Kuchita Tsankho Nʼkosaloledwa
1Abale anga, okhulupirira Yesu Khristu waulemerero, musaonetse tsankho. 2Tangoganizirani, pakati panu patabwera munthu atavala mphete yagolide ndi zovala zapamwamba, ndipo winanso wosauka nʼkulowa atavala sanza. 3Ngati musamala kwambiri munthu wovala bwinoyu uja, nʼkumuwuza kuti, “Khalani pa mpando wabwinowu,” koma wosauka uja nʼkumuwuza kuti, “Ima apo,” kapena “Khala pansi pafupi ndi chopondapo mapazi angawa,” 4kodi simunachite tsankho pakati panu ndi kukhala oweruza a maganizo oyipa?
5Tamverani abale anga okondedwa, kodi Mulungu sanasankhe amene dziko lapansi limawaona ngati amphawi kuti akhale olemera mʼchikhulupiriro ndi kulowa ufumu umene Iye analonjeza kwa amene amamukonda? 6Koma mwakhala mukunyoza amphawi. Kodi si anthu olemerawa amene akukudyerani masuku pamutu? Si anthu amenewa amene amakukokerani ku bwalo la milandu? 7Kodi si omwewa amene amachita chipongwe dzina la wolemekezeka, limene inu mumatchulidwa?
8Ngati musungadi lamulo laufumu lija lopezeka mʼMalemba lakuti, “Konda mnansi wako monga iwe mwini,” ndiye kuti mukuchita bwino. 9Koma mukamaonetsa tsankho mukuchimwa, ndipo ndinu wochimwa monga wophwanya lamulo. 10Pakuti amene amasunga Malamulo onse, akangophwanya fundo imodzi yokha, waphwanya Malamulo onse. 11Pakuti amene anati “Usachite chigololo” ndi yemweyonso anati “Usaphe.” Ngati suchita chigololo koma umapha, ndiwe wophwanya Malamulo.
12Muziyankhula ndi kuchita zinthu monga anthu amene mudzaweruzidwe ndi lamulo limene limapereka ufulu, 13chifukwa munthu woweruza mopanda chifundo, nayenso adzaweruzidwa mopanda chifundo. Chifundo chimapambana pa chiweruzo.
Chikhulupiriro ndi Ntchito Zabwino
14Abale anga, phindu lake nʼchiyani ngati munthu anena kuti ali ndi chikhulupiriro koma chopanda ntchito zabwino? Kodi chikhulupiriro choterechi chingamupulumutse? 15Tangoganizirani, mʼbale kapena mlongo amene ali ndi usiwa, ndipo alibe chakudya cha tsiku ndi tsiku. 16Ngati mmodzi wa inu amuwuza kuti, “Pita ndi mtendere, ukafundidwe ndipo ukakhute,” koma osamupatsa zimene akuzisowa, phindu lake nʼchiyani pamenepa? 17Chomwechonso, chikhulupiriro chokha chopanda ntchito zabwino ndi chakufa.
18Koma wina anganene kuti, “Inuyo muli ndi chikhulupiriro koma ine ndili ndi ntchito zabwino.”
Onetsani chikhulupiriro chanu chopanda ntchito zabwino ndipo ineyo ndidzakuonetsani chikhulupiriro changa pochita ntchito zabwino. 19Mumakhulupirira kuti kuli Mulungu mmodzi yekha. Mumachita bwino. Komatu ngakhale ziwanda zimakhulupirira zimenezi ndipo zimanjenjemera ndi mantha.
20Munthu wopusa iwe, kodi ukufuna umboni woti chikhulupiriro chopanda ntchito zabwino nʼchakufa? 21Kodi Abrahamu kholo lathu sanatengedwe kukhala wolungama chifukwa cha zimene anachita pamene anapereka mwana wake Isake pa guwa lansembe? 22Tsono mukuona kuti chikhulupiriro chake ndi ntchito zabwino zinkachitika pamodzi, ndipo chikhulupiriro chake chinasanduka chenicheni chifukwa cha ntchito zake zabwino. 23Ndipo Malemba akunena kuti, “Abrahamu anakhulupirira Mulungu ndipo anatengedwa kukhala wolungama,” ndipo anatchedwa bwenzi la Mulungu. 24Tsono mukuona kuti munthu amasanduka wolungama ndi ntchito zabwino osati ndi chikhulupiriro chokha ayi.
