Tito 1 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tito 1:1-16

1Ndine Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndinatumidwa kuti nditsogolere amene Mulungu anawasankha ku chikhulupiriro ndi ku chidziwitso cha choonadi chimene chimawafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu 2ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. 3Pa nthawi yake Mulungu, Mpulumutsi wathu anawulula poyera mawu ake ndipo analamula kuti ndipatsidwe udindo wolalikira uthengawu.

4Kwa Tito, mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro cha ife tonse:

Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.

Ntchito ya Tito ku Krete

5Ndinakusiya ku Krete kuti ulongosole zonse zimene ndinazisiya zisanathe ndiponso usankhe akulu ampingo mʼmizinda yonse, monga momwe ndinakulamulira. 6Mkulu wampingo akhale munthu wopanda cholakwa, akhale wa mkazi mmodzi yekha, munthu amene ana ake ndi okhulupirira, osati amakhalidwe oyipa ndi osamvera. 7Popeza mkulu wa mpingo amayendetsa ntchito za banja la Mulungu, ayenera kukhala wopanda cholakwa, asakhale womva zayekha, kapena wopsa mtima msanga, kapena womwa zoledzeretsa, kapena wandewu, kapena wopeza phindu mwachinyengo. 8Koma akhale wosamala bwino alendo, wokonda zabwino, wodziretsa, wolungama, woyera mtima ndi wosunga mwambo. 9Iye ayenera kugwiritsa mawu okhulupirika monga tinaphunzitsira, kuti athe kulimbikitsa ena ndi chiphunzitso choona ndiponso kugonjetsa amene atsutsana nacho.

Kudzudzula Olephera Kuchita Bwino

10Paja pali anthu ambiri osaweruzika, makamaka mʼgulu la anthu a mdulidwe, oyankhula nkhani zopanda pake ndi kusocheretsa anzawo. 11Ayenera kuletsedwa kuyankhula chifukwa akusokoneza mabanja athunthu pophunzitsa zinthu zomwe sayenera kuwaphunzitsa. Iwo amachita izi kuti apeze ndalama mwachinyengo. 12Mneneri wina, mmodzi wa iwo omwewo anati, “Akrete nthawi zonse ndi amabodza, akhalidwe loyipitsitsa ndiponso alesi adyera.” 13Mawu amenewa ndi woona. Nʼchifukwa chake, uwadzudzule mwamphamvu, kuti akhale ndi chikhulupiriro choona, 14kuti asasamalenso nthano za Chiyuda, ndi malamulo a anthu amene akukana choonadi. 15Kwa oyera mtima, zinthu zonse ndi zoyera, koma kwa amene ndi odetsedwa ndi osakhulupirira, palibe kanthu koyera. Kunena zoona, mitima yawo ndi chikumbumtima chawo, zonse nʼzodetsedwa. 16Iwo amati amadziwa Mulungu, pamene ndi zochita zawo amamukana. Ndi anthu onyansa ndi osamvera, ndi osayenera kuchita kalikonse kabwino.

Thai New Contemporary Bible

ทิตัส 1:1-16

1จดหมายฉบับนี้จากข้าพเจ้าเปาโลผู้เป็นผู้รับใช้ของพระเจ้าและอัครทูตของพระเยซูคริสต์ เพื่อความเชื่อของผู้ที่พระเจ้าทรงเลือกสรรและเพื่อความรู้ถึงความจริงอันนำไปสู่ทางพระเจ้า 2คือความเชื่อและความรู้ที่ตั้งอยู่บนความหวังในชีวิตนิรันดร์ ซึ่งพระเจ้าผู้ไม่ทรงมุสาได้ทรงสัญญาไว้ตั้งแต่ก่อนจุดเริ่มต้นของเวลา 3และเมื่อถึงวาระที่ทรงกำหนดพระองค์ได้ทรงให้พระวจนะของพระองค์เป็นที่ทราบทั่วกันผ่านทางการประกาศที่ได้ทรงมอบหมายไว้แก่ข้าพเจ้าตามพระบัญชาของพระเจ้าองค์พระผู้ช่วยให้รอดของเรา

