Yeremiya 12 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 12:1-17

Madandawulo a Yeremiya

1Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse

ndikati nditsutsane nanu.

Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga.

Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino?

Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?

2Inu munawadzala ndipo anamera mizu;

amakula ndi kubereka zipatso.

Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse,

koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.

3Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa;

mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga.

Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa!

Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!

4Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti

ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti?

Nyama ndi mbalame kulibiretu

chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa.

Iwo amati:

“Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”

Yankho la Mulungu

5Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu

nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo?

Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino,

udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango

za ku Yorodani?

6Ngakhale abale ako

ndi anansi akuwukira,

onsewo amvana zokuyimba mlandu.

Usawakhulupirire,

ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.

7“Ine ndawasiya anthu anga;

anthu amene ndinawasankha ndawataya.

Ndapereka okondedwa anga

mʼmanja mwa adani awo.

8Anthu amene ndinawasankha

asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango.

Akundibangulira mwaukali;

nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.

9Anthu anga amene ndinawasankha

asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga

imene akabawi ayizinga.

Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo.

Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.

10Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa,

anapondereza munda wanga;

munda wanga wabwino uja

anawusandutsa chipululu.

11Unawusandutsadi chipululu.

Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine.

Dziko lonse lasanduka chipululu

chifukwa palibe wolisamalira.

12Anthu onse owononga abalalikira

ku zitunda zonse za mʼchipululu.

Yehova watuma ankhondo ake

kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko,

ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.

13Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga;

anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse.

Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu

chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”

14“Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo. 15Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake. 16Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga. 17Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.

Nova Versão Internacional

Jeremias 12:1-17

A Queixa de Jeremias

1Tu és justo, Senhor,

quando apresento uma causa diante de ti.

Contudo, eu gostaria de discutir contigo sobre a tua justiça.

Por que o caminho dos ímpios prospera?

Por que todos os traidores vivem sem problemas?

2Tu os plantaste, e eles criaram raízes;

crescem e dão fruto.

Tu estás sempre perto dos seus lábios,

mas longe dos seus corações.

3Tu, porém, me conheces, Senhor;

tu me vês e provas a minha atitude para contigo.

Arranca os ímpios como a ovelhas destinadas ao matadouro!

Reserva-os para o dia da matança!

4Até quando a terra ficará de luto12.4 Ou a terra pranteará

e a relva de todo o campo estará seca?

Perecem os animais e as aves por causa da maldade

dos que habitam nesta terra,

pois eles disseram:

“Ele não verá o fim que nos espera”.

A Resposta de Deus

5“Se você correu com homens

e eles o cansaram,

como poderá competir com cavalos?

Se você tropeça12.5 Ou você se sente seguro em terreno seguro,12.5 Ou Se você põe a confiança numa terra segura,

o que fará nos matagais junto ao Jordão?12.5 Ou fará quando o Jordão inundar?

6Até mesmo os seus irmãos

e a sua própria família traíram você

e o perseguem aos gritos.

Não confie neles,

mesmo quando dizem coisas boas.

7“Abandonei a minha família,

deixei a minha propriedade

e entreguei aquela a quem amo

nas mãos dos seus inimigos.

8O povo de minha propriedade tornou-se para mim

como um leão na floresta.

Ele ruge contra mim,

por isso eu o detesto.

9O povo de minha propriedade tornou-se para mim

como uma toca de hiena,

sobre a qual pairam as aves de rapina.

Reúnam todos os animais selvagens;

tragam-nos para o banquete.

10A minha vinha foi destruída por muitos pastores,

que pisotearam a minha propriedade.

Eles tornaram a minha preciosa propriedade

num deserto devastado.

11Fizeram dela uma terra devastada;

e devastada ela pranteia diante de mim.

A terra toda foi devastada,

mas não há quem se importe com isso.

12Destruidores vieram sobre todas as planícies do deserto,

pois a espada do Senhor devora esta terra

de uma extremidade à outra; ninguém está seguro.

13Semearam trigo, mas colheram espinhos;

cansaram-se de trabalhar para nada produzir.

Estão desapontados com a colheita

por causa do fogo da ira do Senhor.”

14Assim diz o Senhor a respeito de todos os meus vizinhos, as nações ímpias que se apoderam da herança que dei a Israel, o meu povo: “Eu os arrancarei da sua terra, e arrancarei Judá do meio deles. 15Mas, depois de arrancá-los, terei compaixão de novo e os farei voltar, cada um à sua propriedade e à sua terra. 16E, se aprenderem a comportar-se como o meu povo, e jurarem pelo nome do Senhor, dizendo: ‘Juro pelo nome do Senhor’—como antes ensinaram o meu povo a jurar por Baal—, então eles serão estabelecidos no meio do meu povo. 17Mas, se não me ouvirem, eu arrancarei completamente aquela nação e a destruirei”, declara o Senhor.