Yakobo 5 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yakobo 5:1-20

Chenjezo kwa Achuma Opondereza Anzawo

1Tsono tamverani, inu anthu achuma, lirani ndi kufuwula chifukwa cha zovuta zimene zidzakugwereni. 2Chuma chanu chawola ndipo njenjete zadya zovala zanu. 3Golide ndi siliva wanu zachita dzimbiri. Dzimbirilo lidzakhala umboni wokutsutsani ndi kuwononga mnofu wanu ngati moto. Mwadziwunjikira chuma pa masiku ano otsiriza. 4Taonani, ndalama za malipiro zimene munakanika kulipira aganyu aja ankasenga mʼmunda mwanu zikulira mokutsutsani. Kulira kwa okololawo kwamveka mʼmakutu mwa Ambuye Wamphamvuzonse. 5Mwakhala pa dziko lapansi pano moyo ofewa ndipo mwalidyera dziko lapansi. Mwadzinenepetsa pa tsiku lokaphedwa. 6Mwaweruza kuti ndi wolakwa ndipo mwapha munthu wosalakwa, amene sakutsutsana nanu.

Kupirira Mʼmasautso

7Tsono abale, pirirani mpaka kubwera kwa Ambuye. Onani mmene amachitira mlimi. Amadikirira kuti zipatso zabwino zioneke mʼmunda mwake. Amayembekezera mokhazikika mtima kuyambira nthawi ya mvula yoyamba mpaka yotsiriza. 8Inunso mukhale owugwira mtima ndi osasinthika chifukwa Ambuye ali pafupi kubwera. 9Abale, musamanenezane zoyipa kuopa kuti mungadzaweruzidwe. Woweruza ali pa khomo!

10Abale, tengerani chitsanzo cha aneneri amene anayankhula mʼdzina la Ambuye. Iwowo anakumana ndi zovuta koma anapirira. 11Monga mukudziwa, tinawatenga ngati odalitsika anthu amene anapirira. Munamva za kupirira kwa Yobu ndipo mwaona zimene Ambuye anamuchitira potsiriza pake. Ambuye ndi wodzaza ndi chisoni ndi chifundo.

12Koposa zonse, abale anga, musamalumbire. Polumbira osamatchula kumwamba kapena dziko lapansi, kapena china chilichonse. “Inde” wanu azikhala “Inde,” ndipo “Ayi” wanu azikhala “Ayi,” kuopa kuti mungadzapezeke olakwa.

Pemphero la Chikhulupiriro

13Kodi alipo wina mwa inu amene ali pa mavuto? Apemphere. Kodi wina wakondwa? Ayimbe nyimbo zolemekeza. 14Kodi alipo wina mwa inu akudwala? Ayitane akulu ampingo kuti adzamupempherere ndi kumudzoza mafuta mʼdzina la Ambuye. 15Ndipo pemphero lachikhulupiriro lidzachiritsa munthu wodwalayo ndipo Ambuye adzamuutsa. Ngati wachimwa adzakhululukidwa. 16Choncho, ululiranani machimo anu ndi kupemphererana wina ndi mnzake kuti muchiritsidwe. Pemphero la munthu wolungama ndi lamphamvu ndipo limagwira ntchito.

17Eliya anali munthu ngati ife. Iye anapemphera mwamphamvu kuti mvula isagwe ndipo sinagwedi kwa zaka zitatu ndi theka. 18Kenaka anapempheranso, ndipo kumwamba kunagwetsa mvula, ndipo dziko lapansi linatulutsa zomera zake. 19Abale anga, ngati mmodzi wa inu apatuka pa choonadi ndipo wina wake ndi kumubweza, 20kumbukirani izi: Aliyense wobweza wochimwa kuchoka ku cholakwa chake, adzamupulumutsa ku imfa ndi kukwirira machimo ambiri.

Slovo na cestu

Jakubův 5:1-20

Varování bohatým vykořisťovatelům

1Vy, boháči, už teď plačte a naříkejte nad tím, co vás čeká. 2-3Nahromadili jste tolik potravin, že vám hnijí, vaše šatstvo žerou moli a vaše peníze ztrácejí na ceně.

Chtěli jste si nashromáždit poklady, a zatím jste si navršili hranici, která při posledním soudu shoří i s vámi. 4Mzda, o kterou jste ošidili dělníky najaté ke sklizni vašich polí, svědčí proti vám a nářek ženců dolehl k Božímu sluchu. 5Váš život strávený v radovánkách a hýření se podobá vykrmování zvířat na porážku. 6Odsoudili jste a zabili nevinného, který se nebránil.

Trpělivost v utrpení

7Bratři, čekejte trpělivě až přijde Pán. Vezměte si příklad z rolníka, který vytrvale čeká na vytouženou sklizeň, až uzraje po podzimních a jarních deštích. 8Nedejte se zviklat a mějte jistotu v srdci, vždyť příchod Páně se blíží.

9Bratři, nestěžujte si jeden na druhého, vždyť sami nejste lepší než ti, které odsuzujete. Nezapomeňte, že velký Soudce je již přede dveřmi a bude soudit i vás.

10Za příklad trpělivosti si vezměte proroky, kteří trpěli proto, že vyřizovali Boží poselství. 11Vážíme si těch, kteří vydrželi. Slyšeli jste o Jobově trpělivosti a vzpomeňte si, jak Bůh nakonec jeho utrpení obrátil k dobrému. Vidíte, jak je Pán plný soucitu a slitování.

12Nehřešte tím, že si berete Boha za svědka svých řečí. Buďte tak pravdomluvní, aby každý mohl věřit vašemu prostému ano nebo ne.

Modlitba víry

13Prožívá někdo z vás těžkosti? Ať se modlí! Daří se někomu z vás dobře? Ať zpěvem chválí Boha! 14Sužuje-li někoho nemoc, ať pozve starší sboru, aby se za něho modlili a potírali ho olejem ve jménu Páně. 15Modlitba spojená s opravdovou vírou uzdraví nemocného, Pán ho povzbudí, a tíží-li ho svědomí, odpustí mu hříchy.

16Vyznávejte si vzájemně své hříchy a modlete se jedni za druhé, abyste mohli být uzdraveni. Opravdová modlitba upřímně věřícího má velkou moc. 17Vzpomínáte si na Elijáše? Byl to člověk stejně křehký jako my, ale když se opravdově modlil, aby nepršelo, jeho modlitba byla vyslyšena – nesprchlo tři a půl roku. 18Potom se modlil znovu a tentokrát prosil za déšť. Také tato modlitba byla vyslyšena a země se po dešti opět zazelenala a dala úrodu.

19Moji bratři, jestliže někdo zabloudí od pravdy a druhý ho přivede zpět, 20zachrání jeho duši před zahynutím a pomůže mu získat plné odpuštění.