Yakobo 1 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yakobo 1:1-27

1Yakobo, mtumiki wa Mulungu ndi wa Ambuye Yesu Khristu,

kulembera mafuko khumi ndi awiri obalalikana ku mayiko osiyanasiyana.

Landirani moni.

Masautso ndi Mayesero

2Abale, muchiyese ngati chimwemwe chenicheni nthawi zonse pamene mukukumana ndi mayesero amitundumitundu. 3Inu mukudziwa kuti kuyesedwa kwa chikhulupiriro chanu kumabweretsa chipiriro. 4Chipiriro chiyenera kugwira ntchito yake kuti mukhale okhwima ndi angwiro, osasowa kanthu kalikonse. 5Ngati wina pakati panu akusowa nzeru, apemphe kwa Mulungu amene amapereka kwa onse mwaulere ndi mosatonzera, ndipo adzapatsidwa. 6Koma pamene mupempha, muyenera kukhulupirira osakayika, chifukwa amene amakayika ali ngati mafunde pa nyanja amene amawinduka nakankhika ndi mphepo. 7Munthu wotere asayembekezere kulandira kalikonse kuchokera kwa Ambuye. 8Iyeyu ndi munthu wa mitima iwiri, wosakhazikika pa zimene akuchita.

9Abale omwe ndi anthu wamba anyadire pamene akwezedwa. 10Koma olemera anyadire pamene atsitsidwa, chifukwa adzatha ngati duwa lakuthengo. 11Pakuti dzuwa limatuluka nʼkutentha kwake, ndipo limafotetsa zomera. Duwa lake limathothoka ndipo kukongola kwake kumatheratu. Momwemonso munthu wachuma adzazimirira ngakhale atamachitabe malonda ake.

12Wodala ndi munthu amene amapirira mʼmayesero, chifukwa akapambana adzalandira chipewa cha ulemerero chimene Mulungu analonjeza anthu amene amamukonda.

13Munthu akayesedwa asanene kuti, “Mulungu akundiyesa.” Pakuti Mulungu sangayesedwe ndi choyipa kapena Iyeyo kuyesa munthu aliyense. 14Koma munthu aliyense amayesedwa akakokedwa ndi zilakolako zake zoyipa ndi kukopedwa nazo. 15Pamenepo, chilakolako chikakula chimabala tchimo; ndipo tchimo likakhwima limabereka imfa.

16Musanyengedwe abale anga okondedwa. 17Mphatso iliyonse yabwino ndi yangwiro imachokera kumwamba, kwa Atate mwini kuwala, amene sasintha ngati mthunzi woyendayenda. 18Iye anasankha kutibereka ife kudzera mʼmawu a choonadi, kuti pakati pa zolengedwa zake zonse, tikakhale ngati zipatso zoyamba.

Kumva ndi Kuchita

19Abale anga okondedwa, gwiritsitsani mawu awa: munthu aliyense azifulumira kumva, koma asamafulumire kuyankhula, ndipo asamafulumirenso kupsa mtima. 20Pakuti mkwiyo wa munthu subweretsa chilungamo chimene amafuna Mulungu. 21Choncho chotsani chizolowezi choyipa ndi khalidwe loyipa pakati panu, ndipo modzichepetsa landirani mawu amene anadzalidwa mwa inu, amene akhoza kukupulumutsani.

22Musamangomvetsera chabe mawu, ndi kumadzinyenga nokha. Chitani zimene mawuwo amanena. 23Munthu aliyense amene amangomva mawu koma osachita zimene mawuwo amanena, ali ngati munthu amene amayangʼana nkhope yake pa galasi. 24Akadziyangʼana amachoka, nthawi yomweyo nʼkuyiwala mmene akuonekera. 25Koma munthu amene amayangʼana mwachidwi lamulo langwiro limene limapatsa ufulu ndi kupitiriza kutero, osayiwala chimene wamva koma kuchita adzadalitsika pa zimene amachita.

