Tito 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tito 3:1-15

Kuchita Ntchito Zabwino

1Uwakumbutse anthu kuti azigonjera oweruza ndi olamulira, aziwamvera ndi kukhala okonzeka kuchita chilichonse chabwino. 2Asamachitire chipongwe aliyense, asamakangane, akhale ofatsa ndipo oganizira ena, ndipo nthawi zonse akhale aulemu kwa anthu onse.

3Nthawi ina tinali opusa, osamvera, onamizidwa ndi omangidwa ndi zilakolako ndi zokondweretsa zamitundumitundu. Tinkakhala moyo wadumbo ndi wakaduka, odedwa ndiponso odana wina ndi mnzake. 4Koma kukoma mtima ndi chikondi cha Mulungu Mpulumutsi wathu chitaonekera, 5Iye anatipulumutsa, osati chifukwa cha ntchito zathu zolungama zimene tinachita koma chifukwa cha chifundo chake. Anatipulumutsa potisambitsa, kutibadwitsa kwatsopano ndi kutikonzanso mwa Mzimu Woyera 6amene anatipatsa mowolowamanja kudzera mwa Yesu Khristu Mpulumutsi wathu, 7kuti titalungamitsidwa mwachisomo chake, tikhale olowamʼmalo okhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha. 8Mawuwa ndi okhulupirika ndipo ine ndikufuna kuti iwe utsindike zinthu izi, kuti amene akhulupirira Mulungu adzipereke kuchita ntchito zabwino. Zinthu izi ndi zabwino kwambiri ndi zopindulitsa kwa aliyense.

9Koma upewe kufufuzafufuza zopusa, kuwerengawerenga mndandanda wa mibado ya makolo, mikangano ndi mitsutso pa za Malamulo, chifukwa zimenezi ndi zosapindulitsa ndi zopanda pake. 10Munthu woyambitsa mipatuko umuchenjeze koyamba, ndiponso umuchenjeze kachiwiri. Kenaka umupewe. 11Iwe udziwe kuti munthu wotero ngosokoneza ndi wochimwa, ndipo akudzitsutsa yekha.

Mawu Otsiriza

12Ndikadzamutuma Artema kapena Tukiko kwanuko, udzayesetse kundipeza ku Nikapoli, chifukwa ndatsimikiza kukhala kumeneko pa nthawi yozizira. 13Uyesetse chilichonse ungathe kuthandiza Zena katswiri wa malamulo ndi Apolo, kuti apitirize ulendo wawo, ndipo uwonetsetse asasowe kanthu. 14Anthu athu aphunzire kudzipereka pogwira ntchito zabwino, nʼcholinga chakuti athandize zinthu zimene zikufunika msangamsanga. Ndipo asakhale moyo osapindulitsa.

15Onse amene ali ndi ine akupereka moni. Upereke moni kwa amene amatikonda ife mʼchikhulupiriro.

Chisomo chikhale ndi inu nonse.

New Russian Translation

Титу 3:1-15

Посвящение себя добрым делам

1Напоминай людям о том, что они должны подчиняться начальству и властям и быть послушными и готовыми выполнить любое доброе дело. 2Учи их также не злословить никого, не быть задиристыми, но мягкими, и являть кротость в обращении со всеми людьми.

3Мы тоже когда-то были глупы, непокорны, обмануты и порабощены всевозможными страстями и удовольствиями. Нашу жизнь наполняли злоба и зависть, мы были отвратительны, ненавидя друг друга. 4Но Бог, наш Спаситель, проявил к нам доброту и любовь. 5Он спас нас не за наши праведные дела, которые мы совершили, а по Своей милости, через возрождающее омовение и обновление Святым Духом, 6Которого щедро излил на нас через нашего Спасителя Иисуса Христа, 7чтобы мы, оправданные Его благодатью, стали наследниками вечной жизни, на которую мы надеемся.

Избегай разделений

8Эти слова верны, и я хочу, чтобы ты подчеркивал эти истины, чтобы уверовавшие в Бога посвятили себя добрым делам. Все это хорошо и полезно людям. 9Избегай глупых прений, пустых разговоров о родословиях, споров и ссор по поводу Закона: это не приносит пользы и не имеет смысла. 10Того, кто вызывает разделения, предупреди раз, другой, но больше времени на него не трать. 11Такой человек уже полностью сбился с пути, грешит и этим сам себя осудил.

Просьбы и заключительные приветствия

12Когда я пошлю к тебе Артема или Тихика, постарайся прийти ко мне в Никополь, я решил там перезимовать. 13Помоги, пожалуйста, юристу Зенасу и Аполлосу в их путешествии, позаботься о том, чтобы у них было все необходимое. 14Пусть и наши учатся посвящать себя деланию добра ради удовлетворения необходимых нужд других, чтобы их жизнь не была бесплодной.

15Все, кто находится сейчас со мной, передают тебе приветы. Привет всем верующим, любящим нас. Благодать Бога пусть будет со всеми вами.