Tito 3 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tito 3:1-15

Kuchita Ntchito Zabwino

1Uwakumbutse anthu kuti azigonjera oweruza ndi olamulira, aziwamvera ndi kukhala okonzeka kuchita chilichonse chabwino. 2Asamachitire chipongwe aliyense, asamakangane, akhale ofatsa ndipo oganizira ena, ndipo nthawi zonse akhale aulemu kwa anthu onse.

3Nthawi ina tinali opusa, osamvera, onamizidwa ndi omangidwa ndi zilakolako ndi zokondweretsa zamitundumitundu. Tinkakhala moyo wadumbo ndi wakaduka, odedwa ndiponso odana wina ndi mnzake. 4Koma kukoma mtima ndi chikondi cha Mulungu Mpulumutsi wathu chitaonekera, 5Iye anatipulumutsa, osati chifukwa cha ntchito zathu zolungama zimene tinachita koma chifukwa cha chifundo chake. Anatipulumutsa potisambitsa, kutibadwitsa kwatsopano ndi kutikonzanso mwa Mzimu Woyera 6amene anatipatsa mowolowamanja kudzera mwa Yesu Khristu Mpulumutsi wathu, 7kuti titalungamitsidwa mwachisomo chake, tikhale olowamʼmalo okhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha. 8Mawuwa ndi okhulupirika ndipo ine ndikufuna kuti iwe utsindike zinthu izi, kuti amene akhulupirira Mulungu adzipereke kuchita ntchito zabwino. Zinthu izi ndi zabwino kwambiri ndi zopindulitsa kwa aliyense.

9Koma upewe kufufuzafufuza zopusa, kuwerengawerenga mndandanda wa mibado ya makolo, mikangano ndi mitsutso pa za Malamulo, chifukwa zimenezi ndi zosapindulitsa ndi zopanda pake. 10Munthu woyambitsa mipatuko umuchenjeze koyamba, ndiponso umuchenjeze kachiwiri. Kenaka umupewe. 11Iwe udziwe kuti munthu wotero ngosokoneza ndi wochimwa, ndipo akudzitsutsa yekha.

Mawu Otsiriza

12Ndikadzamutuma Artema kapena Tukiko kwanuko, udzayesetse kundipeza ku Nikapoli, chifukwa ndatsimikiza kukhala kumeneko pa nthawi yozizira. 13Uyesetse chilichonse ungathe kuthandiza Zena katswiri wa malamulo ndi Apolo, kuti apitirize ulendo wawo, ndipo uwonetsetse asasowe kanthu. 14Anthu athu aphunzire kudzipereka pogwira ntchito zabwino, nʼcholinga chakuti athandize zinthu zimene zikufunika msangamsanga. Ndipo asakhale moyo osapindulitsa.

15Onse amene ali ndi ine akupereka moni. Upereke moni kwa amene amatikonda ife mʼchikhulupiriro.

Chisomo chikhale ndi inu nonse.

O Livro

Tito 3:1-15

Fazendo o bem

1Lembra a todos que devem sujeitar-se aos governantes e autoridades instituídas, e obedecer às leis, estando prontos a participar em qualquer obra boa. 2Não devem falar mal de ninguém, nem meter-se em disputas; devem antes ser amáveis, mostrando simpatia para com toda a gente.

3Porque nós também, noutro tempo, éramos insensatos e revoltados. Andávamos ao sabor da opinião de outras pessoas, dominados por paixões variadas e por deleites dos sentidos. Vivíamos sob a lei da maldade, da inveja e do ódio e, por isso, nos odiávamos uns aos outros.

4Mas quando a bondade e o amor divino de Deus nosso Salvador se manifestaram para com a humanidade, 5ele salvou-nos pela lavagem purificadora do Espírito Santo, da qual emergimos como novamente nascidos, não por causa de atos justos que tivéssemos praticado, mas por causa da sua misericórdia. 6Esse Espírito Santo, Deus o derramou abundantemente sobre nós, através de Jesus Cristo, nosso Salvador. 7E desta forma, sendo declarados justos pela sua graça, tornámo-nos herdeiros da esperança da vida eterna.

8O que te tenho dito merece toda a confiança. Quero que insistas nisto com firmeza, para que os que creem em Deus procurem dedicar-se à prática do bem. Uma vida assim é reta e torna-se proveitosa para toda a gente.

9E não te deixes envolver em discussões insensatas de genealogias e contendas sobre a obediência à Lei. São coisas inúteis e sem verdadeiro significado. 10Se alguém estiver a causar divisões avisa-o uma primeira e segunda vez; mas se não se convencer, afasta-te dele. 11O seu entendimento está pervertido; por isso, peca, e já tem a sua própria condenação.

Saudações

12Assim que te tiver enviado Artemas e Tíquico, procura vir ter comigo a Nicópolis, porque decidi passar aí o inverno. 13Peço-te que ajudes Zenas, o jurista, e Apolo, na sua viagem, para que nada lhes falte. 14É preciso que os cristãos das nossas congregações saibam o que é praticar o bem e ajudar os outros em caso de necessidade. Só assim as suas vidas não ficarão improdutivas.

15Todos os que aqui estão comigo te mandam saudações. E tu saúda os que nos amam na fé.

Que a graça de Deus seja com todos!