Yakobo 2 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yakobo 2:1-26

Kuchita Tsankho Nʼkosaloledwa

1Abale anga, okhulupirira Yesu Khristu waulemerero, musaonetse tsankho. 2Tangoganizirani, pakati panu patabwera munthu atavala mphete yagolide ndi zovala zapamwamba, ndipo winanso wosauka nʼkulowa atavala sanza. 3Ngati musamala kwambiri munthu wovala bwinoyu uja, nʼkumuwuza kuti, “Khalani pa mpando wabwinowu,” koma wosauka uja nʼkumuwuza kuti, “Ima apo,” kapena “Khala pansi pafupi ndi chopondapo mapazi angawa,” 4kodi simunachite tsankho pakati panu ndi kukhala oweruza a maganizo oyipa?

5Tamverani abale anga okondedwa, kodi Mulungu sanasankhe amene dziko lapansi limawaona ngati amphawi kuti akhale olemera mʼchikhulupiriro ndi kulowa ufumu umene Iye analonjeza kwa amene amamukonda? 6Koma mwakhala mukunyoza amphawi. Kodi si anthu olemerawa amene akukudyerani masuku pamutu? Si anthu amenewa amene amakukokerani ku bwalo la milandu? 7Kodi si omwewa amene amachita chipongwe dzina la wolemekezeka, limene inu mumatchulidwa?

8Ngati musungadi lamulo laufumu lija lopezeka mʼMalemba lakuti, “Konda mnansi wako monga iwe mwini,” ndiye kuti mukuchita bwino. 9Koma mukamaonetsa tsankho mukuchimwa, ndipo ndinu wochimwa monga wophwanya lamulo. 10Pakuti amene amasunga Malamulo onse, akangophwanya fundo imodzi yokha, waphwanya Malamulo onse. 11Pakuti amene anati “Usachite chigololo” ndi yemweyonso anati “Usaphe.” Ngati suchita chigololo koma umapha, ndiwe wophwanya Malamulo.

12Muziyankhula ndi kuchita zinthu monga anthu amene mudzaweruzidwe ndi lamulo limene limapereka ufulu, 13chifukwa munthu woweruza mopanda chifundo, nayenso adzaweruzidwa mopanda chifundo. Chifundo chimapambana pa chiweruzo.

Chikhulupiriro ndi Ntchito Zabwino

14Abale anga, phindu lake nʼchiyani ngati munthu anena kuti ali ndi chikhulupiriro koma chopanda ntchito zabwino? Kodi chikhulupiriro choterechi chingamupulumutse? 15Tangoganizirani, mʼbale kapena mlongo amene ali ndi usiwa, ndipo alibe chakudya cha tsiku ndi tsiku. 16Ngati mmodzi wa inu amuwuza kuti, “Pita ndi mtendere, ukafundidwe ndipo ukakhute,” koma osamupatsa zimene akuzisowa, phindu lake nʼchiyani pamenepa? 17Chomwechonso, chikhulupiriro chokha chopanda ntchito zabwino ndi chakufa.

18Koma wina anganene kuti, “Inuyo muli ndi chikhulupiriro koma ine ndili ndi ntchito zabwino.”

Onetsani chikhulupiriro chanu chopanda ntchito zabwino ndipo ineyo ndidzakuonetsani chikhulupiriro changa pochita ntchito zabwino. 19Mumakhulupirira kuti kuli Mulungu mmodzi yekha. Mumachita bwino. Komatu ngakhale ziwanda zimakhulupirira zimenezi ndipo zimanjenjemera ndi mantha.

20Munthu wopusa iwe, kodi ukufuna umboni woti chikhulupiriro chopanda ntchito zabwino nʼchakufa? 21Kodi Abrahamu kholo lathu sanatengedwe kukhala wolungama chifukwa cha zimene anachita pamene anapereka mwana wake Isake pa guwa lansembe? 22Tsono mukuona kuti chikhulupiriro chake ndi ntchito zabwino zinkachitika pamodzi, ndipo chikhulupiriro chake chinasanduka chenicheni chifukwa cha ntchito zake zabwino. 23Ndipo Malemba akunena kuti, “Abrahamu anakhulupirira Mulungu ndipo anatengedwa kukhala wolungama,” ndipo anatchedwa bwenzi la Mulungu. 24Tsono mukuona kuti munthu amasanduka wolungama ndi ntchito zabwino osati ndi chikhulupiriro chokha ayi.

