. 3Dann gab er mir noch einen Auftrag: 4»Geh mit deinem neuen Gürtel an den Euphrat13,4 Oder: nach Para (ein Ort in der Nähe von Jeremias Heimatstadt Anatot). und versteck ihn dort in einer Felsspalte!« 5Wieder tat ich, was der Herr mir gesagt hatte, ging zum Euphrat und versteckte den Gürtel dort. 6Nach langer Zeit sprach der Herr zu mir: »Geh zurück an den Euphrat und hol den Gürtel, den du auf meinen Befehl dort versteckt hast!« 7Da wanderte ich wieder zum Euphrat und holte den Gürtel aus seinem Versteck hervor. Doch er war verrottet und zu nichts mehr zu gebrauchen.

8Der Herr sprach zu mir: 9»Genauso werde ich den Hochmut der Bewohner von Jerusalem und ganz Juda zunichtemachen. 10Sie sind ein boshaftes Volk, das sich weigert, auf mich zu hören, und tut, wozu sein Eigensinn es treibt. Anderen Göttern laufen sie nach, dienen ihnen und beten sie an – darum werden sie diesem Gürtel gleichen, der zu nichts mehr zu gebrauchen ist! 11Wie sich ein Mann seinen Gürtel um die Hüften bindet, so wollte ich, der Herr, mich mit Israel und Juda verbinden. Mein Volk sollten sie sein, meinen Namen bekannt machen, mir Lob und Ehre bringen – doch sie haben mir nicht gehorcht!«

Die Weinkrüge sind voll

12»Sag ihnen: ›So spricht der Herr, der Gott Israels: Weinkrüge sind dazu da, dass man sie füllt.‹ Wenn sie dir entgegnen: ›Das weiß doch jeder, dass Weinkrüge voll sein müssen!‹, 13dann antworte: ›Der Herr kündigt euch an: Die Bewohner dieses Landes, die Könige, die als Nachkommen von David regieren, die Priester und Propheten, ja, alle Einwohner von Jerusalem – sie sind die Krüge, und ich werde sie mit Wein füllen, bis sie betrunken sind! 14Und dann schlage ich sie gegeneinander, so dass einer am anderen zerbricht, die Väter und die Söhne. Ich werde kein Mitleid mit ihnen haben und sie nicht schonen, sondern sie erbarmungslos zerschmettern. Darauf gebe ich, der Herr, mein Wort.‹«

Nehmt Gottes Warnung ernst!

15Der Herr hat zu euch gesprochen, darum seid nicht überheblich, sondern hört genau zu und nehmt es euch zu Herzen! 16Ehrt den Herrn, euren Gott, bevor er die Nacht hereinbrechen lässt und ihr in der Dämmerung auf den Hügeln umherstolpert, ehe er das Licht, auf das ihr wartet, in tiefe Nacht und hoffnungslose Dunkelheit verwandelt. 17Doch wenn ihr seine Warnungen in den Wind schlagt, werde ich heimlich über euren Hochmut weinen; dann kann ich meine Tränen nicht mehr zurückhalten, weil Gottes Volk, seine Herde, in die Gefangenschaft getrieben wird.

Eine Botschaft für König Jojachin

18Der Herr sagt: »Richtet dem König und seiner Mutter aus: Steigt herab vom Thron und setzt euch auf den Boden, denn die Zeit eurer glanzvollen Herrschaft ist vorbei! 19Die Städte im Süden von Juda werden belagert, und niemand kann zu ihnen durchkommen. Ganz Juda wird in die Gefangenschaft verschleppt.«

Jerusalem wird geschändet

20»Jerusalem, siehst du, wie deine Feinde von Norden her kommen? Was soll nun aus deiner Herde werden, die du beschützen solltest und auf die du so stolz warst? 21Was wirst du sagen, wenn ich die als Herren über dich einsetze, die du für deine Freunde hieltest? Schmerzen werden dich überfallen wie die Wehen eine schwangere Frau. 22Und wenn du dich dann fragst: ›Warum trifft mich dieses Unheil?‹, dann sollst du wissen: Wegen deiner unzähligen Sünden reißt man dir jetzt dein Kleid hoch und tut dir Gewalt an.

23Sag mir: Kann ein dunkelhäutiger Mensch etwa seine Hautfarbe wechseln oder ein Leopard sein geflecktes Fell? Genauso wenig kannst du Gutes tun, die du ans Böse gewöhnt bist! 24Zerstreuen werde ich deine Einwohner wie Spreu im Wüstenwind!

25Dieses Los erwartet dich, das ist der gerechte Lohn, den ich dir gebe, weil du mich vergessen und falschen Göttern geglaubt hast. Darauf gebe ich, der Herr, mein Wort! 26Wegen deiner Untreue werde auch ich dir jetzt das Kleid hochreißen, hoch bis über dein Gesicht, damit alle dich nackt sehen. 27Dein ständiges Ehebrechen, dein aufreizendes Lachen und deine schamlose Hurerei: Das alles ist mir nicht entgangen! Auf den Hügeln und Feldern hast du abscheuliche Götzen verehrt. Wehe dir, Jerusalem! Wie lange soll das noch so weitergehen? Willst du denn nie wieder rein werden?«