25Nʼchimodzimodzinso, kodi wadama uja, Rahabe, sanasanduke wolungama chifukwa cha zomwe anachita pamene anapereka malo ogona kwa azondi aja ndi kuwathawitsira mbali ina? 26Monga thupi lopanda mzimu ndi lakufa, chomwechonso chikhulupiriro chopanda ntchito zabwino ndi chakufa.
Upozorenje na pristranost
1Braćo moja, vi vjerujete u slavnoga Gospodina Isusa Krista i zato ne budite pristrani!
2Kad bi u vaš sastanak ušao čovjek sa zlatnim prstenjem i u skupoj odjeći, a istodobno došao i bijedno obučeni siromah 3te kad biste onomu u skupoj odjeći rekli: “Sjednite ovdje, na dobro mjesto”, a siromahu: “Ti možeš ondje stajati ili sjesti na pod pokraj mojeg stolca”— 4ne bi li to značilo da ste pristrani i da nepravedno sudite?
5Poslušajte me, ljubljena moja braćo! Zar Bog nije izabrao siromahe ovoga svijeta da budu bogataši u vjeri? Nisu li oni baštinici Kraljevstva koje je Bog obećao ljudima koji njega ljube? 6A vi ste prezreli siromaha! Zar nisu upravo bogataši ti koji vas tlače i koji vas povlače po sudovima? 7Ne kunu li upravo oni lijepo ime Onoga po kome se zovete?
8Ako zaista izvršavate kraljevski zakon iz Pisma: “Ljubi svojega bližnjega kao sebe samoga”,2:8 Levitski zakonik 19:18. dobro činite. 9Ali ako pristrano postupate prema ljudima, činite grijeh, i prema Zakonu ste prijestupnici. 10Tko vrši sav Zakon, a samo u jednoj odredbi pogriješi, kriv je kao da je sve prekršio. 11Jer Bog koji je rekao: “Ne čini preljub” kazao je i: “Ne ubij!” Pa ako i nisi počinio preljub, ali si nekog ubio, u potpunosti si prekršio Zakon i pred Bogom si kriv za sve.
12I zato, ma što govorili ili činili, imajte na umu da će vam biti suđeno prema zakonu ljubavi, zakonu koji vas je oslobodio. 13Jer za onoga tko nije milostiv prema drugima, na sudu također neće biti milosti. Ali za one koji su milosrdni, Božje će milosrđe pobijediti nad sudom.
Vjera bez dobrih djela je mrtva
14Draga braćo i sestre, što koristi ako tko veli da ima vjeru, a ne čini dobra djela? Zar ga takva vjera može spasiti? 15Ako su vam koji brat ili sestra bez svagdašnje hrane i odjeće, 16a vi im kažete: “Idite u miru, utoplite se i najedite se”—ali im ne date hranu ni odjeću, od kakve je to koristi?
17Tako je i s vjerom: ne rodi li dobrim djelima, mrtva je i nekorisna.
18Netko bi, naprotiv, mogao reći: “Ti imaš vjeru, a ja imam djela.” Ali ja kažem: “Dokaži mi svoju vjeru odvojeno od djela, a ja ću tebi dokazati svoju vjeru djelima!”
19Zar još misliš kako je dostatno vjerovati da postoji samo jedan Bog? Dobro je to vjerovati. I zlodusi u to vjeruju—i dršću! 20Kad ćeš već jednom naučiti, šuplja glavo, da je vjera bez dobrih djela nekorisna?
21Zar se naš predak Abraham nije pred Bogom opravdao djelom kad je na žrtvenik prinio svojega sina Izaka? 22Toliko je vjerovao Bogu da je bio voljan učiniti sve što on od njega zatraži. Vjera mu je dakle pomogla da učini dobro djelo te je tako, s pomoću djela, postala savršenom. 23Tako se ispunilo ono što piše u Svetome pismu: “Abraham povjerovao Bogu i Bog ga je proglasio pravednim zbog njegove vjere.”2:23 Postanak 15:6. Nazvao ga je čak “Božjim prijateljem”. 24Vidite, dakle, čovjek biva opravdan zbog svojih djela, a ne samo zbog svoje vjere.
25Nije li se isto tako djelom opravdala i bludnica Rahaba kad je primila glasnike i izvela ih drugim putem? 26Kao što je tijelo bez duha mrtvo, mrtva je i vjera bez djela.