4ถึงทิตัสลูกแท้ของข้าพเจ้าในความเชื่อเดียวกัน

ขอพระคุณและสันติสุขจากพระเจ้าพระบิดาและพระเยซูคริสต์องค์พระผู้ช่วยให้รอดของเรามีแก่ท่าน

ภารกิจของทิตัสที่เกาะครีต

5เหตุที่ข้าพเจ้าละท่านไว้ที่เกาะครีตก็เพื่อให้ท่านสะสางงานที่ยังคั่งค้างและแต่งตั้ง1:5 หรือสถาปนาคณะผู้ปกครองของคริสตจักรในทุกเมืองตามที่ข้าพเจ้าได้สั่งท่านไว้ 6ผู้ปกครองนั้นต้องปราศจากที่ติ เป็นสามีของภรรยาคนเดียว บุตรของเขาต้องเป็นผู้เชื่อและไม่มีพฤติกรรมที่ใครจะกล่าวหาได้ว่าเป็นคนพาลเกเรและไม่เชื่อฟัง 7เนื่องจากผู้ปกครอง1:7 โดยปกติแปลว่าบิชอปดูแลคริสตจักรได้รับมอบหมายงานของพระเจ้า เขาจึงต้องไม่มีที่ติ ไม่ใช้อำนาจบาตรใหญ่ ไม่เลือดร้อนเจ้าโทสะ ไม่ดื่มสุราเมามาย ไม่ก้าวร้าวใช้กำลัง ไม่หาประโยชน์ในทางทุจริต 8แต่เขาต้องเป็นผู้มีน้ำใจรับรองแขก รักสิ่งที่ดี ควบคุมตัวเองได้ ยุติธรรม บริสุทธิ์ และมีวินัย 9เขาต้องยึดมั่นในหลักคำสอนอันเชื่อถือได้ตามที่เรียนรู้มา เพื่อเขาจะสามารถให้กำลังผู้อื่นด้วยคำสอนอันมีหลักและโต้แย้งผู้ที่ต่อต้านคำสอนนั้น

10เพราะมีหลายคนที่มักขัดขืนไม่เชื่อฟังพวกเขา เป็นคนดีแต่พูดและหลอกลวงโดยเฉพาะคนเหล่านั้นจากกลุ่มเข้าสุหนัต 11ต้องทำให้พวกนี้สงบปากสงบคำ เพราะหลายครัวเรือนกำลังถูกเขาทำลายทั้งครอบครัวโดยการสอนสิ่งที่เขาไม่ควรสอนและการสอนนั้นก็เพื่อหาประโยชน์ในทางทุจริต 12แม้แต่ผู้พยากรณ์คนหนึ่งของพวกเขาเองยังกล่าวว่า “ชาวครีตเป็นคนโกหกเสมอ เป็นสัตว์ป่าชั่วร้าย เป็นคนตะกละตะกลามที่เกียจคร้าน” 13และคำพูดนี้ก็เป็นความจริง ฉะนั้นจงว่ากล่าวเขาอย่างเข้มงวดเพื่อเขาจะไม่มีข้อบกพร่องในความเชื่อนั้น 14และจะไม่ใส่ใจกับนิยายปรัมปราของยิวหรือกฎเกณฑ์ของพวกที่ปฏิเสธความจริง 15สำหรับผู้บริสุทธิ์นั้นทุกสิ่งก็บริสุทธิ์ แต่สำหรับผู้เสื่อมทรามและไม่เชื่อแล้ว ไม่มีสิ่งใดบริสุทธิ์เลย อันที่จริงความคิดและจิตสำนึกของเขาก็เสื่อมทราม 16เขาอ้างว่ารู้จักพระเจ้า แต่ปฏิเสธพระองค์ด้วยการกระทำของเขา เขาเป็นคนน่ารังเกียจ ไม่เชื่อฟัง ไม่เหมาะสำหรับการทำดีใดๆ