25Nʼchimodzimodzinso, kodi wadama uja, Rahabe, sanasanduke wolungama chifukwa cha zomwe anachita pamene anapereka malo ogona kwa azondi aja ndi kuwathawitsira mbali ina? 26Monga thupi lopanda mzimu ndi lakufa, chomwechonso chikhulupiriro chopanda ntchito zabwino ndi chakufa.

Slovo na cestu

Jakubův 2:1-26

Pravá víra

1Bratři, jestliže věříte v Ježíše Krista, který je slavným Pánem všech, nemůžete měřit lidi podle kabátu.

2Představte si, že do vašeho shromáždění přijde bohatě oblečený host se zlatým prstenem na ruce a hned za ním obyčejný člověk v obnošených šatech. 3K prvnímu budete samá pozornost a uvedete ho na pěkné místo, zatímco druhého si ani nevšimnete a necháte ho někde stát. 4Čeho jste se dopustili? Udělali jste rozdíl mezi lidmi, a navíc podle zvrácených měřítek.

5Nezapomeňte, že Bůh si často z bezvýznamných lidí vírou dělá osobnosti a otevírá dveře do svého království těm, kdo ho milují, ne těm, kdo na to mají. 6A vy byste s takovým člověkem pohrdli! Copak vás právě vlivní lidé nepronásledují a nevláčejí po soudech? 7Vždyť právě oni se tak často posmívají jménu toho, který je pro vás vším!

8Korunou Božích přikázání je láska. Jednáte správně, posloucháte-li příkaz Písma: „Miluj svého bližního právě tak, jako miluješ sebe!“ 9Nadržovat jednomu a přehlížet druhého je podle tohoto zákona hřích.

10Člověk, který chce přísně dodržovat Boží zákon, ale v jedné věci se od něho odchyluje, je vinen právě tak jako ten, kdo porušuje celý zákon. 11Bůh, který řekl „Nezabiješ!“ řekl také „Nezcizoložíš!“. A tak i když jsi nikoho nezabil, ale porušil jsi nevěrou manželství, stejně jsi porušil zákon.

12Každý z vás bude souzen podle toho, zda se ve svém životě řídil či neřídil Božím zákonem lásky. Proto dávejte pozor na to, co říkáte a jak jednáte. 13Kdo jedná nemilosrdně, hrozí mu přísný soud. Milosrdenství však soud převažuje.

14Co by vám byla platná víra, bratři, kdybyste podle ní nežili? Myslíte, že vás taková víra spasí? 15Řekněme, že někdo z vašich přátel bude hladovět a nebude mít co na sebe. 16Řeknete-li mu: „Tak se měj dobře, ať nenachladneš a nemáš hlad!“ a sami mu nedáte ani jídlo ani oblečení, jakou to má cenu?

17Víra, která se neprojevuje činy, je sama o sobě mrtvá a bezcenná. 18Máte-li jen takovou víru, pak vám může někdo namítnout: „Ty mluvíš o své víře. Dokaž ji svými činy. A o mně říkáš, že víru nemám. O mé víře svědčí činy.“

19Věříš, že je Bůh. To je dobře. Ale nezapomeň, že v Boha věří i ďábel, ale nic mu to nepomůže. Chvěje se před Božím soudem. 20Vy bláhoví, ještě chcete, abych vás přesvědčoval o bezcennosti víry, která není dokázána skutky?

21Čím projevil Abraham svou víru? Tím, že byl ochoten i k takovému činu, jako obětovat Bohu svého syna Izáka. 22U něho šla víra ruku v ruce s činem a dozrála poslušností. 23O takovou víru jde v Písmu, když čteme: „Abraham uvěřil Bohu, Bůh se k němu přiznal a nazval ho svým přítelem.“ 24Vidíte, že Bůh může přijmout člověka jen tehdy, když svou víru dokazuje skutky. 25Poslušný čin víry zachránil i prostitutku Rachab, když ukryla izraelské zvědy a umožnila jim útěk. 26Víra bez činů je jako tělo bez duše.