Yakobo 3 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yakobo 3:1-18

Za Lilime

1Abale anga, ambiri musakhale aphunzitsi chifukwa mumadziwa kuti aphunzitsife tidzaweruzidwa mowuma kuposa anthu ena onse. 2Tonsefe timapunthwa mʼnjira zambiri. Ngati wina salakwa poyankhula, ameneyo ndi munthu wangwiro, wodziwa kuyangʼanira bwino thupi lake lonse.

3Tikayika tizitsulo mʼkamwa mwa akavalo kuti atimvere, timatha kuwongolera thupi lake lonse. 4Taonani sitima zapamadzi. Ngakhale ndi zazikulu kwambiri ndipo zimakankhidwa ndi mphepo yamphamvu, zimawongoleredwa ndi tsigiro lalingʼono kulikonse kumene woyendetsayo akufuna kupita. 5Momwemonso, lilime ndi kachiwalo kakangʼono ka thupi koma limadzitama kuti nʼkuchita zikuluzikulu. Tangoganizirani za nkhalango yayikulu imene ingapse ndi kalawi kamoto koyamba mochepa. 6Lilime nalonso ndi moto, dziko la zoyipa pakati pa ziwalo za thupi. Limawononga munthu yense wathunthu. Limayika zonse za moyo wake pa moto, ndipo moto wake ndi wochokera ku gehena.

7Mitundu yonse ya nyama, ya mbalame, ya zokwawa ndi ya zolengedwa za mʼnyanja, zikuwetedwa ndipo munthu wakhala akuziweta, 8koma palibe munthu amene angaweta lilime. Lilime ndipo silitha kupuma, ndi lodzaza ndi ululu wakupha.

9Ndi lilime lomwelo timatamanda Ambuye ndi Atate athu, komanso ndi lilime lomwelo timalalatira anthu, amene anapangidwa mʼchifanizo cha Mulungu. 10Mʼkamwa momwemo mutuluka matamando ndi kulalata. Abale anga, zisamatero ayi. 11Kodi madzi abwino ndi a mchere angatuluke pa kasupe mmodzi? 12Abale anga, kodi mtengo wa mkuyu nʼkubala mphesa, kapena mtengo wampesa nʼkubala nkhuyu? Kasupe wa madzi a mchere sangatulutsenso madzi abwino.

Mitundu Iwiri ya Nzeru

13Ndani mwa inu amene ndi wanzeru ndi womvetsa zinthu? Mulekeni aonetse ndi makhalidwe ake abwino kuti nzeru ndiye zikutsogolera kudzichepetsa kwake ndi zochita zake 14Koma ngati muli ndi mtima wakaduka ndi odzikonda, musadzitamandire kapena kukana choonadi. 15“Nzeru” zotere sizochokera kumwamba koma ndi za mʼdziko lapansi, si zauzimu koma ndi za ziwanda. 16Pakuti pamene pali kaduka ndi kudzikonda pomweponso pamakhala chisokonezo ndi zochitika zoyipa zonse.

17Koma nzeru imene imachoka kumwamba, poyamba ndi yangwiro, ndi yokonda mtendere, yoganizira za ena, yogonjera, yodzaza ndi chifundo ndi chipatso chabwino, yosakondera ndi yoona mtima. 18Anthu amtendere amene amadzala mtendere amakolola chilungamo.

New International Reader’s Version

James 3:1-18

Control What You Say

1My brothers and sisters, most of you shouldn’t become teachers. That’s because you know that those of us who teach will be held more accountable. 2All of us get tripped up in many ways. Suppose someone is never wrong in what they say. Then they are perfect. They are able to keep their whole body under control.

3We put a small piece of metal in the mouth of a horse to make it obey us. We can control the whole animal with it. 4And how about ships? They are very big. They are driven along by strong winds. But they are steered by a very small rudder. It makes them go where the captain wants to go. 5In the same way, the tongue is a small part of a person’s body. But it talks big. Think about how a small spark can set a big forest on fire. 6The tongue is also a fire. The tongue is the most evil part of the body. It makes the whole body impure. It sets a person’s whole way of life on fire. And the tongue itself is set on fire by hell.

7People have tamed all kinds of wild animals, birds, reptiles and sea creatures. And they still tame them. 8But no one can tame the tongue. It is an evil thing that never rests. It is full of deadly poison.

9With our tongues we praise our Lord and Father. With our tongues we curse people. We do it even though people have been created to be like God. 10Praise and cursing come out of the same mouth. My brothers and sisters, it shouldn’t be this way. 11Can fresh water and salt water flow out of the same spring? 12My brothers and sisters, can a fig tree produce olives? Can a grapevine produce figs? Of course not. And a saltwater spring can’t produce fresh water either.

Two Kinds of Wisdom

13Is anyone among you wise and understanding? That person should show it by living a good life. A wise person isn’t proud when they do good deeds. 14But suppose your hearts are jealous and bitter. Suppose you are concerned only about getting ahead. Then don’t brag about it. And don’t say no to the truth. 15Wisdom like this doesn’t come down from heaven. It belongs to the earth. It doesn’t come from the Holy Spirit. It comes from the devil. 16Are you jealous? Are you concerned only about getting ahead? Then your life will be a mess. You will be doing all kinds of evil things.

17But the wisdom that comes from heaven is pure. That’s the most important thing about it. And that’s not all. It also loves peace. It thinks about others. It obeys. It is full of mercy and good fruit. It is fair. It doesn’t pretend to be what it is not. 18Those who make peace plant it like a seed. They will harvest a crop of right living.