Yakobo 5 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yakobo 5:1-20

Chenjezo kwa Achuma Opondereza Anzawo

1Tsono tamverani, inu anthu achuma, lirani ndi kufuwula chifukwa cha zovuta zimene zidzakugwereni. 2Chuma chanu chawola ndipo njenjete zadya zovala zanu. 3Golide ndi siliva wanu zachita dzimbiri. Dzimbirilo lidzakhala umboni wokutsutsani ndi kuwononga mnofu wanu ngati moto. Mwadziwunjikira chuma pa masiku ano otsiriza. 4Taonani, ndalama za malipiro zimene munakanika kulipira aganyu aja ankasenga mʼmunda mwanu zikulira mokutsutsani. Kulira kwa okololawo kwamveka mʼmakutu mwa Ambuye Wamphamvuzonse. 5Mwakhala pa dziko lapansi pano moyo ofewa ndipo mwalidyera dziko lapansi. Mwadzinenepetsa pa tsiku lokaphedwa. 6Mwaweruza kuti ndi wolakwa ndipo mwapha munthu wosalakwa, amene sakutsutsana nanu.

Kupirira Mʼmasautso

7Tsono abale, pirirani mpaka kubwera kwa Ambuye. Onani mmene amachitira mlimi. Amadikirira kuti zipatso zabwino zioneke mʼmunda mwake. Amayembekezera mokhazikika mtima kuyambira nthawi ya mvula yoyamba mpaka yotsiriza. 8Inunso mukhale owugwira mtima ndi osasinthika chifukwa Ambuye ali pafupi kubwera. 9Abale, musamanenezane zoyipa kuopa kuti mungadzaweruzidwe. Woweruza ali pa khomo!

10Abale, tengerani chitsanzo cha aneneri amene anayankhula mʼdzina la Ambuye. Iwowo anakumana ndi zovuta koma anapirira. 11Monga mukudziwa, tinawatenga ngati odalitsika anthu amene anapirira. Munamva za kupirira kwa Yobu ndipo mwaona zimene Ambuye anamuchitira potsiriza pake. Ambuye ndi wodzaza ndi chisoni ndi chifundo.

12Koposa zonse, abale anga, musamalumbire. Polumbira osamatchula kumwamba kapena dziko lapansi, kapena china chilichonse. “Inde” wanu azikhala “Inde,” ndipo “Ayi” wanu azikhala “Ayi,” kuopa kuti mungadzapezeke olakwa.

Pemphero la Chikhulupiriro

13Kodi alipo wina mwa inu amene ali pa mavuto? Apemphere. Kodi wina wakondwa? Ayimbe nyimbo zolemekeza. 14Kodi alipo wina mwa inu akudwala? Ayitane akulu ampingo kuti adzamupempherere ndi kumudzoza mafuta mʼdzina la Ambuye. 15Ndipo pemphero lachikhulupiriro lidzachiritsa munthu wodwalayo ndipo Ambuye adzamuutsa. Ngati wachimwa adzakhululukidwa. 16Choncho, ululiranani machimo anu ndi kupemphererana wina ndi mnzake kuti muchiritsidwe. Pemphero la munthu wolungama ndi lamphamvu ndipo limagwira ntchito.

17Eliya anali munthu ngati ife. Iye anapemphera mwamphamvu kuti mvula isagwe ndipo sinagwedi kwa zaka zitatu ndi theka. 18Kenaka anapempheranso, ndipo kumwamba kunagwetsa mvula, ndipo dziko lapansi linatulutsa zomera zake. 19Abale anga, ngati mmodzi wa inu apatuka pa choonadi ndipo wina wake ndi kumubweza, 20kumbukirani izi: Aliyense wobweza wochimwa kuchoka ku cholakwa chake, adzamupulumutsa ku imfa ndi kukwirira machimo ambiri.

Knijga O Kristu

Jakovljeva 5:1-20

Opomena bogatašima

1Čujte me, bogataši! Zaplačite i zakukajte nad nevoljama koje će vas snaći. 2Bogatstvo vam trune, a odjeću vam izgrizaju moljci. 3Vaše zlato i srebro hrđaju i postaju nevrijednima. Baš to bogatstvo u koje ste se pouzdali progutat će vaša tijela kao oganj. To blago koje ste skupili bit će dokaz protiv vas na Dan suda. 4Slušajte! Viču žeteoci vaših njiva kojima ste uskratili plaću. Plaća koju im niste dali viče protiv vas. Glasovi žetelaca doprli su do ušiju Gospodina nad vojskama. 5Živjeli ste na zemlji raskošno i razuzdano. Srca su vam utovljena za dan klanja. 6Osudili ste i ubili pravednika koji vam se nije mogao suprotstaviti.

Strpljivost u patnjama

7Draga braćo i sestre, strpite se do Gospodnjeg dolaska. I ratar, eto, iščekuje dragocjeni urod zemlje, čekajući ranu i kasnu kišu. 8Strpite se i vi i ohrabrite jer se Gospodnji dolazak približio.

9Ne prigovarajte jedni drugima, braćo i sestre, da vas Bog ne osudi. Pazite! Sudac već stoji pred vratima.

10Uzorom strpljivog podnošenja nevolja neka vam budu proroci koji su govorili u ime Gospodnje. 11Blaženima smatramo one koji su ustrajali. Job je bio čovjek koji je strpljivo trpio. Iz njegova iskustva vidimo da se Božja nakana pokazala dobrom jer je Bog pun samilosti i milosrđa.

12A prije svega, draga braćo i sestre, ne zaklinjite se ni nebom, ni zemljom, ni bilo čime drugim. Neka vaše “da” znači “da”, a vaše “ne” neka znači “ne”, da ne zgriješite i ne padnete pod osudu.

Snaga molitve

13Trpi li tko među vama? Neka se za to moli. Ako je tko radostan, neka pjeva hvalospjeve.

14Je li tko od vas bolestan? Neka dozove crkvene starješine da se mole nad njim. Neka ga pomažu uljem u ime Gospodnje 15pa će molitva vjere ozdraviti bolesnika. Gospodin će ga podignuti i oprostiti mu ako je zgriješio.

16Ispovijedajte dakle jedni drugima grijehe i molite se jedni za druge da ozdravite. Žarka molitva pravednika mnogo može učiniti. 17Ilija je bio samo čovjek kao i mi, ali kad se usrdno pomolio da ne pada kiša, nije pala na zemlju tri godine i šest mjeseci. 18Zatim se pomolio da kišna padne pa je nebo dalo kišu i zemlja je opet donijela rod.

Vraćanje zalutalih vjernika na pravi put

19Draga braćo i sestre, odluta li tko od vas od istine pa ga tko vrati, 20znajte da će onaj tko je vratio grešnika s krivog puta spasiti njegovu dušu od smrti i postignuti oproštenje mnogih grijeha.