26Ngati wina amadziyesa ngati ndi wachipembedzo, koma chonsecho saletsa lilime lake, amadzinyenga yekha ndipo chipembedzo chakecho ndi cha chabechabe. 27Chipembedzo chimene Mulungu Atate athu amachivomereza kuti ndi changwiro ndi chopanda zolakwika ndi ichi: kusamalira ana amasiye ndi akazi amasiye pa mavuto awo, ndi kudzisunga bwino kuopa kudetsedwa ndi dziko lapansi.

Knijga O Kristu

Jakovljeva 1:1-27

1Jakov, sluga Boga i Gospodina Isusa Krista, piše dvanaestorim plemenima rasijanima po svijetu i pozdravlja ih.

Vjera i postojanost

2Draga braćo i sestre, kad god zapadnete u kušnju, smatrajte da se imate čemu radovati. 3Jer kad vam je vjera na kušnji, jača vaša postojanost. 4Zato je pustite da se potpuno razvije, da postanete besprijekornima, bez ikakva nedostatka.

5Treba li vam mudrosti, iskajte ju od Boga koji je svima daje rado, obilno i bez prigovora. 6Ali tražite s vjerom, ne sumnjajući da ćete dobiti, jer čovjek koji sumnja nestalan je kao morski valovi koje vjetar lako baca amo-tamo. 7Takav neka se ne nada išta primiti od Gospodina 8jer je čovjek podijeljene duše, nepostojan na svim svojim putovima.

9Neka se kršćanin1:9 U grčkome: brat. niskoga položaja ponosi time što ga je Bog uzvisio, 10a bogataš time što ga je ponizio, jer će nestati poput poljskoga cvijeta. 11Sunce žarko zasja, biljka usahne i cvijet joj otpadne te sva njegova ljepota nestane. Tako će i bogataši usahnuti na svojim putovima.

12Blago čovjeku koji odolijeva kušnji. Kad se pokaže prokušanim, dobit će vijenac života koji je Bog obećao svima koji ga ljube. 13Neka nitko od vas u napasti ne kaže: “Bog me napastuje.” Niti se Boga može napastovati da čini zlo, niti on koga napastuje. 14Svakoga, naprotiv, napastuje njegova vlastita požuda koja ga privlači i mami. 15Požuda zatim začne i rodi grijeh, a kad se grijeh potpuno razvije, rađa smrt.

16Zato se ne dajte varati, ljubljena braćo. 17Sve što je dobro i savršeno dolazi nam odozgora, od Boga koji je stvorio sva nebeska svjetlila. Za razliku od njih, on se nikada ne mijenja; u njemu nema sjene zbog mijena. 18On nas je dragovoljno rodio riječju istine, da budemo prvenci iznad svih stvorenja.

Poslušnost i djela

19Upamtite, draga braćo: svatko bi trebao biti brz na slušanju, spor na pričanju i spor na srdžbi 20jer ljudska srdžba ne može postupati prema Božjoj pravednosti.

21Zato izbacite iz svojih života svako zlo i prljavštinu te ponizno prihvatite Božju poruku zasađenu u svoja srca jer ona može spasiti vaše duše.

22I ne zaboravite da tu poruku nije dostatno samo slušati već treba i postupati prema njoj. Inače sami sebe zavaravate. 23Jer ako samo slušate Riječ, a ne vršite ju, onda ste poput čovjeka koji pogleda vlastito lice u zrcalu, 24ali čim se promotri, odmah ode ne popravivši što je trebalo i zaboravi kako izgleda. 25Ali tko se ogleda u savršenomu Božjem zakonu—zakonu koji oslobađa—i nije samo zaboravan slušatelj, nego ga zaista i izvršava, Bog će ga blagosloviti u svemu što čini.

26Umišlja li tko da je pobožan, a ne obuzdava svoj jezik, sam sebe vara jer je njegova pobožnost nevrijedna. 27Želite li da vaša pobožnost u očima Boga Oca bude čista i neokaljana, pomažite sirotama i udovicama u njihovoj nevolji i čuvajte se neokaljanima od pokvarenosti ovoga svijeta.