Tito 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tito 1:1-16

1Ndine Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndinatumidwa kuti nditsogolere amene Mulungu anawasankha ku chikhulupiriro ndi ku chidziwitso cha choonadi chimene chimawafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu 2ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. 3Pa nthawi yake Mulungu, Mpulumutsi wathu anawulula poyera mawu ake ndipo analamula kuti ndipatsidwe udindo wolalikira uthengawu.

4Kwa Tito, mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro cha ife tonse:

Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.

Ntchito ya Tito ku Krete

5Ndinakusiya ku Krete kuti ulongosole zonse zimene ndinazisiya zisanathe ndiponso usankhe akulu ampingo mʼmizinda yonse, monga momwe ndinakulamulira. 6Mkulu wampingo akhale munthu wopanda cholakwa, akhale wa mkazi mmodzi yekha, munthu amene ana ake ndi okhulupirira, osati amakhalidwe oyipa ndi osamvera. 7Popeza mkulu wa mpingo amayendetsa ntchito za banja la Mulungu, ayenera kukhala wopanda cholakwa, asakhale womva zayekha, kapena wopsa mtima msanga, kapena womwa zoledzeretsa, kapena wandewu, kapena wopeza phindu mwachinyengo. 8Koma akhale wosamala bwino alendo, wokonda zabwino, wodziretsa, wolungama, woyera mtima ndi wosunga mwambo. 9Iye ayenera kugwiritsa mawu okhulupirika monga tinaphunzitsira, kuti athe kulimbikitsa ena ndi chiphunzitso choona ndiponso kugonjetsa amene atsutsana nacho.

Kudzudzula Olephera Kuchita Bwino

10Paja pali anthu ambiri osaweruzika, makamaka mʼgulu la anthu a mdulidwe, oyankhula nkhani zopanda pake ndi kusocheretsa anzawo. 11Ayenera kuletsedwa kuyankhula chifukwa akusokoneza mabanja athunthu pophunzitsa zinthu zomwe sayenera kuwaphunzitsa. Iwo amachita izi kuti apeze ndalama mwachinyengo. 12Mneneri wina, mmodzi wa iwo omwewo anati, “Akrete nthawi zonse ndi amabodza, akhalidwe loyipitsitsa ndiponso alesi adyera.” 13Mawu amenewa ndi woona. Nʼchifukwa chake, uwadzudzule mwamphamvu, kuti akhale ndi chikhulupiriro choona, 14kuti asasamalenso nthano za Chiyuda, ndi malamulo a anthu amene akukana choonadi. 15Kwa oyera mtima, zinthu zonse ndi zoyera, koma kwa amene ndi odetsedwa ndi osakhulupirira, palibe kanthu koyera. Kunena zoona, mitima yawo ndi chikumbumtima chawo, zonse nʼzodetsedwa. 16Iwo amati amadziwa Mulungu, pamene ndi zochita zawo amamukana. Ndi anthu onyansa ndi osamvera, ndi osayenera kuchita kalikonse kabwino.

New Russian Translation

Титу 1:1-16

Приветствие

1От Павла, слуги Бога и апостола Иисуса Христа, посланного, чтобы приводить избранных Богом к вере и к познанию истины, которая ведет к благочестию 2и дает надежду на вечную жизнь. Эту вечную жизнь еще до сотворения мира обещал Бог, Который никогда не лжет. 3И когда подошло назначенное время, Он явил Свое слово через проповедь, которая была доверена мне по повелению Бога – нашего Спасителя.

4Титу, моему истинному сыну по общей вере.

Благодать и мир тебе от Бога Отца и Иисуса Христа – нашего Спасителя.

Качества, необходимые духовному руководителю

5Я оставил тебя на Крите для того, чтобы ты довел до конца то, что было начато, и назначил по несколько старейшин в каждом городе, как я тебе велел. 6Руководитель должен быть человеком с безупречной репутацией, муж одной жены1:6 Муж одной жены – существует несколько толкований этого места: 1) имеющий только одну жену; 2) верный своей жене; 3) женатый не более одного раза.; его дети должны быть верующими и не вызывать упреков в распущенности или непослушании. 7Он должен быть безупречен, так как ему доверен труд Божий. Он не должен быть высокомерным, раздражительным, склонным к пьянству, драчуном, не должен преследовать корыстные цели. 8Наоборот, ему следует быть гостеприимным, любящим добро, благоразумным, справедливым, благочестивым, умеющим владеть собой человеком. 9Он должен быть верен слову истины, которому был научен, чтобы он мог наставлять других в здравом учении и опровергать тех, кто этому учению противится.

Действия по отношению к лжеучителям

10Есть много людей, особенно среди обрезанных1:10 То есть среди иудеев., которые не признают над собой власти, занимаются пустыми разговорами и обманывают других. 11Их надо заставлять молчать, потому что они ради низкой корысти губят целые семьи, уча тому, чему не следует. 12Даже один из них, их собственный пророк1:12 Здесь приводится цитата Эпименида Критского, жившего в VI – V вв. до н. э., поэта, которого почитали за пророка. сказал: «Критяне всегда лжецы, злобные звери, ленивые обжоры». 13И это верное свидетельство. Поэтому строго обличай их, чтобы их вера была здравой, 14чтобы они не обращали внимания на иудейские выдумки и приказания людей, отвернувшихся от истины. 15Для чистых все чисто, но для людей испорченных и неверующих нет ничего чистого, потому что их ум и совесть испорчены. 16Они заявляют, что знают Бога, но своими делами они отвергают Его. Они отвратительны, непослушны и бесполезны для всякого доброго дела.